< Yesaya 15 >

1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Breme Moavu. Da, obnoæ se raskopa Ar Moavski i propade; da, obnoæ se raskopa Kir Moavski i propade.
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
Otide u dom i u Devon, na visine, da plaèe: Moav æe ridati za Nevonom i za Medevom, sve æe mu glave biti æelave, svaka brada oskubena.
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
Po ulicama æe njegovijem pripasivati kostrijet, na krovovima njegovijem i na ulicama njegovijem sve æe ridati suze lijuæi.
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
I vikaæe Esevon i Eleala, do Jase èuæe im se glas; i vojnici æe Moavski vikati, duša æe se u svakom uzmuèiti.
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
Srce moje vapije za Moavom; bjegunci njegovi pobjegoše dori do Sigora kao junica treæakinja; jer æe se iæi uz brdo Luitsko plaèuæi, i putem Oronaimskim razlijegaæe æe se jauk.
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
Jer æe nestati voda Nimrimskih, jer æe posahnuti bilje, nestaæe trave, zeleni neæe biti.
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
I zato što su ostavljali i što su èuvali odnijeæe se na potok Arapski.
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
Jer æe vika iæi oko meða Moavskih, do Eglaima jauk njihov, i do Vir-Elima jauk njihov.
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
Jer æe se voda Dimonska napuniti krvi; i još æu dometnuti Dimonu, na bjegunce Moavske i na ostatak zemaljski poslaæu lavove.

< Yesaya 15 >