< Habakuku 2 >

1 Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
Na swej warcie będę stać, stanę na baszcie i będę się wpatrywać, aby zobaczyć, co [Bóg] będzie mówił i co mam odpowiedzieć, gdy zostanę upomniany.
2 Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
Wtedy PAN mi odpowiedział: Zapisz to widzenie, [zapisz je] wyraźnie na tablicach, aby czytający mógł je szybko przeczytać.
3 Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
[To] widzenie bowiem [dotyczy] oznaczonego czasu, [a] na końcu oznajmi, a nie skłamie; [a] choćby się odwlekało, oczekuj go, bo z pewnością przyjdzie, nie spóźni się.
4 “Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
Oto dusza tego, który się wywyższa, nie jest w nim prawa. Ale sprawiedliwy będzie żył ze swojej wiary.
5 Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol h7585)
Owszem, ponieważ upija się, jest on hardym człowiekiem i nie pozostaje w [swoim] domu; pomnaża swoją żądzę jak piekło i jak śmierć nie może się nasycić, choć zgromadził u siebie wszystkie narody i zebrał u siebie wszystkich ludzi. (Sheol h7585)
6 “Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
Czy ci wszyscy nie ułożą o nim przypowieści i szyderczego przysłowia, mówiąc: Biada temu, który gromadzi nie swoje rzeczy (jak długo?) i obciąża się gęstym błotem!
7 Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
Czy nie powstaną nagle [ci], którzy będą cię kąsać, i nie obudzą się [ci], którzy będą cię szarpać? A staniesz się dla nich łupem.
8 Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Ponieważ złupiłeś wiele narodów, złupią cię też wszystkie pozostałe narody z powodu krwi ludzkiej i przemocy [dokonanej w] ziemi, miastu i wszystkim jego mieszkańcom.
9 “Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
Biada temu, który chciwie pragnie niegodziwego zysku dla swego domu, aby wystawił wysoko swoje gniazdo i tak uszedł mocy zła!
10 Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
Postanowiłeś wytracić wiele narodów na hańbę swemu domowi, a grzeszyłeś przeciwko własnej duszy.
11 Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
Kamień bowiem będzie wołać z muru i sęk z drewna da [o tym] świadectwo.
12 “Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
Biada [temu], który krwią buduje miasto i utwierdza miasto nieprawością!
13 Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
Czyż to nie [pochodzi] od PANA zastępów, że ludy będą się trudzić przy ogniu, a narody będą się męczyć daremnie?
14 Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
Ziemia bowiem będzie napełniona poznaniem chwały PANA, jak wody napełniają morze.
15 “Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
Biada temu, który poi swego bliźniego, przystawiając mu swe naczynie, aż go upoi, by patrzeć na jego nagość!
16 Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
Nasyciłeś się hańbą zamiast sławą; upij się sam i będziesz obnażony. Kielich prawicy PANA zwróci się przeciw tobie i sromotne wymioty [pokryją] twoją sławę.
17 Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Okryje cię bowiem bezprawie Libanu i spustoszenie bestii, które ich straszyły, z powodu krwi ludzkiej i przemocy [dokonanej w] ziemi miastu i wszystkim jego mieszkańcom.
18 “Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
Cóż pomoże rzeźbiony posąg, który wykonał jego rzemieślnik, [albo] odlany [obraz] i nauczyciel kłamstwa, aby rzemieślnik pokładał w nim ufność, czyniąc nieme bożki?
19 Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
Biada [temu], który mówi do drewna: Przebudź się, a do niemego kamienia: Obudź się! Czyż on może nauczać? Spójrz na niego, jest powleczony złotem i srebrem, ale nie ma w nim żadnego ducha.
20 Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”
PAN jest w swoim świętym przybytku. Niech cała ziemia zamilknie przed nim.

< Habakuku 2 >