< Habakuku 2 >

1 Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
I will stand upon my watch, and mount upon the rock, and watch to see what he will say by me, and what I shall answer when I am reproved.
2 Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
And the Lord answered me and said, Write the vision, and [that] plainly on a tablet, that he that reads it may run.
3 Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
For the vision [is] yet for a time, and it shall shoot forth at the end, and not in vain: though he should tarry, wait for him; for he will surely come, and will not tarry.
4 “Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
If he should draw back, my soul has no pleasure in him: but the just shall live by my faith.
5 Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol h7585)
But the arrogant man and the scorner, the boastful man, shall not finish anything; who has enlarged his desire as the grave, and like death he is never satisfied, and he will gather to himself all the nations, and will receive to himself all the peoples. (Sheol h7585)
6 “Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
Shall not all these take up a parable against him? and a proverb to tell against him? and they shall say, Woe to him that multiplies to himself the possessions which are not his! how long? and who heavily loads his yoke.
7 Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
For suddenly there shall arise up those that bite him, and they that plot against thee shall awake, and thou shalt be a plunder to them.
8 Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Because thou hast spoiled many nations, all the nations that are left shall spoil [thee], because of the blood of men, and the sins of the land and city, and of all that dwell in it.
9 “Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
Woe to him that covets an evil covetousness to his house, that he may set his nest on high, that he may be delivered from the power of evils.
10 Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
Thou hast devised shame to thy house, thou hast utterly destroyed many nations, and thy soul has sinned.
11 Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
For the stone shall cry out of the wall, and the beetle out of the timber shall speak.
12 “Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
Woe to him that builds a city with blood, and establishes a city by unrighteousness.
13 Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
Are not these things of the Lord Almighty? surely many people have been exhausted in the fire, and many nations have fainted.
14 Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
For the earth shall be filled with the knowledge of the glory of the Lord; it shall cover them as water.
15 “Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
Woe to him that gives his neighbour to drink the thick lees [of wine], and intoxicates [him], that he may look upon their secret parts.
16 Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
Drink thou also [thy] fill of disgrace instead of glory: shake, O heart, and quake, the cup of the right hand of the Lord has come round upon thee, and dishonour has gathered upon thy glory.
17 Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
For the ungodliness of Libanus shall cover thee, and distress because of wild beasts shall dismay thee, because of the blood of men, and the sins of the land and city, and of all that dwell in it.
18 “Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
What profit it the graven image, that they have graven it? [one] has made it a molten work, a false image; for the maker has trusted in his work, to make dumb idols.
19 Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
Woe to him that says to the wood, Awake, arise; and to the stone, Be thou exalted! whereas it is an image, and this is a casting of gold and silver, and there is no breath in it.
20 Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”
But the Lord is in his holy temple: let all the earth fear before him.

< Habakuku 2 >