< Genesis 44 >

1 Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
Wtedy [Józef] rozkazał zarządcy swego domu: Napełnij wory tych ludzi zbożem, ile tylko mogą unieść, a pieniądze każdego włóż na wierzch jego wora.
2 Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
Mój kielich też, kielich srebrny, włóż na wierzch wora najmłodszego razem z pieniędzmi za zboże. I zrobił według słów Józefa, jak mu rozkazał.
3 Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
O świcie wyprawiono tych ludzi razem z ich osłami.
4 Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
Gdy wyszli z miasta i byli niedaleko, Józef powiedział do zarządcy swego domu: Wstań, goń tych ludzi, a gdy ich dogonisz, powiedz do nich: Czemu oddaliście złem za dobro?
5 Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
Czy to nie jest [kielich], z którego pija mój pan i z którego wróży? Źle postąpiliście, dopuszczając się tego.
6 Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
[Ten] dogonił ich więc i powiedział do nich te słowa.
7 Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
Ale [oni] mu odpowiedzieli: Dlaczego mój pan mówi takie słowa? Nie daj Boże, aby twoi słudzy mieli tak postąpić.
8 Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
Przecież pieniądze, które znaleźliśmy na wierzchu naszych worów, przynieśliśmy do ciebie z powrotem z ziemi Kanaan. Jakże mielibyśmy kraść z domu twego pana srebro lub złoto?
9 Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
U którego z twoich sług to się znajdzie, niech umrze, a my będziemy niewolnikami mego pana.
10 Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
[On] powiedział: Niech będzie tak, jak mówicie. Przy którym znajdzie się kielich, ten będzie niewolnikiem, a wy będziecie niewinni.
11 Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
Wtedy każdy szybko zdjął swój wór na ziemię i rozwiązał go.
12 Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
I szukał, zaczynając od starszego, a kończąc na najmłodszym. I znalazł kielich w worze Beniamina.
13 Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
Wtedy rozdarli swoje szaty, każdy załadował swego osła i wrócili do miasta.
14 Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
Przyszedł więc Juda i jego bracia do domu Józefa, który tam jeszcze był. I upadli przed nim na ziemię.
15 Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
I Józef zapytał ich: Co zrobiliście? Czy nie wiedzieliście, że [taki] człowiek jak ja potrafi wróżyć?
16 Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
Wtedy Juda odpowiedział: Cóż możemy odpowiedzieć memu panu? Co możemy mówić i jak mamy się usprawiedliwić? Bóg znalazł nieprawość u twoich sług. Oto jesteśmy niewolnikami mego pana, zarówno my, jak i ten, u którego znalazł się kielich.
17 Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
A on odpowiedział: Nie daj Boże, abym miał tak uczynić. Człowiek, w którego ręku znaleziono kielich, będzie moim niewolnikiem. Wy zaś jedźcie w pokoju do waszego ojca.
18 Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
Wtedy Juda podszedł do niego i powiedział: Mój panie! [Pozwól] twemu słudze mówić słowo do uszu mego pana, a niech nie zapala się twój gniew na twego sługę, gdyż ty jesteś jak sam faraon.
19 Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
Mój pan pytał swoich sług: Czy macie ojca albo brata?
20 Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
Wtedy odpowiedzieliśmy memu panu: Mamy ojca, starca, i chłopca małego [spłodzonego] w jego starości. Jego brat umarł i tylko on został [po] swej matce, i jego ojciec go kocha.
21 “Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
Potem mówiłeś [do nas], swoich sług: Przyprowadźcie go do mnie, abym mógł go zobaczyć własnymi oczyma.
22 Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
I mówiliśmy do mego pana: Chłopiec nie będzie mógł opuścić swego ojca, bo gdyby opuścił swego ojca, ten by umarł.
23 Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
Wtedy powiedziałeś do swoich sług: Jeśli nie przyjdzie z wami wasz najmłodszy brat, więcej nie zobaczycie mojej twarzy.
24 Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
Gdy więc przyszliśmy do twego sługi, mego ojca, powtórzyliśmy mu te słowa mego pana.
25 “Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
Wtedy nasz ojciec powiedział: Jedźcie znowu i kupcie nam trochę żywności.
26 Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
I powiedzieliśmy: Nie możemy [tam] iść. Lecz jeśli [będzie] z nami nasz najmłodszy brat, wtedy pojedziemy. Bo nie będziemy mogli zobaczyć twarzy tego człowieka, jeśli nie będzie z nami naszego najmłodszego brata.
27 “Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
I twój sługa, mój ojciec, powiedział do nas: Wy wiecie, że moja żona urodziła mi dwóch [synów].
28 Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
Jeden wyszedł ode mnie i powiedziałem: Na pewno został rozszarpany [przez zwierzę] i nie widziałem go do dziś.
29 Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol h7585)
A jeśli zabierzecie mi też tego i spotka go nieszczęście, wtedy w żalu doprowadzicie mnie, osiwiałego, do grobu. (Sheol h7585)
30 “Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
Dlatego jeśli przyjdę do twego sługi, mojego ojca, a nie będzie z nami chłopca, z którym jest bardzo związany;
31 ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol h7585)
Stanie się tak, że jak tylko zobaczy, że chłopca nie ma, umrze. A twoi słudzy doprowadzą twego sługę, naszego ojca, osiwiałego, z żalu do grobu. (Sheol h7585)
32 Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
Bo twój sługa wziął na siebie odpowiedzialność przed ojcem i mówił: Jeśli go nie przyprowadzę, będę po wszystkie dni winien grzechu przeciw mojemu ojcu.
33 “Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
Teraz więc, proszę, niech twój sługa zostanie niewolnikiem mego pana zamiast tego chłopca, a niech chłopak idzie ze swymi braćmi.
34 Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”
Bo jak ja mam wrócić do mego ojca, gdy nie będzie ze mną tego chłopca? Nie chciałbym patrzeć na rozpacz, która by dotknęła mego ojca.

< Genesis 44 >