< Yesaya 31 >

1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Teško onima koji idu u Misir za pomoæ, koji se oslanjaju na konje, i uzdaju se u kola što ih je mnogo, i u konjike što ih je veliko mnoštvo, a ne gledaju na sveca Izrailjeva i ne traže Gospoda.
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
Ali je i on mudar, i navuæi æe zlo, i neæe poreæi svoje rijeèi, nego æe ustati na dom nevaljalijeh ljudi i na one koji pomažu onima koji èine bezakonje.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
A Misirci su ljudi a ne Bog, i konji su njihovi tijelo a ne duh; i zato æe Gospod mahnuti rukom svojom, te æe pasti pomagaè, pašæe i onaj kome pomaže, i svi æe zajedno poginuti.
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
Jer ovako mi reèe Gospod: kao što lav i laviæ rièe nad lovom svojim, i ako se i svièe na nj mnoštvo pastira, on se ne plaši od vike njihove niti se pokorava na buku njihovu, tako æe Gospod nad vojskama siæi da vojuje za goru Sionsku i za hum njezin.
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
Kao ptice krilima Gospod æe nad vojskama zaklanjati Jerusalim, i zaklanjajuæi izbaviæe, i oblazeæi saèuvaæe.
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
Vratite se k njemu, od kojega se sasvijem odvrgoste, sinovi Izrailjevi!
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
Jer æe u onaj dan svaki odbaciti idole svoje srebrne, i zlatne svoje idole, koje vam ruke vaše naèiniše na grijeh.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
I Asirac æe pasti od maèa ne èovjeèijega, i maè ne èovjeèji poješæe ga, i bježaæe ispred maèa, i mladiæi æe njegovi plaæati danak.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
I stijena æe njegova proæi od straha, i knezovi æe se njegovi prepasti od zastave, veli Gospod, èiji je oganj na Sionu i peæ u Jerusalimu.

< Yesaya 31 >