< Genesis 47 >

1 Yosefe anapita kukamuwuza Farao kuti, “Abambo anga, abale anga pamodzi ndi nkhosa, ngʼombe zawo, ndi antchito awo abwera kuchokera ku dziko la Kanaani ndipo tsopano ali ku Goseni.”
I otišav Josif javi Faraonu i reèe: otac moj i braæa moja s ovcama svojim i s govedima svojim i sa svijem što imaju doðoše iz zemlje Hananske, i evo ih u zemlji Gesemskoj.
2 Iye anapita kwa Farao kuja ndi abale ake asanu, kukawaonetsa.
I uzev nekolicinu braæe svoje, pet ljudi, izvede ih pred Faraona.
3 Farao anafunsa abale akewo kuti, “Mumagwira ntchito yanji?” Iwo anamuyankha kuti, “Ife, bwana ndife oweta ziweto, monga ankachitira makolo athu.
A Faraon reèe braæi njegovoj: kakvu radnju radite? A oni rekoše Faraonu: pastiri su sluge tvoje, i mi i naši stari.
4 Ife tabwera kudzakhala kuno kwa kanthawi chifukwa njala yafika poopsa ku Kanaani motero kuti kulibe msipu wodyetsera ziweto. Ndiye bwana tiloleni kuti tikhale ku Goseni.”
Još rekoše Faraonu: doðosmo da živimo kao došljaci u ovoj zemlji, jer nema paše za stoku tvojih sluga, jer je velika glad u zemlji Hananskoj; a sada dopusti da žive u zemlji Gesemskoj sluge tvoje.
5 Farao anati kwa Yosefe, “Abambo ako ndi abale ako abwera kwa iwe.
A Faraon reèe Josifu: otac tvoj i braæa tvoja doðoše k tebi;
6 Dziko lonse la Igupto lili mʼdzanja lako. Uwakhazike abambo ako ndi abale ako mʼmalo achonde kwambiri. Akhale ku Goseni. Ndipo ngati ukudziwapo ena mwa iwo amene ali akatswiri pa kuweta ziweto, uwapatse udindo woyangʼanira ziweto zanga.”
U tvojoj je vlasti zemlja Misirska; na najboljem mjestu u ovoj zemlji naseli oca svojega i braæu svoju, neka žive u zemlji Gesemskoj; i ako koje znaš izmeðu njih da su vrijedni ljudi, postavi ih nad mojom stokom.
7 Kenaka Yosefe anapita ndi abambo ake kwa Farao kukawaonetsa, ndipo Yakobo anadalitsa Faraoyo.
Poslije dovede Josif i Jakova oca svojega i izvede ga pred Faraona, i blagoslovi Jakov Faraona.
8 Atatero, Farao anafunsa Yakobo kuti, “Muli ndi zaka zingati?”
A Faraon reèe Jakovu: koliko ti ima godina?
9 Yakobo anayankha kuti, “Zaka za maulendo anga zakwana 130. Zaka za moyo wanga ndi zowerengeka, komanso zakhala zaka za masautso. Zaka za moyo wanga sizingafanane ndi zaka za moyo wa makolo anga.”
Odgovori Jakov Faraonu: meni ima sto i trideset godina, kako sam došljak. Malo je dana života mojega i zli su bili, niti stižu vijeka otaca mojih, koliko su oni živjeli.
10 Atatha kumudalitsa Farao uja, Yakobo anatsanzika nʼkunyamuka.
I blagosloviv Jakov Faraona otide od Faraona.
11 Choncho Yosefe anakhazika abambo ake aja ndi abale ake mʼdziko la Igupto. Iye anawapatsa dera la Ramesesi limene linali dziko lachonde kwambiri monga analamulira Farao.
A Josif naseli oca svojega i braæu svoju, i dade im dobro u zemlji Misirskoj na najboljem mjestu te zemlje, u zemlji Rameskoj, kao što zapovjedi Faraon.
12 Yosefe anaperekanso chakudya kwa abambo ake, kwa abale ake ndi kwa onse a mʼnyumba ya abambo ake monga mwa chiwerengero cha ana awo.
I hranjaše Josif hljebom oca svojega i braæu svoju i sav dom oca svojega do najmanjega.
13 Njala inakula kwambiri motero kuti chakudya chinasowa mʼdziko lonse. Anthu a ku Igupto ndi ku Kanaani analefuka nayo njalayo.
Ali nesta hljeba u svoj zemlji, jer glad bijaše vrlo velika, i uzmuèi se zemlja Misirska i zemlja Hananska od gladi.
14 Yosefe anasonkhanitsa ndalama zonse zimene anthu a mu Igupto ndi Kanaani ankapereka pogula tirigu, ndipo anabwera nazo ku nyumba kwa Farao.
I pokupi Josif sve novce što se nalažahu po zemlji Misirskoj i po zemlji Hananskoj za žito koje kupovahu, i slagaše novce u kuæu Faraonovu.
15 Anthu a ku Igupto ndi Kanaani ndalama zitawathera, Aigupto onse anabwera kwa Yosefe nati, “Tipatseni chakudya. Nanga tiferenji pamaso panu? Ndalama zathu zatha.”
A kad nesta novaca u zemlji Misirskoj i u zemlji Hananskoj, stadoše svi Misirci dolaziti k Josifu govoreæi: daj nam hljeba; zašto da mremo kod tebe, što novaca nema?
16 Ndipo Yosefe anawayankha kuti, “Bwerani ndi ziweto zanu ndipo tidzasinthana ndi chakudya poti mukuti ndalama zanu zatha.”
A Josif im govoraše: dajte stoku svoju, pa æu vam dati hljeba za stoku, kad je nestalo novaca.
17 Choncho anthu anabwera ndi ziweto zawo monga akavalo, nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi abulu ndipo Yosefe anawapatsa zakudya.
I dovoðahu stoku svoju k Josifu, i Josif im davaše hljeba za konje i za ovce i za goveda i za magarce. Tako ih prehrani onu godinu hljebom za svu stoku njihovu.
18 Chitatha chaka chimenecho, anthu anapitanso kwa Yosefe chaka chinacho nati, “Ife sitingakubisireni mbuye wathu kuti ndalama zathu zatithera ndipo ziweto zathu zili ndi inu, palibenso choti nʼkukupatsani mbuye wathu kupatula matupi athu ndi dziko lathu.
A kad proðe ona godina, stadoše opet dolaziti k njemu druge godine govoreæi: ne možemo tajiti od gospodara svojega, ali je novaca nestalo, i stoka koju imasmo u našega je gospodara; i nije ostalo ništa da donesemo gospodaru svojemu osim tjelesa naših i njiva naših.
19 Tiferenji ife ndi dziko lathu inu mukuona? Mutipatse chakudya ndipo tidzigulitsa ife ndi minda yathu yomwe. Ife tidzakhala akapolo a Farao. Tipatseni mbewuzo kuti tikhale ndi moyo tisafe ndipo dziko lisachite bwinja.”
Zašto da mremo na tvoje oèi? evo i nas i naših njiva; kupi nas i njive naše za hljeb, da s njivama svojim budemo robovi Faraonu, i daj žita da ostanemo živi i ne pomremo i da zemlja ne opusti.
20 Choncho Yosefe anamugulira Farao dziko lonse la Igupto. Aliyense mu Igupto anagulitsa munda wake chifukwa njala inakula kwambiri. Dziko lonse linasanduka la Farao,
Tako pokupova Josif Faraonu sve njive u Misiru, jer Misirci prodavahu svaki svoju njivu, kad glad uze jako mah meðu njima. I zemlja posta Faraonova.
21 ndipo Yosefe anawasandutsa anthu onse kukhala akapolo a Farao, kuchokera ku malire a mbali ina ya Igupto kukafika ku malire a mbali ina ya dzikolo.
A narod preseli u gradove od jednoga kraja Misira do drugoga.
22 Komabe, sanagule minda ya ansembe chifukwa Farao ankawapatsa thandizo lokwanira. Nʼchifukwa chake sanagulitse minda yawo.
Samo ne kupi sveštenièkih njiva; jer Faraon odredi dio sveštenicima, i hranjahu se od svojega dijela, koji im dade Faraon, te ne prodaše svojih njiva.
23 Yosefe anati kwa anthuwo, “Tsono poti ndakugulani inu ndi minda yanu, kugulira Farao. Nayi mbewu kuti mudzale mʼminda yanu.
A Josif reèe narodu: evo kupih danas vas i njive vaše Faraonu; evo vam sjemena, pa zasijte njive.
24 Koma podzakolola, mudzapereka gawo limodzi la magawo asanu aliwonse kwa Farao. Magawo anayi enawo adzakhala anu. Zina mudzasunge mbewu ndi zina mudzadye inuyo, mabanja anu ndi ana anu.”
A što bude roda, daæete peto Faraonu, a èetiri dijela neka budu vama za sjeme po njivama i za hranu vama i onijema koji su po kuæama vašim i za hranu djeci vašoj.
25 Iwo anati, “Mwatipulumutsa potichitira zabwinozi, mbuye wathu, tsono tidzakhala akapolo a Farao.”
A oni rekoše: ti si nam život saèuvao; neka naðemo milost pred gospodarem svojim da budemo robovi Faraonu.
26 Choncho Yosefe anakhazikitsa lamulo limene lilipobe mpaka lero mʼdziko lonse la Igupto kuti limodzi la magawo asanu a zokolola ndi la Farao. Ndi minda ya ansembe yokha imene sinatengedwe kukhala ya Farao.
I postavi Josif zakon do današnjega dana za njive Misirske da se daje peto Faraonu; samo njive sveštenièke ne postaše Faraonove.
27 Tsono Aisraeli anakhazikika mʼdziko la Igupto ku chigawo cha Goseni. Kumeneko anapeza chuma ndipo anaberekana nachuluka kwambiri.
A djeca Izrailjeva življahu u zemlji Misirskoj u kraju Gesemskom, i držahu ga, i narodiše se i namnožiše se veoma.
28 Yakobo anakhala ku Igupto zaka 17 ndipo zaka za moyo wake zinali 147.
I Jakov poživje u zemlji Misirskoj sedamnaest godina; a svega bi Jakovu sto i èetrdeset i sedam godina.
29 Nthawi itayandikira yoti Israeli amwalire, anayitanitsa mwana wake Yosefe nati kwa iye, “Ngati ukundikondadi monga abambo ako, ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga ndipo ulonjeze kuti udzaonetsa kukoma mtima ndi kukhulupirika kwako kwa ine kuti sudzayika mtembo wanga kuno ku Igupto.
A kad se približi vrijeme Izrailju da umre, dozva sina svojega Josifa, i reèe mu: ako sam našao milost pred tobom, metni ruku svoju pod stegno moje, i uèini mi milost i vjeru, nemoj me pogrepsti u Misiru;
30 Ine ndikagona pamodzi ndi makolo anga. Choncho ndikadzamwalira udzanditulutse mu Igupto muno ndipo ukayike mtembo wanga kumene anayikidwa makolo anga.” Yosefe anati, “Ndidzachita monga mwanenera.”
Nego neka ležim kod otaca svojih; i ti me odnesi iz Misira i pogrebi me u grobu njihovu. A on reèe: uèiniæu kako si kazao.
31 Yakobo anati, “Lumbira kwa ine.” Yosefe analumbira kwa iye, ndipo Israeli anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
I reèe mu Jakov: zakuni mi se. I on mu se zakle. I pokloni se Izrailj preko uzglavlja od odra svojega.

< Genesis 47 >