< Hoseya 11 >

1 “Israeli ali mwana, ndinamukonda, ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
Kad Izrailj bješe dijete, ljubljah ga, i iz Misira dozvah sina svojega.
2 Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana iwo amandithawa kupita kutali. Ankapereka nsembe kwa Abaala ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
Koliko ih zvaše, toliko oni odlaziše od njih; prinosiše žrtve Valima, kadiše likovima.
3 Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda, ndipo ndinawagwira pa mkono; koma iwo sanazindikire kuti ndine amene ndinawachiritsa.
Ja uèih Jefrema hoditi držeæi ga za ruke, ali ne poznaše da sam ih ja lijeèio.
4 Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu ndi zomangira za chikondi; ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.
Vukoh ih uzicama èovjeèjim, užima ljubavnijem; i bijah im kao oni koji im skidaju jaram s èeljusti, i davah im hranu.
5 “Sadzabwerera ku Igupto, koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo pakuti akana kutembenuka.
Neæe se vratiti u zemlju Misirsku, nego æe mu Asirac biti car, jer se ne htješe obratiti.
6 Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo, ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo nadzathetseratu malingaliro awo.
I maè æe stajati u gradovima njegovijem, i potræe prijevornice njegove i proždrijeti za namjere njihove.
7 Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine. Ngakhale atayitana Wammwambamwamba, sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.
Narod je moj prionuo za otpad od mene; zovu ga k višnjemu, ali se nijedan ne podiže.
8 “Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu? Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli? Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima? Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu? Mtima wanga wakana kutero; chifundo changa chonse chikusefukira.
Kako da te dam, Jefreme? da te predam, Izrailju? kako da uèinim od tebe kao od Adame? da te obratim da budeš kao Sevojim? Ustreptalo je srce moje u meni, uskolebala se utroba moja od žalosti.
9 Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa, kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu. Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu, Woyerayo pakati panu. Sindidzabwera mwaukali.
Neæu izvršiti ljutoga gnjeva svojega, neæu opet zatrti Jefrema; jer sam ja Bog a ne èovjek, svetac usred tebe; neæu doæi na grad.
10 Iwo adzatsatira Yehova; Iye adzabangula ngati mkango. Akadzabangula, ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
Iæi æe oni za Gospodom; on æe rikati kao lav; kad rikne, sa strahom æe dotrèati sinovi s mora;
11 Adzabwera akunjenjemera ngati mbalame kuchokera ku Igupto, ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya. Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,” akutero Yehova.
Sa strahom æe dotrèati iz Misira kao ptica, i kao golub iz zemlje Asirske; i naseliæu ih u kuæama njihovijem, govori Gospod.
12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza, nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo. Ndipo Yuda wawukira Mulungu, wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.
Opkolio me je Jefrem lažju i dom Izrailjev prijevarom; ali Juda još vlada s Bogom i vjeran je sa svetima.

< Hoseya 11 >