< Yesaya 37 >

1 Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
A gdy król Ezechiasz to usłyszał, rozdarł swoje szaty, oblekł się w wór i wszedł do domu PANA.
2 Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
I posłał Eliakima, przełożonego swego domu, pisarza Szebnę i starszych spośród kapłanów, obleczonych w wory, do proroka Izajasza, syna Amosa.
3 Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’
I powiedzieli mu: Tak mówi Ezechiasz: Ten dzień jest dniem utrapienia, upomnienia i bluźnierstwa. Nadszedł bowiem czas porodu dzieci, a nie ma siły, aby je urodzić.
4 Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”
Może PAN, twój Bóg, usłyszy słowa Rabszaka, którego przysłał król Asyrii, jego pan, aby znieważać Boga żywego, i pomści słowa, które usłyszał PAN, twój Bóg. Zanieś więc modlitwę za resztkę, która pozostaje.
5 Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
Tak to słudzy króla Ezechiasza przyszli do Izajasza.
6 Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
A Izajasz im odpowiedział: Tak powiedzcie waszemu panu: Tak mówi PAN: Nie bój się tych słów, które słyszałeś, którymi bluźnili mi słudzy króla Asyrii.
7 Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
Oto ześlę na niego ducha i usłyszy [pewną] wieść, [a potem] wróci do swojej ziemi i sprawię, że padnie od miecza w swojej ziemi.
8 Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
Wrócił więc Rabszak i zastał króla Asyrii walczącego przeciwko Libnie. Usłyszał bowiem, że odstąpił od Lakisz.
9 Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
A dotarło do niego, że mówiono o Tirhace, królu Etiopii: Oto wyruszył na wojnę przeciwko tobie. Gdy to usłyszał, wysłał posłańców do Ezechiasza z tymi słowami:
10 “Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
Tak powiedzcie Ezechiaszowi, królowi Judy: Niech cię nie zwodzi twój Bóg, któremu ufasz, mówiąc: Jerozolima nie zostanie wydana w ręce króla Asyrii.
11 Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka?
Oto słyszałeś, co uczynili królowie Asyrii wszystkim ziemiom, niszcząc je. A ty miałbyś zostać wybawiony?
12 Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi?
Czy bogowie narodów wybawili tych, których moi ojcowie wygubili: Gozan, Charan, Resef i synów Edenu, którzy byli w Telassar?
13 Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”
Gdzie jest król Chamatu, król Arpadu i król miasta Sefarwaim, Heny i Iwwy?
14 Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova.
Gdy Ezechiasz wziął list z rąk posłów, przeczytał go, wszedł do domu PANA i rozwinął go przed PANEM.
15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova:
I Ezechiasz modlił się do PANA, mówiąc:
16 “Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
PANIE zastępów, Boże Izraela, który zasiadasz pomiędzy cherubinami, ty, ty jedynie jesteś Bogiem wszystkich królestw ziemi, ty stworzyłeś niebo i ziemię.
17 Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.
Nakłoń swego ucha, PANIE, i słuchaj. Otwórz swe oczy, PANIE, i spójrz. Słuchaj wszystkich słów Sennacheryba, które przesłał, aby znieważać Boga żywego.
18 “Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo.
To prawda, PANIE, że królowie Asyrii spustoszyli wszystkie narody i ich ziemie;
19 Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu.
I powrzucali ich bogów do ognia. Nie byli bowiem bogami, ale dziełem rąk ludzkich, drewnem i kamieniem. Dlatego ich zniszczyli.
20 Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”
Teraz więc, PANIE, nasz Boże, wybaw nas z jego ręki, aby wszystkie królestwa ziemi poznały, że jedynie ty jesteś PANEM.
21 Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.
Wtedy Izajasz, syn Amosa, posłał [wiadomość] do Ezechiasza: Tak mówi PAN, Bóg Izraela: Ponieważ modliłeś się do mnie w sprawie Sennacheryba, króla Asyrii;
22 Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa: “Mwana wamkazi wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka. Mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
Oto słowo, które PAN o nim wypowiedział: Dziewica, córka Syjonu, wzgardziła tobą i śmiała się z ciebie. Córka Jerozolimy kiwała głową za tobą.
23 Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani? Kodi iwe wafuwulira ndi kumuyangʼana monyada ndani? Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
Kogo znieważyłeś i komu bluźniłeś? Przeciwko komu podniosłeś swój głos i wysoko podniosłeś swoje oczy? Przeciwko Świętemu Izraela.
24 Kudzera mwa amithenga ako iwe wanyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta anga ochuluka ndafika pamwamba pa mapiri, pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni. Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri, ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini. Ndafika pa msonga pake penipeni, nkhalango yake yowirira kwambiri.
Przez swoje sługi znieważyłeś Pana i powiedziałeś: Z mnóstwem swoich rydwanów wyszedłem na wysokie góry i zbocza Libanu. Wytnę jego wysokie cedry i jego wyborowe cyprysy i przyjdę aż do najwyższego jego szczytu, do lasów i do lasu jego pola.
25 Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndi kumva madzi akumeneko ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’
Ja wykopałem studnie i piłem wody, swoimi stopami wysuszyłem wszystkie rzeki oblężonych miejsc.
26 “Kodi sunamvepo kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale? Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndazichitadi, kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
Czy nie słyszałeś, że ja dawno to uczyniłem i za dawnych dni to sprawiłem? A teraz wypełniam, gdy obracasz warowne miasta w stosy gruzów.
27 Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu, ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi. Anali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu omera pa denga, umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.
Ich mieszkańcy, bezsilni, przestraszyli się i zawstydzili. Byli jak trawa polna, jak świeża zieleń, jak trawa na dachach, jak [zboże], które uschło, zanim dojrzało.
28 “Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe; ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa, ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
Znam twoje miejsce pobytu, twoje wyjście i twoje wejście, a także twoją wściekłość przeciwko mnie.
29 Chifukwa umandikwiyira Ine ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa njira yomwe unadzera pobwera.
Ponieważ twoja wściekłość na mnie i twoja zuchwałość doszły do moich uszu, włożę moje kółko w twoje nozdrza i moje wędzidło na twoje wargi i zawrócę cię tą drogą, którą przyszedłeś.
30 “Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
A to będzie znakiem dla ciebie: Tego roku będziesz jadł zboże samorodne, w drugim roku także zboże samorodne, w trzecim roku zaś siejcie i zbierajcie żniwo, sadźcie winnice i jedzcie ich owoce.
31 Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
Resztka ocalonych z domu Judy ponownie zapuści korzenie w głąb i wyda owoc w górze.
32 Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka. Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
Z Jerozolimy wyjdą bowiem resztka i ci, którzy ocaleli z góry Syjon. Sprawi to gorliwość PANA zastępów.
33 “Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya: “Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi uliwonse. Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
Dlatego tak mówi PAN o królu Asyrii: Nie wejdzie do tego miasta ani nie wypuści tam strzały, nie wyruszy przeciw niemu z tarczą ani nie usypie szańców przeciwko niemu.
34 Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu,” akutero Yehova.
Drogą, którą przyszedł, powróci, a do tego miasta nie wejdzie, mówi PAN.
35 “Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”
Będę bowiem bronił tego miasta i ocalę je ze względu na siebie i ze względu na Dawida, swego sługę.
36 Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse!
Wtedy wyszedł Anioł PANA i zabił w obozie Asyrii sto osiemdziesiąt pięć tysięcy [osób]. A gdy wstali wcześnie rano, oto wszędzie [było] pełno trupów.
37 Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.
Sennacheryb, król Asyrii, wycofał się więc i wyruszył. Wrócił i zamieszkał w Niniwie.
38 Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.
A gdy oddawał pokłon w domu swego boga Nisroka, jego synowie – Adramelek i Sareser – zabili go mieczem. Potem uciekli do ziemi Ararat. I Asarchaddon, jego syn, królował w jego miejsce.

< Yesaya 37 >