< Genesis 43 >

1 Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
In the meene tyme hungur oppresside greetli al the lond;
2 Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
and whanne the meetis weren wastid, whiche thei brouyten fro Egipt, Jacob seide to hise sones, Turne ye ayen, and bie ye a litil of meetis to vs.
3 Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
Judas answeride, The ilke man denounside to vs vndir witnessyng of an ooth, and seide, Ye schulen not se my face, if ye schulen not brynge with you youre leeste brother;
4 Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
therfor if thou wolt sende hym with vs, we schulen go to gidere, and we schulen bie necessaries to thee;
5 Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
ellis if thou wolt not, we schulen not go; for as we seiden ofte, the man denounside to vs, and seide, Ye schulen not se my face with out youre leeste brother.
6 Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
Forsothe Israel seide to hem, Ye diden this in to my wretchidnesse, that ye schewiden to hym, that ye hadden also another brother.
7 Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
And thei answeriden, The man axide vs bi ordre oure generacioun, if the fadir lyuede, if we hadden a brother; and we answeriden suyngli to hym, bi that that he axide; whether we myyten wite that he wolde seie, Brynge ye youre brothir with you?
8 Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
And Judas seide to his fadir, Sende the child with me, that we go, and moun lyue, lest we dien, and oure litle children;
9 Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
Y take the child, require thou hym of myn hoond; if Y schal not brynge ayen, and bitake hym to thee, Y schal be gilti of synne ayens thee in al tyme;
10 Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
if delai hadde not be, we hadden come now anothir tyme.
11 Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
Therfor Israel, `the fadir of hem, seide to hem, If it is nede so, do ye that that ye wolen; `take ye of the beste fruytis of the lond in youre vesselis, and `bere ye yiftis to the man, a litil of gumme, and of hony, and of storax, and of mirre, and of therebynte, and of alemaundis;
12 Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
and `bere ye with you double money, and `bere ye ayen that money which ye founden in baggis, lest perauenture it be doon bi errour;
13 Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
but also take ye youre brother, and go ye to the man;
14 Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
forsothe my God Almyyti mak him pesible to you, and sende he ayen youre brother, whom he holdith in boondis, and this Beniamyn; forsothe Y schal be as maad bare without sones.
15 Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
Therfor the men token yiftis, and double monei, and Beniamyn; and thei yeden doun in to Egipt, and stoden bifore Joseph.
16 Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
And whanne he hadde seyn `hem and Beniamyn togidere, he comaundide the dispendere of his hows, and seide, Lede these men in to the hous, and sle beestis, and make a feeste; for thei schulen ete with me to dai.
17 Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
He dide as it was comaundid, and ledde the men in to the hows;
18 Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
and there thei weren aferd, and seiden to gidere, We ben brouyt in for the monei which we baren ayen bifore in oure sackis, that he putte chalenge `in to vs, and make suget bi violence to seruage bothe vs and oure assis.
19 Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
Wherfor thei neiyeden in the `yatis, and spaken to the dispendere,
20 “Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
Lord, we preien that thou here vs; we camen doun now bifore that we schulden bie metis;
21 koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
whanne tho weren bouyt, whanne we camen to the ynne, we openeden oure baggis, and we founden money in the mouth of sackis, which money we han brouyt ayen now in the same weiyte;
22 Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
but also we han brouyt other siluer, that we bie tho thingis that ben nedeful to vs; it is not in oure conscience, who puttide the money in oure pursis.
23 Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
And he answerde, Pees be to you, nyle ye drede; youre God and God of youre fadir yaf to you tresouris in youre baggis; for I haue the monei preued, which ye yauen to me. And he ledde out Symeon to hem;
24 Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
and whanne thei weren brouyt in to the hows, he brouyte watir, and thei waischiden her feet, and he yaf `meetis to her assis.
25 Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
Sotheli thei maden redi yiftis til Joseph entride at myd day, for thei hadden herd that thei schulden ete breed there.
26 Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
Therfor Joseph entride in to his hows, and thei offriden yiftis to hym, and helden in the hondis, and worschipiden lowe to erthe.
27 Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
And he grette hem ayen mekeli; and he axide hem, and seide, Whether youre fadir, the elde man, is saaf, of whom ye seiden to me? lyueth he yit?
28 Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
Whiche answeriden, He is hool, thi seruaunt oure fadir lyueth yit; and thei weren bowid, and worschipiden hym.
29 Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
Forsothe Joseph reyside hise iyen, and siy Beniamyn his brother of the same wombe, and seide, Is this youre litil brother, of whom ye seiden to me? And eft Joseph seide, My sone, God haue merci of thee.
30 Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
And Joseph hastide in to the hous, for his entrailis weren moued on his brother, and teeris brasten out, and he entride into a closet, and wepte.
31 Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
And eft whanne the face was waischun, he yede out, and refreynede hym silf, and seide, Sette ye looues.
32 Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
`And whanne tho weren set to Joseph by hym silf, and to the britheren bi hem silf, and to Egipcyans that eeten to gidre by hem silf; for it is vnleueful to Egipcians to ete with Ebrewis, and thei gessen sich a feeste vnhooli.
33 Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
Therfor thei saten bifore hym, the firste gendrid bi the rite of his firste gendryng, and the leeste bi his age; and thei wondriden greetli,
34 Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.
whanne the partis weren takun whiche thei hadden resseyued of him, and the more part cam to Beniamyn, so that it passide in fyue partis; and thei drunken, and weren fillid with him.

< Genesis 43 >