< Yesaya 13 >

1 Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
Breme Vavilonu, koje vidje Isaija sin Amosov.
2 Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
Na gori visokoj podignite zastavu, vièite im iza glasa, mašite rukom, neka uðu na vrata kneževska.
3 Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
Ja sam zapovjedio izabranima svojim i dozvao sam junake svoje da izvrše gnjev moj koji se raduju s velièine moje.
4 Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
Vika stoji ljudstva na gorama kao da je velik narod, vika i vreva carstva skupljenijeh naroda; Gospod nad vojskama pregleda vojsku ubojitu.
5 Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
Dolaze iz daljne zemlje, s kraja nebesa, Gospod i oruða srdnje njegove, da zatre svu zemlju.
6 Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Ridajte, jer je blizu dan Gospodnji; doæi æe kao pustoš od svemoguæega.
7 Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
Zato æe svaka ruka klonuti, i svako srce èovjeèije rastopiti se.
8 Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
I oni æe se smesti, muke i bolovi spopašæe ih, muèiæe se kao porodilja, prepašæe se jedan od drugoga, lica æe im biti kao plamen.
9 Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
Evo, ide dan Gospodnji ljuti s gnjevom i jarošæu da obrati zemlju u pustoš, i grješnike da istrijebi iz nje.
10 Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
Jer zvijezde nebeske i prilike nebeske neæe pustiti svjetlosti svoje, sunce æe pomrèati o roðaju svom, i mjesec neæe pustiti svjetlosti svoje.
11 Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
I pohodiæu vasiljenu za zloæu, i bezbožnike za bezakonje; i ukinuæu razmetanje oholijeh, i ponos silnijeh oboriæu.
12 Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
Uèiniæu da æe èovjek više vrijediti nego zlato èisto, više nego zlato Ofirsko.
13 Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
Zato æu zatresti nebo, i zemlja æe se pokrenuti sa svoga mjesta od jarosti Gospoda nad vojskama i u dan kad se raspali gnjev njegov.
14 Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
I biæe kao srna poplašena i kao stado kojega niko ne sabira; svak æe gledati za svojim narodom, i svak æe bježati u svoju zemlju.
15 Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
Ko se god naðe, biæe proboden, i koji se god skupe, poginuæe od maèa.
16 Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
I djecu æe im razmrskati na njihove oèi, kuæe æe im oplijeniti i žene æe im sramotiti.
17 Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
Evo, ja æu podignuti na njih Mide, koji neæe mariti za srebro, niti æe zlata iskati.
18 Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
Nego æe iz lukova djecu ubijati, ni na plod u utrobi neæe se smilovati, niti æe djece žaliti oko njihovo.
19 Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
I Vavilon, ures carstvima i dika slavi Haldejskoj, biæe kao Sodom i Gomor kad ih Bog zatr.
20 Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
Neæe se u njemu živjeti niti æe se ko naseliti od koljena do koljena, niti æe Arapin razapeti u njemu šatora, niti æe pastiri poèivati onuda.
21 Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
Nego æe poèivati ondje divlje zvijeri, i kuæe æe njihove biti pune velikih zmija, i ondje æe nastavati sove, i aveti æe skakati onuda.
22 Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.
I dovikivaæe se buljine u pustijem kuæama i zmajevi u dvorima veselijem. A doæi æe njegovo vrijeme, i blizu je, i dani njegovi neæe se protegnuti.

< Yesaya 13 >