< Yesaya 34 >

1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Pristupite, narodi, da èujete; pazite, narodi; neka èuje zemlja i što je u njoj, vasiljena i što se god raða u njoj.
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
Jer se Gospod razgnjevio na sve narode, i razljutio se na svu vojsku njihovu, zatræe ih, predaæe ih na pokolj.
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
I pobijeni njihovi baciæe se, i od mrtvaca njihovijeh dizaæe se smrad i gore æe se rasplinuti od krvi njihove.
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
I sva æe se vojska nebeska rastopiti, i saviæe se nebesa kao knjiga, i sva vojska njihova popadaæe kao što pada list s vinove loze i kao što pada sa smokve.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
Jer je opojen na nebu maè moj, evo, siæi æe na sud na Edomce i na narod koji sam prokleo da se zatre.
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
Maè je Gospodnji pun krvi i tovan od pretiline, od krvi jagnjeæe i jarèije, od pretiline bubrega ovnujskih; jer Gospod ima žrtvu u Vosoru i veliko klanje u zemlji Edomskoj.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
I jednorozi æe siæi s njima i junci s bikovima; zemlja æe se njihova opiti od krvi i prah æe njihov utiti od pretiline.
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
Jer æe biti dan osvete Gospodnje, godina plaæanja, da bi se osvetio Sion.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
I potoci æe se njezini pretvoriti u smolu, i prah njezin u sumpor, i zemlja æe njihova postati smola razgorjela.
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
Neæe se gasiti ni noæu ni danju, dovijeka æe se dizati dim njezin, od koljena do koljena ostaæe pusta, niko neæe prelaziti preko nje dovijeka.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
Nego æe je naslijediti gem i æuk, sova i gavran naseliæe se u njoj, i Gospod æe rastegnuti preko nje uže pogibli i mjerila pustoši.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
Plemiæe njezine zvaæe da caruju, ali neæe biti nijednoga, i svi æe knezovi njezini otiæi u ništa.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
I trnje æe izniknuti u dvorima njihovijem, kopriva i èkalj u gradovima njihovijem, i biæe stan zmajevima i naselje sovama.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
I sretaæe se divlje zvijeri s buljinama, aveti æe se dovikivati, ondje æe se naseliti vještice i naæi poèivalište.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
Ondje æe se gnijezditi æuk i nositi jaja i leæi ptiæe i sabirati ih pod sjen svoj; ondje æe se sastajati i jastrebovi jedan s drugim.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
Tražite u knjizi Gospodnjoj i èitajte, ništa od ovoga neæe izostati i nijedno neæe biti bez drugoga; jer što kažem, on je zapovjedio, i duh æe ih njegov sabrati.
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
Jer im on baci ždrijeb, i ruka njegova razdijeli im zemlju užem, i njihova æe biti dovijeka, od koljena do koljena nastavaæe u njoj.

< Yesaya 34 >