< Yesaya 13 >

1 Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
Umthwalo weBhabhiloni awubonayo uIsaya indodana kaAmozi.
2 Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
Phakamisani uphawu entabeni eligceke, libaphakamisele ilizwi, liqhwebe ngesandla, ukuze bangene eminyango yeziphathamandla.
3 Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
Mina ngibalayile abangcwelisiweyo bami, ngibizile lamaqhawe ami kuntukuthelo yami, abathokozayo ngobukhosi bami.
4 Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
Ukuxokozela kwexuku ezintabeni, kungathi ngokwabantu abanengi, umsindo wokuxokozela kwemibuso, kwezizwe ezibutheneyo; iNkosi yamabandla ibutha ibutho lempi.
5 Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
Bavela elizweni elikhatshana, emkhawulweni wamazulu, iNkosi kanye lezikhali zentukuthelo yayo, ukuchitha ilizwe lonke.
6 Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Qhinqani isililo, ngoba usuku lweNkosi lusondele; njengokuchitheka okuvela kuSomandla luzafika.
7 Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
Ngenxa yalokhu izandla zonke zizaxega, lenhliziyo yonke yomuntu incibilike;
8 Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
babesebetshaywa luvalo; imihelo lobuhlungu kubabambe; bafuthelwe njengowesifazana obelethayo; bamangale ngulowo ngomakhelwane wakhe; ubuso babo buyibuso bamalangabi.
9 Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
Khangelani, usuku lweNkosi luyeza, lulesihluku lokufutheka lolaka oluvuthayo, ukubeka umhlaba ube yincithakalo; ibhubhise izoni zawo zisuke kuwo.
10 Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
Ngoba inkanyezi zamazulu lemithala yazo kaziyikukhanyisa ukukhanya kwazo; ilanga lizakuba mnyama ekuphumeni kwalo, lenyanga kayiyikukhanyisa ukukhanya kwayo.
11 Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
Ngoba ngizaphindisela ububi phezu komhlaba, laphezu kwabakhohlakeleyo izono zabo; ngiqede ukuzigqaja kwabazikhukhumezayo; ngithobise ukuzikhukhumeza kwabalesihluku.
12 Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
Ngizakwenza ukuthi indoda ibe ligugu elikhulu kulegolide elicwengekileyo, lomuntu kulegolide leOfiri.
13 Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
Ngenxa yalokhu ngizazamazamisa amazulu, lomhlaba uzanyikinyeka usuke endaweni yawo, entukuthelweni yeNkosi yamabandla, losukwini lokuvutha kolaka lwayo.
14 Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
Njalo kuzakuba njengomziki oxotshwayo, lanjengezimvu okungelamuntu oziqoqayo; bazaphenduka ngulowo lalowo ebantwini bakibo, babalekele ngulowo lalowo elizweni lakhe.
15 Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
Wonke ozatholakala uzagwazwa, laye wonke ozabanjwa uzakuwa ngenkemba.
16 Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
Labantwana babo bazachotshozwa phambi kwamehlo abo, izindlu zabo ziphangwe, labomkabo badlwengulwe.
17 Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
Khangela, ngizabavusela amaMede, angakhathaleli isiliva, legolide, angathokozi ngalo.
18 Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
Lamadandili awo azachoboza amajaha; njalo kawayikuba lesihawu ngesithelo sesizalo; ilihlo lawo kaliyikuhawukela abantwana.
19 Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
LeBhabhiloni, udumo lwemibuso, ubuhle bokuziqhenya kwamaKhaladiya, izakuba njengokugenqulwa nguNkulunkulu kweSodoma leGomora.
20 Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
Kakuyikuba lendawo yokuhlala kuze kube nininini, njalo kayiyikuhlalwa kusizukulwana lesizukulwana; lomArabhiya kayikumisa ithente khona, labelusi kabayikulalisa umhlambi khona.
21 Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
Kodwa izilo zeganga zizalala khona, lezindlu zayo zizagcwala izilo ezikhonyayo; lamadodakazi ezintshe azahlala khona, lamagogo aqolotshe khona.
22 Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.
Lezimpisi zizaphendulana emanxiweni ayo, lemigobho ezigodlweni ezilentokozo. Lesikhathi sayo siseduze ukufika, lezinsuku zayo kaziyikuphuziswa.

< Yesaya 13 >