< Hoseya 7 >

1 Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
Kad lijeèim Izrailja, tada se pokazuje bezakonje Jefremovo i zloæa Samarijska; jer èine laž, i lupež ulazi, i napolju udara èeta.
2 Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
I ne govore u srcu svom da ja pamtim svako bezakonje njihovo; sada stoje oko njih djela njihova, preda mnom su.
3 “Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
Nevaljalstvom svojim vesele cara i lažima svojim knezove.
4 Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
Svi èine preljubu; kao peæ su koju užari hljebar, koji prestane stražiti kad zamijesi tijesto pa dokle uskisne.
5 Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
Na dan cara našega razbolješe se knezovi od mijeha vina, i on pruži ruku svoju potsmjevaèima.
6 Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
Jer na zasjede svoje upravljaju srce svoje, koje je kao peæ; hljebar njihov spava cijelu noæ, ujutru gori kao plamen ognjeni.
7 Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
Svi su kao peæ ugrijani i proždiru svoje sudije; svi carevi njihovi padaju, nijedan izmeðu njih ne vièe k meni.
8 “Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
Jefrem se pomiješao s narodima; Jefrem je pogaèa neprevrnuta.
9 Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
Inostranci jedu mu silu, a on ne zna; sijede kose popadaju ga, a on ne zna.
10 Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
I ponositost Izrailjeva svjedoèi mu u oèi, ali se ne vraæaju ka Gospodu Bogu svojemu niti ga traže uza sve to.
11 “Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
I Jefrem je kao golub, lud, bezuman; zovu Misir, idu u Asirsku.
12 Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
Kad otidu, razapeæu na njih mrežu svoju, kao ptice nebeske svuæi æu ih, karaæu ih kako je kazivano u zboru njihovu.
13 Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
Teško njima, jer zaðoše od mene; pogibao æe im biti, jer me iznevjeriše; ja ih iskupih, a oni govoriše na me laž.
14 Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
Niti me prizivaše iz srca svojega, nego ridaše na odrima svojim; žita i vina radi skupljajuæi se otstupaju od mene.
15 Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
Kad ih karah, ukrijepih im mišice; ali oni misliše zlo na me.
16 Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.
Vraæaju se, ali ne k višnjemu, postaše kao luk lažljiv; knezovi æe njihovi popadati od maèa s obijesti jezika svojega; to æe im biti potsmijeh u zemlji Misirskoj.

< Hoseya 7 >