< Hoseya 9 >

1 Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
Ne raduj se, Izrailju, veseleæi se kao narodi, što se kurvaš otstupivši od Boga svojega, miluješ platu kurvarsku po svijem gumnima žitnijem.
2 Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
Gumno i kaca neæe ih hraniti, i mast æe ih prevariti.
3 Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
Oni neæe nastavati u zemlji Gospodnjoj; nego æe se vratiti Jefrem u Misir, i oni æe jesti neèistotu u Asirskoj.
4 Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
Neæe prinositi Gospodu vina, niti æe mu biti ugodne žrtve njihove, nego æe im biti kao hljeb onijeh koji tuže, ko ga god jede oskvrniæe se, jer im je hljeb za žrtve njihove, neæe uæi u dom Gospodnji.
5 Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
Šta æete èiniti na dan svetkovine i na dan praznika Gospodnjega?
6 Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
Jer gle, otiæi æe pustošenja radi; Misir æe ih pribrati, Memfis æe ih pogrepsti; zaklade njihove od srebra naslijediæe kopriva, trnje æe im biti u šatorima.
7 Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
Doðoše dani pohoðenju, doðoše dani plaæanju; poznaæe Izrailj; proroci su ludi, bezumni su u kojima je duh, za mnoštvo bezakonja tvojega i veliku mržnju.
8 Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
Stražar je Jefremov s Bogom mojim, prorok je zamka ptièarska po svijem putovima njegovijem, mržnja je u domu Boga njegova.
9 Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
Duboko su se pokvarili kao u vrijeme Gavajsko; opomenuæe se bezakonja njihova, i pohodiæe grijehe njihove.
10 “Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
Naðoh Izrailja kao grožðe u pustinji; vidjeh oce vaše kao prve smokve na drvetu u poèetku njegovu; oni otidoše k Velfegoru, i odvojiše se za sramotom, i postaše gadni kako im bješe milo.
11 Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
Jefremova æe slava odletjeti kao ptica od roðenja i od utrobe i od zaèetka.
12 Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
Ako li i othrani sinove svoje, ja æu ih uèiniti da budu bez djece, da ne ostane nijedan; i teško njima kad otstupim od njih.
13 Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
Jefrem, kad ga gledah, bješe kao Tir, posaðen na ljupku mjestu; ali æe Jefrem izvesti krvniku sinove svoje.
14 Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
Podaj im, Gospode; šta æeš im dati? podaj im utrobu pometljivu i dojke usahle.
15 “Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
Sva je zloæa njihova u Galgalu; zato ondje mrzim na njih; za zloæu djela njihovijeh izagnaæu ih iz doma svojega; neæu ih više ljubiti: svi su knezovi njihovi odmetnici.
16 Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
Udaren bi Jefrem; korijen im posahnu, neæe roditi roda; ako i rode, ubiæu mili porod utrobe njihove.
17 Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.
Odbaciæe ih Bog moj, jer ga ne slušaju, i skitaæe se po narodima.

< Hoseya 9 >