< Yesaya 24 >

1 Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi ndi kulisandutsa chipululu; Iye adzasakaza maonekedwe ake ndi kumwaza anthu ake onse.
Hina Gode da liligi huluane mugululi, osobo bagade da gugunufinisi dagoi ba: mu. E da soge bagade wadela: mu amola fifi asi gala dunu huluane afafane, sefasimu.
2 Aliyense zidzamuchitikira mofanana: wansembe chimodzimodzi munthu wamba, antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna, antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi, wogula chimodzimodzi wogulitsa, wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa, okongola chimodzimodzi okongoza.
Dunu huluane, amo gobele salasu dunu, dunudafa, udigili hawa: hamosu dunu, ilia ouligisu dunu, bidiga lama: ne dunu, fa: no dabema: ne muni iasu dunu, bu ima: ne muni lasu dunu, bagade gagui dunu amola hame gagui dunu, amo huluane da defele se lamu.
3 Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu ndi kusakazikiratu. Yehova wanena mawu awa.
Osobo bagade da goudane, wadela: lesi dagoi ba: mu. Hina Gode da amane sia: i dagoi, amola Ea sia: i liligi da hamoi dagoi ba: mu.
4 Dziko lapansi likulira ndipo likufota, dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma, anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.
Osobo da hafoga: sa, amola gisi amola ifa da biosa. Osobo bagade huluane da gasa hame agoane ba: sa. Osobo bagade amola mu da dasasa.
5 Anthu ayipitsa dziko lapansi; posamvera malangizo ake; pophwanya mawu ake ndi pangano lake lamuyaya.
Osobo bagade fifi asi gala da osobo bagade ledo hamone wadela: lesi dagoi. Bai ilia Gode Ea Sema fi dagoi amola gousa: su amo Gode da eso huluane dialoma: ne hamoi, ilia da wadela: lesi dagoi.
6 Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi; anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo, iwo asakazika ndipo atsala ochepa okha.
Amaiba: le, Gode da osobo bagade amoma gagabusu aligi dagoi. Osobo bagade dunu, ilia wadela: i hamobeba: le, wali dabe laha. Wali bagahame esalebe ba: sa. Aya bagahamedafa esalebe ba: mu.
7 Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota; onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.
Waini efe da biolala amola waini hano fonobahadi fawane gala. Dunu da musa: hahawane esalu da wali da: i dioiwane esalebe ba: sa.
8 Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha, phokoso la anthu osangalala latha, zeze wosangalatsa wati zii.
Ilia ‘sani baidama’ amola ilibu dusu da ouiya: i dagoi.
9 Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo; akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.
Waini hano nabeba: le, dunu ilia musa: hahawane gesami hame hea: su. Be wali waini hano da ilima hedai hame ba: sa.
10 Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka; nyumba iliyonse yatsekedwa.
Moilai amo ganodini, bidi hamosu fawane gala. Dunu da beda: iba: le, ilia diasu ganodini golili sa: ili, logo ga: sili, gagili sala.
11 Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo; chimwemwe chonse chatheratu, palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.
Waini hano da ebeleiba: le, dunu da logoga bagade halasa. Hahawane hou da fisi dagoi. Fedege agoane, hahawane hou da gadili sefasi dagoi.
12 Mzinda wasanduka bwinja zipata zake zagumuka.
Moilai bai bagade da mugului dagoi amola ea logo ga: su da wadela: lesi dagoi.
13 Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi ndiponso pakati pa mitundu ya anthu. Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa, kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.
Amo hou da osobo bagade fifi asi gala huluanedafa amo ganodini ba: mu. Amo eso da ha: i manu gamisu eso da dagoi agoane ba: mu. Olife fage da olife ifa amoga fai dagoi amola waini fage amo waini efe amoga fai agoaiwane ba: mu.
14 Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe; anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.
Be nowa da mae bogole esalebe ba: sea, da hahawaneba: le gesami hea: mu. Dunu da eso dabe la: idi sogega esalea, da Hina Gode Ea gasa bagade hou olelemu.
15 Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova; ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.
Amola dunu da gusudili esalea, da Godema nodomu. Dunu amo da hano wayabo bagade amo ea bega: esala da Isala: ili ilia Hina Gode, Ema nodomu.
16 Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda “Wolungamayo.” Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu! Tsoka kwa ine! Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo, inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”
Osobo bagade ganodini, sedaga esalebe fi da moloidafa hamosu fi amo Isala: ili, ilima nodone sia: mu. Be na dafawane esaloma: beyale dawa: lusu da fisi dagoi. Na da: i da geloga: le, wadela: sa. Hohonosu dunu da hohonana, amola ilia da bu baligili agoane hohonana.
17 Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje ndi msampha zikukudikirani.
Dunu huluane! Na sia: nabima! Beda: ma: ne liligi, amola sani amola sani uli dogoi da dili wadela: musa: dialebe.
18 Aliyense wothawa phokoso la zoopsa adzagwa mʼdzenje; ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo adzakodwa ndi msampha. Zitseko zakumwamba zatsekulidwa, ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.
Nowa da beda: ma: ne liligi amoga hobeale ahoasea, da sani uli dogoi amoga sa: imu. Amola nowa da ulidogoi amo ganodini hame dasea, da saniga sa: imu. Gibu bagadedafa, hano nawa: li agoane da muagado sa: imu. Osobo bagade ea bai da yagugumu.
19 Dziko lapansi lathyokathyoka, ndipo lagawika pakati, dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.
Osobo bagade da fili, goudane gugunufinisimu.
20 Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba; lalemedwa ndi machimo ake. Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.
Osobo bagade da adini ba: i dunu defele, feloale masunu, amola diasu foga fabeba: le yagugusa, agoane yagugumu. Wadela: i hou da dioi bagadeba: le, osobo bagade banenesisa. Osobo bagade da dafane, bu hamedafa wa: legadomu.
21 Tsiku limenelo Yehova adzalanga amphamvu a kumwamba ndiponso mafumu apansi pano.
Eso da misunu, amoga Hina Gode da wadela: i ouligisu a: silibu muagado esala, ilima se imunu. Amola E da osobo bagade ouligisu dunu ilima se imunu.
22 Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi ngati amʼndende amene ali mʼdzenje. Adzawatsekera mʼndende ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.
Gode da osobo bagade hina bagade dunu amo guba: le gilisili, ilia da se iasu diasu hamosu dunu uli dogoi ganodini gilisi agoane ba: mu. E da ili se iasu diasu ganodini salimu. Amasea, ilima dabe imunu eso da doaga: sea, E da ilima se imunu.
23 Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi; pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira; pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu, ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.
Oubi da bu gasi agoane ba: mu, amola eso da hame diga: mu. Bai Hina Gode Bagade da Hinadafa esalumu. E da Yelusaleme amo ganodini, Saione Goumi da: iya Hinadafa esalumu. Amola Ea fi ouligisu dunu da Ea hadigi ba: mu.

< Yesaya 24 >