< Yesaya 24 >

1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Lo! Yahweh emptying the earth and laying it waste, —And he will overturn the face thereof, And scatter them who dwell therein.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
And it shall be—As the people, so, the priest, As the servant, so his lord, As the maid, so, her mistress, —As the buyer, so, the seller, As the lender, so, the borrower, As the debtor, so! his creditor.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
Emptied—emptied—shall be the earth yea pillaged—pillaged, —For, Yahweh, hath spoken this word.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
Mourneth, fadeth, the earth Languisheth, fadeth, the world, —Languished have the lofty of the people of the earth.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
Yea the earth itself is profaned under them who dwell therein, —For they have Set aside laws, Gone beyond statute, Broken an age-abiding covenant.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
For this cause, a curse, hath devoured the earth, And punished are the dwellers therein, —For this cause, are burned the inhabitants of the earth, And the men left remaining—are few.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
Mourneth the new wine. Withereth the vine, —Sighing are all the merryhearted:
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
Ceased hath the mirth of timbrels, Ended is the noise of the uproarious, —Ceased hath the mirth of the lyre:
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
With a song, they drink not wine, —Bitter is strong drink, to them who drink it:
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
Broken down is the city of desolation, —Shut up every house that it cannot be entered.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
There is an outcry concerning wine in the streets, —Darkened is all joy, Departed the gladness of the earth.
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
There is left in the city. desolation, —And to ruins, have been broken the gate.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
When, thus, it shall be in the earth in the midst of the peoples, [There shall be] like the shaking of an olive-tree, like the going round to pick when closed is the harvest.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
They, shall lift up their voice—shall raise a tremulous note, —On account of the splendour of Yahweh, have they made a shrill cry, on the West;
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
For this cause, In the Regions of Light, give ye glory to Yahweh, —In the Coastlands of the Sea, unto the Name of Yahweh. God of Israel,
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
From the uttermost part of the earth, melodies, have we heard—Beauty, to the righteous one! But I had said—Ruin to me! Ruin to me! Woe to me! Traitors, have betrayed, Yea traitorously, have traitors betrayed!
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
Terror and pit and snare, —are upon thee, O inhabitant of the earth!
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
So shall it be—He that fleeth from the sound of the terror! shall fall into the pit, And, he that getteth up out of the midst of the pit, shall be captured in the snare, —For, the windows on high, have opened, And shaken are the foundations of earth.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
The earth breaketh, breaketh, —The earth crasheth, crasheth, The earth tottereth, tottereth;
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
The earth staggereth—staggereth like a drunken man, And rocketh to and fro like a night-hut, —So shall be heavy upon her, her transgression, And she shall fall and not again rise.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
And it shall be in that day, That Yahweh will bring punishment Upon the host of the height in the height, —And upon the kings of the ground on the ground.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
And they shall be swept together in a crowd, fettered for a pit, And shall be lowered into a dungeon, —And, after many days, shall they be punished.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Then shall blush the silvery moon, Then turn pale the glowing sun, —Because Yahweh of hosts hath become king In Mount Zion And in Jerusalem, And before his Elders in glory,

< Yesaya 24 >