< Genesis 49 >

1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
Poslije sazva Jakov sinove svoje i reèe: skupite se da vam javim šta æe vam biti do pošljetka.
2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
Skupite se i poslušajte, sinovi Jakovljevi, poslušajte Izrailja oca svojega.
3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Ruvime, ti si prvenac moj, krjepost moja i poèetak sile moje; prvi gospodstvom i prvi snagom.
4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
Navro si kao voda; neæeš biti prvi; jer si stao na postelju oca svojega i oskvrnio je legav na nju.
5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
Simeun i Levije, braæa, maèevi su im oružje nepravdi.
6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
U tajne njihove da ne ulazi duša moja, sa zborom njihovijem da se ne sastavlja slava moja; jer u gnjevu svojem pobiše ljude, i za svoje veselje pokidaše volove.
7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
Proklet da je gnjev njihov, što bješe nagao, i ljutina njihova, što bješe žestoka; razdijeliæu ih po Jakovu, i rasuæu ih po Izrailju.
8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
Juda, tebe æe hvaliti braæa tvoja, a ruka æe ti biti za vratom neprijateljima tvojim, i klanjaæe ti se sinovi oca tvojega.
9 Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
Laviæu Juda! s plijena si se vratio, sine moj; spusti se i leže kao lav i kao ljuti lav; ko æe ga probuditi?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
Palica vladalaèka neæe se odvojiti od Jude niti od nogu njegovijeh onaj koji postavlja zakon, dokle ne doðe onaj kome pripada, i njemu æe se pokoravati narodi.
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
Veže za èokot magare svoje, i za plemenitu lozu mlade od magarice svoje; u vinu pere haljinu svoju i ogrtaè svoj u soku od grožða.
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
Oèi mu se crvene od vina i zubi bijele od mlijeka.
13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
Zavulon æe živjeti pokraj mora i gdje pristaju laðe, a meða æe mu biti do Sidona.
14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
Isahar je magarac jak u kostima, koji leži u toru,
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
I vidjev da je poèivanje dobro i da je zemlja mila, sagnuæe ramena svoja da nosi, i plaæaæe danak.
16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
Dan æe suditi svojemu narodu, kao jedno izmeðu plemena Izrailjevih.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
Dan æe biti zmija na putu i guja na stazi, koja ujeda konja za kièicu, te pada konjik nauznako.
18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
Gospode, tebe èekam da me izbaviš.
19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
A Gad, njega æe vojska svladati; ali æe najposlije on nadvladati.
20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
U Asira æe biti obilata hrana, i on æe davati slasti carske.
21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
Neftalim je košuta puštena, i govoriæe lijepe rijeèi.
22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
Josif je rodna grana, rodna grana kraj izvora, kojoj se ogranci raširiše svrh zida.
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
Ako ga i ucvijeliše ljuto i strijeljaše na nj, i biše mu neprijatelji strijelci,
24 Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
Opet osta jak luk njegov i ojaèaše mišice ruku njegovijeh od ruku jakoga Boga Jakovljeva, odakle posta pastir, kamen Izrailju,
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
Od silnoga Boga oca tvojega, koji æe ti pomagati, i od svemoguæega, koji æe te blagosloviti blagoslovima ozgo s neba, blagoslovima ozdo iz bezdana, blagoslovima od dojaka i od materice.
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
Blagoslovi oca tvojega nadvisiše blagoslove mojih starijeh svrh brda vjeènijeh, neka budu nad glavom Josifovom i nad tjemenom odvojenoga izmeðu braæe.
27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
Venijamin je vuk grabljivi, jutrom jede lov, a veèerom dijeli plijen.
28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
Ovo su dvanaest plemena Izrailjevih, i ovo im otac izgovori kad ih blagoslovi, svako blagoslovom njegovijem blagoslovi ih.
29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
Potom im zapovjedi i reèe im: kad se priberem k rodu svojemu, pogrebite me kod otaca mojih u peæini koja je na njivi Efrona Hetejina,
30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
U peæini koja je na njivi Makpelskoj prema Mamriji u zemlji Hananskoj, koju kupi Avram s njivom u Efrona Hetejina da ima svoj grob.
31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
Ondje pogreboše Avrama i Saru ženu njegovu, ondje pogreboše Isaka i Reveku ženu njegovu, i ondje pogreboh Liju.
32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
A kupljena je njiva i peæina na njoj u sinova Hetovijeh.
33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
A kad izgovori Jakov zapovjesti sinovima svojim, diže noge svoje na postelju, i umrije, i pribran bi k rodu svojemu.

< Genesis 49 >