< Yesaya 24 >

1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Look, the LORD makes the earth empty, makes it waste, turns it upside down, and scatters its inhabitants.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
It will be as with the people, so with the priest; as with the servant, so with his master; as with the maid, so with her mistress; as with the buyer, so with the seller; as with the creditor, so with the debtor; as with the taker of interest, so with the giver of interest.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
The earth will be utterly emptied and utterly laid waste; for the LORD has spoken this word.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
The earth mourns and fades away. The world languishes and fades away. The lofty people of the earth languish.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
The earth also is polluted under its inhabitants, because they have transgressed the law, violated the statute, and broken the everlasting covenant.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
Therefore the curse has devoured the earth, and those who dwell in it are found guilty. Therefore the inhabitants of the earth are burned, and few men left.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
The new wine mourns. The vine languishes. All the merry-hearted sigh.
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
The mirth of tambourines ceases. The sound of those who rejoice ends. The joy of the harp ceases.
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
They will not drink wine with a song. Strong drink will be bitter to those who drink it.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
The confused city is broken down. Every house is shut up, that no man may come in.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
There is a crying in the streets because of the wine. All joy is darkened. The mirth of the land is gone.
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
The city is left in desolation, and the gate is struck with destruction.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
For it will be so in the midst of the earth among the peoples, as the shaking of an olive tree, as the gleanings when the vintage is done.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
These shall lift up their voice. They will shout for the majesty of the LORD. They cry aloud from the sea.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
Therefore glorify the LORD in the east, even the name of the LORD, the God of Israel, in the islands of the sea.
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
From the uttermost part of the earth have we heard songs. Glory to the righteous. But I said, "I pine away. I pine away. Woe is me." The treacherous have dealt treacherously. Yes, the treacherous have dealt very treacherously.
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
Fear, the pit, and the snare, are on you who inhabitant the earth.
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
It will happen that he who flees from the noise of the fear will fall into the pit; and he who comes up out of the midst of the pit will be taken in the snare; for the windows of heaven are opened, and the foundations of the earth tremble.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
The earth is utterly broken. The earth is torn apart. The earth is shaken violently.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
The earth will stagger like a drunken man, and will sway back and forth like a hammock. Its disobedience will be heavy on it, and it will fall and not rise again.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
It shall happen in that day that the LORD will punish the army of the high ones on high, and the kings of the earth on the earth.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
And they will be gathered, a gathering in a dungeon, and shall be shut up in the prison; and after many days shall they be visited.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Then the moon shall be confounded, and the sun ashamed, for the LORD of hosts will reign on Mount Zion and in Jerusalem, and before his elders will be glory.

< Yesaya 24 >