< Yesaya 51 >

1 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
Poslušajte me koji idete za pravdom, koji tražite Gospoda; pogledajte stijenu iz koje ste isjeèeni, i duboku jamu iz koje ste iskopani;
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
Pogledajte Avrama, oca svojega, i Saru, koja vas je rodila, kako ga inokosna pozvah i blagoslovih ga i umnožih ga.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
Jer æe Gospod utješiti Sion, utješiæe sve razvaline njegove, i pustinju njegovu uèiniæe da bude kao Edem i pustoš njegova kao vrt Gospodnji, radost æe se i veselje nalaziti u njemu, zahvaljivanje i pjevanje.
4 “Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
Poslušaj me, narode moj, i èuj me, rode moj; jer æe zakon od mene izaæi i sud svoj postaviæu da bude vidjelo narodima.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
Blizu je pravda moja, izaæi æe spasenje moje, i mišice æe moje suditi narodima; mene æe ostrva èekati i u moju æe se mišicu uzdati.
6 Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
Podignite k nebu oèi svoje i pogledajte dolje na zemlju; jer æe nebesa išèeznuti kao dim i zemlja æe kao haljina ovetšati, i koji na njoj žive pomrijeæe takoðer; a spasenje æe moje ostati dovijeka, i pravde moje neæe nestati.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
Poslušajte me koji znate pravdu, narode, kojemu je u srcu zakon moj. Ne bojte se ruženja ljudskoga i od huljenja njihova ne plašite se.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
Jer æe ih moljac izjesti kao haljinu, i kao vunu izješæe ih crv; a pravda moja ostaje dovijeka i spasenje moje od koljena na koljeno.
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
Probudi se, probudi se, obuci se u silu, mišico Gospodnja; probudi se kao u staro vrijeme, za naraštaja prošlijeh; nijesi li ti isjekla Ravu i ranila zmaja?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
Nijesi li ti isušila more, vodu bezdana velikoga, od dubine morske naèinila put da proðu izbavljeni?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
Tako oni koje iskupi Gospod neka se vrate i doðu u Sion pjevajuæi, i veselje vjeèno neka bude nad glavom njihovom; radost i veselje neka zadobiju, a žalost i uzdisanje neka bježi.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
Ja, ja sam utješitelj vaš; ko si ti da se bojiš èovjeka smrtnoga i sina èovjeèijega, koji je kao trava?
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
I zaboravio si Boga tvorca svojega, koji je razapeo nebesa i osnovao zemlju? i jednako se bojiš svaki dan gnjeva onoga koji te pritješnjuje kad se sprema da zatire? a gdje je gnjev onoga koji pritješnjuje?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
Brzo æe se oprostiti sužanj, neæe umrijeti u jami, niti æe biti bez hljeba.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Jer sam ja Gospod Bog tvoj, koji raskidam more, da valovi njegovi buèe; Gospod nad vojskama ime mi je.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
Ja ti metnuh u usta rijeèi svoje i sjenom ruke svoje zaklonih te, da utvrdim nebesa i osnujem zemlju, i reèem Sionu: ti si moj narod.
17 Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
Probudi se, probudi se, ustani, Jerusalime! koji si pio iz ruke Gospodnje èašu gnjeva njegova, pio si, i talog iz strašne èaše ispio si.
18 Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
Od svijeh sinova koje je rodio nijedan ga nije vodio, i od svijeh sinova koje je othranio nijedan ga nije prihvatio za ruku.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
Ovo te dvoje zadesi; ko te požali? Pustoš i rasap, i glad i maè; ko æe te utješiti?
20 Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
Sinovi tvoji obamrli leže po krajevima svijeh ulica kao bivo u mreži puni gnjeva Gospodnjega, i karanja Boga tvojega.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
Zato èuj ovo, nevoljni, i pijani, ne od vina.
22 Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
Ovako veli Gospod tvoj, Gospod i Bog tvoj, koji brani svoj narod: evo uzimam iz tvoje ruke èašu strašnu, talog u èaši gnjeva svojega; neæeš više piti.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”
Nego æu je dati u ruke onima koji te muèe, koji govoriše duši tvojoj: sagni se da prijeðemo, i ti si im podmetao leða svoja da budu kao zemlja i kao ulica onima koji prelaze.

< Yesaya 51 >