< Hoseya 14 >

1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Obrati se, Izrailju, ka Gospodu Bogu svojemu, jer si pao svojega radi bezakonja.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Uzmite sa sobom rijeèi, i obratite se ka Gospodu; recite mu: oprosti sve bezakonje, i primi dobro; i daæemo žrtve usana svojih.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Asirac nas ne može izbaviti, neæemo jahati na konjma, niti æemo više govoriti djelu ruku svojih: Bože naš; jer u tebe nalazi milost sirota.
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
Iscijeliæu otpad njihov, ljubiæu ih drage volje; jer æe se gnjev moj odvratiti od njega.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Biæu kao rosa Izrailju, procvjetaæe kao ljiljan i pustiæe žile svoje kao drveta Livanska.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
Raširiæe se grane njegove, i ljepota æe mu biti kao u masline i miris kao Livanski.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Oni æe se vratiti i sjedjeti pod sjenom njegovijem, raðaæe kao žito i cvjetaæe kao vinova loza; spomen æe mu biti kao vino Livansko.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Jefreme, šta æe mi više idoli? Ja æu ga uslišiti i gledati; ja æu mu biti kao jela zelena; od mene je tvoj plod.
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Ko je mudar, neka razumije ovo; i razuman neka pozna ovo; jer su pravi putovi Gospodnji, i pravednici æe hoditi po njima, a prestupnici æe pasti na njima.

< Hoseya 14 >