< Hagai 1 >

1 Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:
In the secounde yeer of Darius, kyng of Persis, in the sixte monethe, in the firste dai of the monethe, the word of the Lord was maad in the hond of Aggey, profete, to Sorobabel, sone of Salatiel, duyk of Juda, and to Jhesu, the greet preest, sone of Josedech,
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’”
and seide, The Lord of oostis seith these thingis, and spekith, This puple seith, Yit cometh not the tyme of the hous of the Lord to be bildid.
3 Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti,
And the word of the Lord was maad in the hond of Aggei,
4 “Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”
profete, and seide, Whether it is tyme to you, that ye dwelle in housis couplid with tymbir, and this hous be forsakun?
5 Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu.
And now the Lord of oostis seith these thingis, Putte ye youre hertis on youre weies.
6 Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”
Ye han sowe myche, and brouyte in litil; ye han etun, and ben not fillid; ye han drunke, and ye ben not ful of drynk; ye hiliden you, and ye ben not maad hoote; and he that gaderide hiris, sente tho in to a sak holid, ether brokun.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu.
The Lord of oostis seith these thingis, Putte ye youre hertis on youre weies.
8 Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova.
Stie ye vp in to the munteyn, bere ye trees, and bilde ye an hous; and it schal be acceptable to me, and Y schal be glorified, seith the Lord.
9 “Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake.
Ye bihelden to more, and lo! it is maad lesse; and ye brouyten in to the hous, and Y blew it out. For what cause, seith the Lord of oostis? for myn hous is desert, and ye hasten ech man in to his hous.
10 Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera.
For this thing heuenes ben forbedun, that thei schulden not yyue dew on you; and the erthe is forbodun, that it schulde not yyue his buriownyng.
11 Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”
And Y clepide drynesse on erthe, and on mounteyns, and on wheete, and on wyn, and on oile, and what euer thingis the erthe bryngith forth; and on men, and on beestis, and on al labour of hondis.
12 Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.
And Sorobabel, the sone of Salatiel, and Jhesus, the greet preest, the sone of Josedech, and alle relifs of the puple, herden the vois of her God, and the wordis of Aggei, the profete, as the Lord God of hem sente him to hem; and al the puple dredde of the face of the Lord.
13 Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova.
And Aggei, a messanger of the Lord, of the messangeris of the Lord, seide to the puple, and spak, Y am with you, seith the Lord.
14 Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo,
And the Lord reiside the spirit of Sorobabel, the sone of Salatiel, duik of Juda, and the spirit of Jhesu, the greet preest, the sone of Josedech, and the spirit of the relifs of al puple; and thei entriden, and maden werk in the hous of the Lord of oostis, her God.
15 pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.
In the foure and twentithe dai of the monethe, in the sixte monethe, in the secunde yeer of kyng Darius.

< Hagai 1 >