< Yesaya 21 >

1 Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
Breme pustinji na moru. Kao vihori koji prolaze na jug, tako æe doæi iz pustinje, iz zemlje strašne.
2 Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
Ljuta utvara javi mi se. Nevjernik nevjeru èini, pustošnik pustoši; hodi, Elame; opkoli, Midijo! svemu uzdisanju uèiniæu kraj.
3 Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
Zato su bedra moja puna bola; muke me obuzeše kao kad se muèi porodilja; zgurih se èujuæi, prepadoh se videæi.
4 Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
Srce mi se smete, groza me poduze; noæ milina mojih pretvori mi se u strah.
5 Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
Postavi sto, stražar neka straži; jedi, pij; ustajte knezovi, mažite štitove.
6 Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
Jer ovako mi reèe Gospod: idi, postavi stražara da ti javi što vidi.
7 Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
I vidje kola, i dva reda konjika; kola s magarcima i kola s kamilama; i pažaše dobro velikom pažnjom.
8 Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
I povika kao lav: gospodaru, ja stojim jednako na straži danju, i stojim na straži po svu noæ.
9 Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
I evo doðoše na kolima ljudi, u dva reda konjici. Tada povika i reèe: pade, pade Vavilon, i svi rezani likovi bogova njegovijeh razbiše se o zemlju.
10 Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
Vršaju moj, i pšenice gumna mojega! što èuh od Gospoda nad vojskama, Boga Izrailjeva, javih vam.
11 Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
Breme Dumi. Vièe k meni neko sa Sira: stražaru! šta bi noæas? stražaru! šta bi noæas?
12 Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
Stražar reèe: doæi æe jutro, ali i noæ; ako æete tražiti, tražite, vratite se, doðite.
13 Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
Breme Arapskoj. Po šumama u Arapskoj noæivaæete, putnici Dedanski!
14 perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
Iznesite vode pred žedne, koji živite u zemlji Temi, sretite s hljebom bjegunca.
15 Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
Jer æe bježati od maèa, od maèa gologa, od luka zapetoga i od žestokoga boja.
16 Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
Jer ovako mi reèe Gospod: za godinu, kao što je godina najamnièka, nestaæe sve slave Kidarske.
17 Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.
I što ostane hrabrijeh strijelaca sinova Kidarskih, biæe malo; jer Gospod Bog Izrailjev reèe.

< Yesaya 21 >