< Hoseya 13 >

1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
While Ephraim was speaking, a horror entered Israel, and he offended by Baal, and he died.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
And now they add that they will be sinning more. And they have made themselves an image cast from their silver, just like the image of idols; but the whole thing has been made by craftsmen. These say to them, “Sacrifice men, you who adore calves.”
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
For this reason, they will be like the morning clouds, and like the morning dew that passes away, just like the dust that is driven by a whirlwind away from the threshing floor, and like the smoke from a chimney.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
But I am the Lord your God from the land of Egypt, and you will not know God apart from me, and there is no Savior except me.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
I knew you in the desert, in the land of solitude.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
According to their pastures, they have been filled up and have been satisfied. And they have lifted up their heart, and they have forgotten me.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
And I will be to them like a lioness, like a leopard in the way of the Assyrians.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
I will run to meet them like a bear that has been robbed of her young, and I will split open the middle of their liver. And I will devour them there like a lion; the beast of the field will tear them apart.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
Perdition is yours, Israel. Your help is only in me.
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
Where is your king? Now, especially, let him save you in all your cities, and from your judges, about whom you said, “Give me kings and princes.”
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
I will give you a king in my wrath, and I will take him away in my indignation.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
The iniquity of Ephraim has been bound; his sin has been engulfed.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
The pains of giving birth will reach him. He is an unwise son. For now he will not remain firm during the contrition of his sons.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
I will free them from the hand of death; from death I will redeem them. Death, I will be your death. Hell, I will be your deadly wound. Consolation is hidden from my eyes. (Sheol h7585)
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
For he will make a division among brothers. The Lord will bring a burning wind, rising up from the desert, and it will dry up his streams, and it will make his fountain desolate, and he will tear apart every collection of desirable useful things.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Let Samaria perish, because she has urged her God towards bitterness. Let them perish by the sword, let their little ones be thrown down, and let their pregnant women be cut in two.

< Hoseya 13 >