< Yesaya 24 >

1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Some day, Yahweh is going to destroy everything on the earth. He will devastate it and cause it to become a desert and scatter its people.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
He will scatter everyone— priests and common people, servants and their masters, maids and their mistresses, buyers and sellers, lenders and borrowers, people who owe money and people who are owed money.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
Nothing that is worth anything will be left on earth; everything valuable will be destroyed. [That will surely happen because] Yahweh has said it.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
[Everything on] the earth will dry up and die [DOU]; its important people will become weak and unimportant.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
The earth has become unacceptable to Yahweh because the people who live on it have disobeyed his laws; they have rejected the agreement that he intended to last forever.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
Therefore, [Yahweh] will curse the earth; the people who live on it must be punished because of the sins that they have committed. They will be destroyed by fire, and [only a] few people will remain [alive].
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
The grapevines will wither, and there will be no [grapes to make] wine. All [the people] who were previously happy will then groan and mourn.
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
People will no longer play cheerful songs with tambourines, people will no longer play joyfully on their harps, and people will no longer shout noisily [during their celebrations].
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
People will no longer sing while they drink wine, and [all] their alcoholic drinks will taste bitter.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
[Towns and] cities will be desolate; every house will be locked to prevent thieves from entering.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
[Mobs] will gather in the streets, wanting wine; no one on the earth will be happy [DOU] any more.
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
Cities will be ruined and [all] their gates will be battered/broken into pieces.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
It will be like that all over the earth: [there will only be a few people still alive], like what happens when [workers] beat all the olives off a tree [and there are only a few left], [or] when they harvest the grapes and there are only a few left [on the vines].
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
But [those who are left alive] will sing joyfully; people [in nations] to the west [of Israel] will declare that Yahweh is very great;
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
people in nations to the east [of Israel will also] praise Yahweh [MTY]; in countries across the sea, people will praise Yahweh, the God whom we Israelis [worship].
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
We will hear [people] in the most distant places on the earth singing praise to [Yahweh], the [truly] righteous one. But [now], I am [SYN] very sad. Weep for me, [because] I have become thin and weak. Terrible things are happening! Treacherous [people still] betray/deceive others everywhere [DOU].
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
You people all over the earth, you will be terrified, and you will fall into deep pits and traps/snares.
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
Those who [try to] flee because they are terrified will fall into [deep] pits, and those who climb out of the pits will be caught by traps/snares. The sky will split open and torrents [SIM] [of rain will fall]; the foundations of the earth will shake.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
The earth will split apart and be shattered; it will shake violently.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
[It will be as though] the earth will stagger like [SIM] a drunk; it will shake like [SIM] a hut [shakes in a windstorm]. It will collapse and not [be able to] rise again, [because] the guilt of the people who rebel [against Yahweh] is very great.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
At that time, Yahweh will punish the [wicked] powerful beings in the skies and the wicked kings on the earth.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
They will [all] be gathered together and thrown into a dungeon/pit. They will be shut/locked in that dungeon/pit, and later they will be punished.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
At that time the light of the moon and the sun will be lessened; [it will be as though] they are ashamed [in the presence of] Yahweh, because he, the Commander of the armies of angels, will rule gloriously (on Zion Hill/in Jerusalem), in the presence of the leaders [of his people].

< Yesaya 24 >