< Genesis 9 >

1 Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
And God blisside Noe and hise sones, and seide to hem, Encreesse ye, and be ye multiplied, and fille ye the erthe;
2 Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
and youre drede and tremblyng be on alle vnresonable beestis of erthe, and on alle briddis of heuene, with alle thingis that ben moued in erthe; alle fischis of the see ben youun to youre hond.
3 Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
And al thing which is moued and lyueth schal be to you in to mete; Y have youe to you alle thingis as greene wortis,
4 “Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
outakun that ye schulen not ete fleisch with blood,
5 Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
for Y schal seke the blood of youre lyues of the hoond of alle vnresonable beestis and of the hoond of man, of the hoond of man and of hys brother Y schal seke the lijf of man.
6 “Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
Who euere schedith out mannus blood, his blood schal be sched; for man is maad to the ymage of God.
7 Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
Forsothe encreesse ye, and be ye multiplied, and entre ye on erthe, and fille ye it, Also the Lord seide thes thingis to Noe,
8 Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
and to his sones with him, Lo!
9 “Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
Y schal make my couenaunt with you, and with your seed after you,
10 pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
and to ech lyuynge soule which is with you, as wel in briddis as in werk beestis and smale beestis of erthe, and to alle thingis that yeden out of the schip, and to alle vnresonable beestis of erthe.
11 Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
Y schal make my couenaunt with you, and ech fleisch schal no more be slayn of the watris of the greet flood, nethir the greet flood distriynge al erthe schal be more.
12 Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
And God seide, This is the signe of boond of pees, which Y yyue bitwixe me and you, and to ech lyuynge soule which is with you, in to euerlastynge generaciouns.
13 Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
Y schal sette my bowe in the cloudis, and it schal be a signe of boond of pees bitwixe me and erthe;
14 Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
and whanne Y schal hile heuene with cloudis, my bowe schal appere in the cloudis,
15 ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
and Y schal haue mynde of my boond of pees which Y made with you, and with ech soule lyuynge, that nurschith fleisch; and the watris of the greet flood schulen no more be to do awey al fleish.
16 Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
And my bowe schal be in the cloudis, and Y schal se it, and Y schal haue mynde of euerlastynge boond of pees, which is maad bitwixe God and man, and ech soul lyuynge of al fleisch which is on erthe.
17 Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
And God seide to Noe, This schal be a signe of boond of pees, which Y made bitwixe me and ech fleisch on erthe.
18 Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
Therfore thei that yeden out of the schip weren Noe, Sem, Cham, and Japheth; forsothe Cham, thilke is the fadir of Chanaan.
19 Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
These thre weren the sones of Noe, and al the kynde of men was sowun of hem on al erthe.
20 Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
And Noe, an erthe tiliere, bigan to tile the erthe, and he plauntide a viner,
21 Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
and he drank wyn, and was drunkun; and he was nakid, and lay in his tabernacle.
22 Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
And whanne Cham, the fadir of Chanaan, hadde seien this thing, that is, that the schameful membris of his fadir weren maad nakid, he telde to hise tweye britheren with out forth.
23 Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
And sotheli Sem and Jafeth puttiden a mentil on her schuldris, and thei yeden bacward, and hileden the schameful membris of her fadir, and her faces weren turned awei, and thei sien not the priuy membris of her fadir.
24 Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
And forsothe Noe wakide of the wyn, and whanne he hadde lerned what thingis his lesse sone hadde do to hym,
25 anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
he seide, Cursid be the child Canaan, he schal be seruaunt of seruauntis to hise britheren.
26 Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
And Noe seide, Blessid be the Lord God of Sem,
27 Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
and Chanaan be the seruaunt to Sem; God alarge Jafeth, and dwelle in the tabernaclis of Sem, and Chanaan be seruaunt of hym.
28 Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
Forsothe Noe lyuede aftir the greet flood thre hundrid and fifti yeer;
29 Anamwalira ali ndi zaka 950.
and alle the daies of hym weren fillid nyn hundrid and fifty yeer, and he was deed.

< Genesis 9 >