< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
Mówcie swoim braciom: Ammi, i swoim siostrom, Ruchama!
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Spierajcie się z waszą matką, spierajcie się, bo ona [nie jest] moją żoną, a ja też nie jestem jej mężem. Niech usunie swoje czyny nierządu sprzed swego oblicza, a swoje cudzołóstwa spośród swoich piersi;
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
W przeciwnym razie rozbiorę ją do naga i wystawię taką, jaka była w dniu swego narodzenia; uczynię ją podobną do pustyni, zostawię ją jak suchą ziemię i uśmiercę ją pragnieniem.
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
Nie zlituję się nad jej dziećmi, gdyż są dziećmi nierządu.
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Ich matka bowiem uprawiała nierząd, bezwstydnie postępowała ich rodzicielka. Mówiła bowiem: Pójdę za moimi kochankami, którzy dają mi mój chleb i moją wodę, moją wełnę i mój len, moją oliwę i moje napoje.
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
Dlatego oto zagrodzę jej drogę cierniami i otoczę murem, aby nie mogła znaleźć swoich ścieżek.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
Wtedy będzie biegać za swymi kochankami, lecz ich nie dogoni; będzie ich szukać, ale nie znajdzie. Potem powie: Pójdę i wrócę do swego pierwszego męża, bo lepiej mi było wtedy niż teraz.
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
Ona bowiem nie wie, że to ja dawałem jej zboże, moszcz i oliwę, [że] dawałem jej obfitość srebra i złota, [których] oni używali dla Baala.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
Dlatego wrócę i zabiorę moje zboże w swoim czasie, mój moszcz w swoim czasie, odbiorę jej moją wełnę i mój len, [który dałem] na okrywanie jej nagości.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
A teraz odkryję jej bezwstydność na oczach jej kochanków i nikt jej nie wyrwie z mojej ręki.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
I położę kres całej jej radości, jej świętom, jej nowiom, jej szabatom i wszystkim jej uroczystym świętom.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
Zniszczę też jej winorośle i drzewa figowe, o których mówiła: Oto moja zapłata, którą mi dali moi kochankowie. I zamienię je w lasy, które pożrą polne zwierzęta.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
I ukarzę ją za te dni Baalów, gdy im paliła kadzidło, stroiła się w swoje kolczyki i klejnoty i chodziła za swymi kochankami, a o mnie zapomniała, mówi PAN.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
Dlatego oto zwabię ją, zaprowadzę na pustynię i będę mówić do niej łaskawie;
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
I dam jej winnice z tego miejsca i dolinę Akor jako wrota nadziei. Ona będzie tam śpiewała jak za dni swej młodości, jak w dniu, kiedy wyszła z ziemi Egiptu.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
W tym dniu, mówi PAN, będziesz mnie nazywać [Iszi] – mój mężu, a nie będziesz mnie już nazywała [Baal] – mój panie!
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
Usunę bowiem z twoich ust imiona Baalów i ich imiona nie będą już wspomniane.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
W tym dniu zawrę dla ciebie przymierze z polnymi zwierzętami, z ptactwem nieba i z tym, co pełza po ziemi. Pokruszę łuk i miecz, wojnę z ziemi [usunę] i sprawię, że będą mieszkać bezpiecznie.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
I poślubię cię sobie na wieki; poślubię cię sobie w sprawiedliwości, w sądzie, w miłosierdziu i w litości.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
Poślubię cię też sobie w wierności i poznasz PANA.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
W tym dniu wysłucham, mówi PAN, wysłucham niebios, a one wysłuchają ziemi;
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
Ziemia wysłucha zboża, moszczu i oliwy, a te rzeczy wysłuchają Jizreel.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
Zasieję go sobie na ziemi i zlituję się nad tym, który nie dostąpił miłosierdzia, i powiem do tego, który nie był moim ludem: [Ty jesteś] moim ludem! A on powie: [Ty jesteś] moim Bogiem.

< Hoseya 2 >