< Hoseya 13 >

1 Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
According to the word of Ephraim he adopted ordinances for himself in Israel; and he established them for Baal, and died.
2 Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
And now they have sinned increasingly, and have made for themselves a molten image of their silver, according to the fashion of idols, the work of artificers accomplished for them: they say, Sacrifice men, for the calves have come to an end.
3 Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
Therefore shall they be as a morning cloud, and as the early dew that passes away, as chaff blown away from the threshing floor, and as a vapour from tears.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
But I am the Lord your God that establishes the heaven, and creates the earth, whose hands have framed the whole host of heaven: but I showed them not to you that you should go after them: and I brought you up out of the land of Egypt, and you shall know no God but me; and there is no Saviour beside me.
5 Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
I tended you as a shepherd in the wilderness, in an uninhabited land.
6 Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
According to their pastures, so they were completely filled; and their hearts were exalted; therefore they forgot me.
7 Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
And I will be to them as a panther, and as a leopard.
8 Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
I will meet them by the way of the Assyrians, as a she-bear excited, and I will rend the caul of their heart, and the lions' whelps of the thicket shall devour them there; the wild beasts of the field shall rend them in pieces.
9 “Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
O Israel, who will aid [you] in your destruction?
10 Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
Where is this your king? let him even save you in all your cities: let him judge you, of whom you said, Give me a king and a prince.
11 Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
And I gave you a king in mine anger, and kept [him] back in my wrath.
12 Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
Ephraim [has framed] a conspiracy of unrighteousness, his sin is hidden.
13 Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
Pains as of a woman in travail shall come upon him: he is your wise son, because he shall not stay in the destruction of [your] children.
14 “Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
I will deliver [them] out of the power of Hades, and will redeem them from death: where is your penalty, O death? O Hades, where is your sting? comfort is hidden from mine eyes. (Sheol h7585)
15 ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
Forasmuch as he will cause a division amongst [his] brethren, the Lord shall bring upon him an east wind from the desert, and shall dry up his veins [and] quite drain his fountains: he shall dry up his land, and [spoil] all his precious vessels.
16 Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”
Samaria shall be utterly destroyed: for she has resisted her God; they shall fall by the sword, and their sucklings shall be dashed against the ground, and their women with child ripped up.

< Hoseya 13 >