< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
Recite braæi svojoj: narode moj; i sestrama svojim: pomilovana.
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Prite se s materom svojom, prite se, jer mi nije žena, niti sam joj ja muž; neka odbaci kurvarstva svoja od lica svojega, i preljube svoje od dojaka svojih,
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
Da je ne bih svukao golu i uèinio je kaka je bila onaj dan kad se rodila, i da je ne bih postavio da bude kao pustinja i obratio je da bude kao zemlja zasušena, i umorio je žeðu.
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
I neæu se smilovati na djecu njezinu, jer su kopilad.
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Jer se mati njihova kurva, sramoti se roditeljka njihova; jer govori: iæi æu za milosnicima svojim koji mi daju hljeb moj i vodu moju, vunu moju i lan moj, ulje moje i piæe moje.
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
Zato evo ja æu joj zagraditi put trnjem i zazidaæu zidom da ne naðe staza svojih.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
I trèaæe za svojim milosnicima, ali ih neæe stignuti; i tražiæe ih, ali ih neæe naæi; pa æe reæi: idem da se vratim k prvomu mužu svojemu, jer mi bješe bolje onda nego sada.
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
Jer ona ne zna da sam joj ja davao žito i vino i ulje, i umnožavao joj srebro i zlato, od kojega naèiniše Vala.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
Zato æu uzeti natrag žito svoje, kad bude vrijeme, i vino svoje, kad bude vrijeme, i uzeæu vunu svoju i lan svoj, kojim bi pokrivala golotinju svoju.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
I otkriæu rugobu njezinu pred milosnicima njezinijem, i niko je neæe izbaviti iz moje ruke.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
I ukinuæu svaku radost njezinu, svetkovine njezine, mladine njezine i subote njezine i sve praznike njezine.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
I potræu èokote njezine i smokve, za koje govori: plata su mi, što mi dadoše milosnici moji; i obratiæu ih u šumu da ih jede zvijerje poljsko.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
I pohodiæu na njoj dane Valimske, u koje im je kadila i kitila se obocima i grivnama, i išla za svojim milosnicima, i mene zaboravila, govori Gospod.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
Ali evo, ja æu je primamiti i odvešæu je u pustinju, i govoriæu s njom lijepo.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
I daæu joj vinograde njezine od toga mjesta, i dolinu Ahor za vrata nadanju, i ondje æe pjevati kao za mladosti svoje i kao kad je išla iz Misira.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
I tada æeš me, govori Gospod, zvati: mužu moj; a neæeš me više zvati: Vale moj.
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
Jer æu ukloniti iz usta njezinijeh imena Vala; i neæe im se više pominjati imena.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
I tada æu im uèiniti zavjet sa zvijerjem poljskim i sa pticama nebeskim i s bubinama zemaljskim; i polomiæu luk i maè i rat da ih nestane u zemlji, i uèiniæu da leže bez straha.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
I zaruèiæu te sebi dovijeka, zaruèiæu te sebi pravdom i sudom i milošæu i milosrðem.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
I zaruèiæu te sebi vjerom, i poznaæeš Gospoda.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
I tada æu se odazvati, govori Gospod, odazvaæu se nebesima, a ona æe se odazvati zemlji.
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
A zemlja æe se odazvati žitu i vinu i ulju, a to æe se odazvati Jezraelu.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
I posijaæu je sebi na zemlji, i smilovaæu se na Loruhamu, i reæi æu Loamiji: ti si moj narod, i on æe reæi: Bože moj!

< Hoseya 2 >