< Yesaya 20 >

1 Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda,
W roku, w którym Tartan przybył do Aszdodu, wysłany tam przez Sargona, króla Asyrii, walczył przeciw Aszdodu i go zdobył;
2 nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.
W tym czasie PAN powiedział przez Izajasza, syna Amosa: Idź, zdejmij wór ze swych bioder i obuwie ze swoich nóg. I uczynił tak, chodząc nago i boso.
3 Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi,
I PAN powiedział: Jak mój sługa Izajasz chodzi nago i boso przez trzy lata jako znak i cud dla Egiptu i Etiopii;
4 momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto.
Tak król Asyrii uprowadzi więźniów Egiptu i jeńców Etiopii, młodych i starych, nagich i bosych, z obnażonymi pośladkami, na pohańbienie Egiptu.
5 Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi.
I przestraszą się, i zawstydzą z powodu Etiopii, ich nadziei, i z powodu Egiptu, ich chluby.
6 Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’”
Tego dnia mieszkaniec tej wyspy powie: Oto co się stało z naszą nadzieją, do której uciekliśmy się o pomoc, abyśmy zostali wyzwoleni od króla Asyrii. A teraz jak zdołamy ujść cało?

< Yesaya 20 >