< Hoseya 4 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
Słuchajcie słowa PANA, synowie Izraela, bo PAN wnosi skargę przeciwko mieszkańcom tej ziemi, gdyż nie ma prawdy ani żadnego miłosierdzia, ani poznania Boga [w] ziemi.
2 Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
Krzywoprzysięstwo, kłamstwo, zabójstwo, kradzież i cudzołóstwo mnożą się, a morderstwo goni morderstwo.
3 Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
Dlatego ziemia będzie lamentować i marnieje wszystko, co w niej mieszka, wraz z polnymi zwierzętami i ptactwem nieba, nawet ryby morskie wyginą.
4 “Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
Ale niech nikt z nimi się nie spiera ani ich nie strofuje, bo twój lud [jest] jak ci, którzy spierają się z kapłanem.
5 Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
Dlatego upadniesz we dnie, upadnie też wraz z tobą prorok w nocy; wyniszczę twoją matkę.
6 Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
Mój lud ginie z braku poznania; a ponieważ ty odrzuciłeś poznanie, ja też ciebie odrzucę, abyś [już] nie był dla mnie kapłanem. Skoro zapomniałeś o prawie twego Boga, ja też zapomnę o twoich synach.
7 Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
Im bardziej się rozmnożyli, tym więcej grzeszyli przeciwko mnie. [Dlatego] ich chwałę zamienię w hańbę.
8 Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Pożerają ofiary za grzech mego ludu i swoją duszą pragną jego nieprawości.
9 Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
I tak samo stanie się z ludem jak z kapłanem, bo ukarzę ich za ich drogi i oddam im za ich uczynki.
10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
Będą jeść, ale się nie nasycą, będą uprawiać nierząd, ale się nie pomnożą, bo nie chcą zważać na PANA.
11 ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
Nierząd, wino i moszcz odbierają serce.
12 za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
Mój lud radzi się u swego drewna, a jego kij mu odpowiada, bo duch nierządu wprowadza ich w błąd i uprawiali nierząd, odstępując od swego Boga.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
Na szczytach gór składają ofiary i na pagórkach palą kadzidło pod dębem, topolą i wiązem, bo ich cień jest dobry. Dlatego wasze córki uprawiają nierząd i wasze kobiety cudzołożą.
14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
Nie będę karał waszych córek, gdy uprawiają nierząd, ani waszych kobiet, gdy cudzołożą. Oni [sami] bowiem odłączają się z nierządnicami i składają ofiary wraz z nierządnicami. A lud, który [tego] nie rozumie, upadnie.
15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
Jeśli ty, Izraelu, uprawiasz nierząd, niech [chociaż] Juda nie obciąży się winą. Nie idźcie do Gilgal ani nie wstępujcie do Bet-Awen, ani nie przysięgajcie: Jak żyje PAN!
16 Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
Izrael bowiem jest nieujarzmiony jak narowista jałówka. Zaprawdę, PAN będzie ich paść jak jagnię na rozległym miejscu.
17 Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
Efraim związał się z bożkami. Zostaw go.
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
Ich napój czyni ich upartymi; nieustannie uprawiają nierząd; jego obrońcy wstydliwie kochają dary.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
Pochwyci ich wiatr swoimi skrzydłami i będą zawstydzeni z powodu swoich ofiar.

< Hoseya 4 >