< Genesis 5 >

1 Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
Ovo je pleme Adamovo. Kad Bog stvori èovjeka, po oblièju svojemu stvori ga.
2 Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
Muško i žensko stvori ih, i blagoslovi ih, i nazva ih èovjek, kad biše stvoreni.
3 Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
I poživje Adam sto i trideset godina, i rodi sina po oblièju svojemu, kao što je on, i nadjede mu ime Sit.
4 Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Sita poživje Adam osam stotina godina, raðajuæi sinove i kæeri;
5 Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
Tako poživje Adam svega devet stotina i trideset godina; i umrije.
6 Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
A Sit poživje sto i pet godina, i rodi Enosa;
7 Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Enosa poživje Sit osam stotina i sedam godina, raðajuæi sinove i kæeri;
8 Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
Tako poživje Sit svega devet stotina i dvanaest godina; i umrije.
9 Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
A Enos poživje devedeset godina, i rodi Kajinana;
10 Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Kajinana poživje Enos osam stotina i petnaest godina, raðajuæi sinove i kæeri;
11 Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
Tako poživje Enos svega devet stotina i pet godina; i umrije.
12 Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
A Kajinan poživje sedamdeset godina, i rodi Maleleila;
13 Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Maleleila poživje Kajinan osam stotina i èetrdeset godina, raðajuæi sinove i kæeri;
14 Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
Tako poživje Kajinan svega devet stotina i deset godina; i umrije.
15 Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
A Maleleilo poživje šezdeset i pet godina, i rodi Jareda;
16 Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Jareda poživje Maleleilo osam stotina i trideset godina, raðajuæi sinove i kæeri;
17 Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
Tako poživje Maleleilo svega osam stotina i devedeset i pet godina; i umrije.
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
A Jared poživje sto i šezdeset i dvije godine, i rodi Enoha;
19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Enoha poživje Jared osam stotina godina, raðajuæi sinove i kæeri;
20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
Tako poživje Jared svega devet stotina i šezdeset i dvije godine, i umrije.
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
A Enoh poživje šezdeset i pet godina, i rodi Matusala;
22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Matusala poživje Enoh jednako po volji Božjoj trista godina, raðajuæi sinove i kæeri;
23 Zaka zonse za Enoki zinali 365.
Tako poživje Enoh svega trista i šezdeset i pet godina;
24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
I živeæi Enoh jednako po volji Božjoj, nestade ga, jer ga uze Bog.
25 Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
A Matusal poživje sto i osamdeset i sedam godina, i rodi Lameha;
26 Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Lameha poživje Matusal sedam stotina i osamdeset i dvije godine, raðajuæi sinove i kæeri;
27 Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
Tako poživje Matusal svega devet stotina i šezdeset i devet godina; i umrije.
28 Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
A Lameh poživje sto i osamdeset i dvije godine, i rodi sina,
29 Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
I nadjede mu ime Noje govoreæi: ovaj æe nas odmoriti od posala naših i od truda ruku naših na zemlji, koju prokle Gospod.
30 Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
A rodiv Noja poživje Lameh pet stotina i devedeset i pet godina, raðajuæi sinove i kæeri;
31 Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
Tako poživje Lameh svega sedam stotina i sedamdeset i sedam godina; i umrije.
32 Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
A Noju kad bi pet stotina godina, rodi Noje Sima, Hama i Jafeta.

< Genesis 5 >