< Yesaya 5 >

1 Ndidzamuyimbira bwenzi langa nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa: Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa pa phiri la nthaka yachonde.
Zapjevaæu sada dragome svojemu pjesmu dragoga svojega o vinogradu njegovu. Dragi moj ima vinograd na rodnu brdašcu.
2 Anatipula nachotsa miyala yonse ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri. Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo. Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino, koma ayi, unabala mphesa zosadya.
I ogradi ga, i otrijebi iz njega kamenje, i nasadi ga plemenitom lozom, i sazida kulu usred njega, i iskopa pivnicu u njemu, i poèeka da rodi grožðem, a on rodi vinjagom.
3 “Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda, weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.
Pa sada, stanovnici Jerusalimski i ljudi Judejci, sudite izmeðu mene i vinograda mojega.
4 Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa kupambana chomwe ndawuchitira kale? Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino, bwanji unabala mphesa zosadya?
Što je još trebalo èiniti vinogradu mojemu što mu ne uèinih? kad èekah da rodi grožðem, zašto rodi vinjagom?
5 Tsopano ndikuwuzani chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa: ndidzachotsa mpanda wake, ndipo mundawo udzawonongeka; ndidzagwetsa khoma lake, ndipo nyama zidzapondapondamo.
Sada æu vam kazati što æu uèiniti vinogradu svojemu. Oboriæu mu ogradu, neka opusti; razvaliæu mu zid, neka se pogazi;
6 Ndidzawusandutsa tsala, udzakhala wosatengulira ndi wosalimira ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina. Ndidzalamula mitambo kuti isagwetse mvula pa mundapo.”
Uparložiæu ga, neæe se rezati ni kopati, nego æe rasti èkalj i trnje, i zapovjediæu oblacima da ne puštaju više dažda na nj.
7 Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse ndi Aisraeli, ndipo anthu a ku Yuda ndiwo minda yake yomukondweretsa. Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana; mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.
Da, vinograd je Gospoda nad vojskama dom Izrailjev, i ljudi su Judejci mili sad njegov; on èeka sud, a gle nasilja, èeka pravdu, a gle vike.
8 Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba, ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda, mpaka mutalanda malo onse kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.
Teško onima koji sastavljaju kuæu s kuæom, i njivu na njivu nastavljaju, da veæ ne bude mjesta i vi sami ostanete u zemlji.
9 Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti, “Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja, nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.
Od Gospoda nad vojskama èuh: mnoge kuæe opustjeæe, u velikim i lijepijem neæe biti nikoga.
10 Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi, kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”
Jer æe deset rala vinograda dati jedan vat, i gomer sjemena daæe efu.
11 Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa nathamangira chakumwa choledzeretsa, amene amamwa mpaka usiku kufikira ataledzera kotheratu.
Teško onima koji rane, te idu na silovito piæe i ostaju do mraka dok ih vino raspali.
12 Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe, matambolini, zitoliro ndi vinyo, ndipo sasamala ntchito za Yehova, salemekeza ntchito za manja ake.
I na gozbama su im gusle i psaltiri i bubnji i svirale i vino; a ne gledaju na djela Gospodnja i ne vide rada ruku njegovijeh.
13 Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo chifukwa cha kusamvetsa zinthu; atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala, ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.
Zato se narod moj odvede u ropstvo što ne znaju, i koje poštuje gladuju, i ljudstvo njegovo gine od žeði.
14 Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake; mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka; adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko. (Sheol h7585)
Zato se raširio grob i razvalio ždrijelo svoje preveæ, i siæi æe u nj slava njegova i mnoštvo njegovo i vreva njegova i koji se vesele u njemu. (Sheol h7585)
15 Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa, anthu onse adzachepetsedwa, anthu odzikuza adzachita manyazi.
I pognuæe se prost èovjek, i visoki æe se poniziti, i ponosite oèi oboriæe se;
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama. Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.
Gospod nad vojskama uzvisiæe se sudom, i Bog sveti posvetiæe se pravdom.
17 Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo; ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.
I jaganjci æe pasti po svom obièaju, i došljaci æe jesti s pustijeh mjesta pretilinu.
18 Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo, ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,
Teško onima koji vuku bezakonje uzicama od taštine, i grijeh kao užem kolskim,
19 amene amanena kuti, “Yehova afulumire, agwire ntchito yake mwamsanga kuti ntchitoyo tiyione. Ntchito zionekere, zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita, zichitike kuti tizione.”
Koji govore: neka pohiti, neka brzo doðe djelo njegovo, da vidimo, i neka se približi i doðe što je naumio svetac Izrailjev, da poznamo.
20 Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino ndipo zabwino amaziyesa zoyipa, amene mdima amawuyesa kuwala ndipo kuwala amakuyesa mdima, amene zowawasa amaziyesa zotsekemera ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.
Teško onima koji zlo zovu dobro, a dobro zlo, koji prave od mraka svjetlost a od svjetlosti mrak, koji prave od gorkoga slatko a od slatkoga gorko.
21 Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera.
Teško onima koji misle da su mudri, i sami su sebi razumni.
22 Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,
Teško onima koji su jaki piti vino i junaci u miješanju silovita piæa.
23 amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.
Koji pravdaju bezbožnika za poklon, a pravednima uzimaju pravdu.
24 Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto, momwemonso mizu yawo idzawola ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi; chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse, ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.
Zato kao što oganj proždire strnjiku i slame nestaje u plamenu, tako æe korijen njihov biti kao trulež i cvijet njihov otiæi æe kao prah, jer odbaciše zakon Gospoda nad vojskama i prezreše rijeè sveca Izrailjeva.
25 Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake; watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha Mapiri akugwedezeka, ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala. Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke, dzanja lake likanali chitambasulire;
Zato se raspali gnjev Gospodnji na narod njegov, i mahnuv rukom svojom na nj udari ga da se gore zadrmaše i mrtva tjelesa njegova biše kao blato po ulicama. Kod svega toga gnjev se njegov ne odvrati, nego je ruka njegova još podignuta.
26 Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali, akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi. Awo akubwera, akubweradi mofulumira kwambiri!
I podignuæe zastavu narodima daljnijem, i zazviždaæe im s kraja zemlje; i gle, oni æe doæi odmah, brzo.
27 Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa, palibe amene akusinza kapena kugona; palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka, palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.
Neæe biti meðu njima umorna ni sustala, ni dremljiva ni sanljiva, nikome se neæe raspasati pojas oko njega, niti æe se kome otkinuti remen na obuæi.
28 Mivi yawo ndi yakuthwa, mauta awo onse ndi okoka, ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi, magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.
Strijele æe im biti oštre, i svi lukovi njihovi zapeti; kopita u konja njihovijeh biæe kao kremen i toèkovi njihovi kao vihor.
29 Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango, amabangula ngati misona ya mkango; imadzuma pamene ikugwira nyama ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.
Rika æe im biti kao u lava, i rikaæe kao laviæi; buèaæe i ugrabiæe plijen i odnijeti ga, i neæe biti nikoga da otme.
30 Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja. Ndipo wina akakayangʼana dzikolo adzangoona mdima ndi zovuta; ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.
Buèaæe nad njim u to vrijeme kao što more buèi. Tada æe pogledati na zemlju, a to mrak i strah, i svjetlost æe se pomraèiti nad pogiblju njihovom.

< Yesaya 5 >