< Yesaya 46 >

1 Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
Ugiął się Bel, chyli się Nebo. Ich posągi włożono na zwierzęta i bydło, które będąc obciążone, zmęczyły się pod brzemieniem.
2 Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
Pochyliły się i ugięły się razem; nie mogły ratować brzemion, ale one same poszły w niewolę.
3 Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
Słuchajcie mnie, domu Jakuba i cała resztko domu Izraela, których noszę od łona, których piastuję od urodzenia:
4 Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
Aż do waszej starości ja jestem ten sam i aż do siwizny będę was nosić. Ja was uczyniłem, ja też nosić będę; ja mówię, będę was nosił i was wybawię.
5 “Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
Do kogo mnie porównacie i z kim mnie zestawicie albo do kogo uczynicie [mnie] podobnym, abyśmy byli sobie równi?
6 Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
Wysypują złoto z worka i odważają srebro na szalach, najmują złotnika, aby uczynił z nich bożka, przed którym padają i [któremu] oddają pokłon.
7 Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
Noszą go na ramieniu, dźwigają go i stawiają go na swoim miejscu. I stoi, nie ruszy się ze swego miejsca. Jeśli ktoś zawoła do niego, nie odzywa się ani go nie wybawia z jego utrapienia.
8 “Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
Pamiętajcie o tym i wstydźcie się, weźcie to sobie do serca, przestępcy!
9 Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
Wspomnijcie rzeczy dawne i odwieczne, bo ja jestem Bogiem, nie ma żadnego innego, [jestem] Bogiem i nie ma nikogo [podobnego] do mnie;
10 Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
Zapowiadam od początku rzeczy ostatnie i od dawna to, czego jeszcze nie było. Mówię: Mój zamiar się spełni i wykonam całą swoją wolę.
11 Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
Przywołuję ze wschodu ptaka drapieżnego, z dalekiej ziemi mężczyznę, który wykonuje moją radę. Powiedziałem i wykonam to, postanowiłem i uczynię to.
12 Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
Słuchajcie mnie, wy, twardego serca, którzy jesteście dalecy od sprawiedliwości.
13 Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.
Zbliżę moją sprawiedliwość, nie będzie [ona] daleko, a moje zbawienie nie odwlecze się. I położę w Syjonie zbawienie, a w Izraelu moją chwałę.

< Yesaya 46 >