< Genesis 42 >

1 Yakobo atamva kuti ku Igupto kuli tirigu, anati kwa ana ake, “Nʼchifukwa chiyani mukungoyangʼanana wina ndi mnzake?
A Jakov videæi da ima žita u Misiru, reèe sinovima svojim: šta gledate jedan na drugoga?
2 Ine ndamva kuti ku Igupto kuli tirigu. Pitani kumeneko mukatigulireko kuti tisafe ndi njala.”
I reèe: eto èujem da u Misiru ima žita; idite onamo te nam kupite otuda, da ostanemo živi i ne pomremo.
3 Choncho abale ake khumi a Yosefe anapita kukagula tirigu ku Igupto.
I desetorica braæe Josifove otidoše da kupe žita u Misiru.
4 Koma Yakobo sanamulole Benjamini mngʼono wake wa Yosefe kuti apite nawo chifukwa anaopa kuti choyipa chingamuchitikire.
A Venijamina brata Josifova ne pusti otac s braæom govoreæi: da ga ne bi zadesilo kakvo zlo.
5 Choncho ana a Israeli aja anapita pamodzi ndi gulu la anzawo kukagula tirigu pakuti ku Kanaani kunalinso njala.
I doðoše sinovi Izrailjevi da kupe žita s ostalima koji dolažahu; jer bješe glad u zemlji Hananskoj.
6 Pakuti Yosefe anali nduna yayikulu yolamulira dziko la Igupto, ndiye kuti analinso amene ankagulitsa tirigu kwa anthu onse. Choncho abale ake a Yosefe nawonso anabwera, ndipo anamugwadira pansi.
A Josif upravljaše zemljom, i prodavaše žito svemu narodu po zemlji. I braæa Josifova došavši pokloniše mu se licem do zemlje.
7 Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.”
A Josif ugledav braæu svoju pozna ih; ali se uèini da ih ne poznaje, i oštro im progovori i reèe: odakle ste došli? A oni rekoše: iz zemlje Hananske, da kupimo hrane.
8 Ngakhale Yosefe anawazindikira abale ake, koma iwo sanamuzindikire.
Josif dakle pozna braæu svoju; ali oni njega ne poznaše.
9 Pamenepo anakumbukira maloto aja amene analota za iwo ndipo anati, “Inu ndinu akazitape! Mwabwera kudzazonda dziko lathu kuti muone pamene palibe chitetezo.”
I opomenu se Josif sanova koje je snio za njih; i reèe im: vi ste uhode; došli ste da vidite gdje je zemlja slaba.
10 Iwo anayankha, “Ayi mbuye wathu, antchito anufe tabwera kudzagula chakudya.
A oni mu rekoše: nijesmo, gospodaru; nego sluge tvoje doðoše da kupe hrane.
11 Tonse ndife ana a munthu mmodzi. Ndife antchito anu okhulupirika osati akazitape.”
Svi smo sinovi jednoga èovjeka, pošteni ljudi, nigda nijesu sluge tvoje bile uhode.
12 Iye anawawuza kuti, “Ayi! Inu mwabwera kudzaona pamene palibe chitetezo mʼdziko muno.”
A on im reèe: nije istina, nego ste došli da vidite gdje je zemlja slaba.
13 Koma iwo anayankha, “Tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri. Abambo athu ndi mmodzi, ndipo kwathu ndi ku Kanaani. Panopo wotsiriza ali ndi abambo athu ndipo wina anamwalira.”
A oni rekoše: nas je bilo dvanaest braæe, sluga tvojih, sinova jednoga èovjeka u zemlji Hananskoj; i eno, najmlaði je danas kod oca našega, a jednoga nema više.
14 Yosefe anawawuza kuti, “Ndi momwe ndaneneramo: Inu ndinu akazitape.
A Josif im reèe: kažem ja da ste vi uhode.
15 Ndiye ndikuyesani motere: Ine ndikulumbira pali Farao ndithu, inuyo simudzachoka malo ano mpaka wotsirizayo atabwera kuno.
Nego hoæu da se uvjerim ovako: tako živ bio Faraon, neæete izaæi odavde dokle ne doðe amo najmlaði brat vaš.
16 Tumizani mmodzi wa inu akamutenge mʼbale wanuyo ndipo ena nonsenu musungidwa mʼndende, kuti titsimikize ngati zimene mukunenazi ndi zoona. Apo ayi, pali Farao ndithu, inu ndinu akazitape!”
Pošljite jednoga izmeðu sebe neka dovede brata vašega, a vi æete ostati ovdje u tamnici, pa æu vidjeti je li istina što govorite; inaèe ste uhode, tako živ bio Faraon!
17 Ndipo onse anawayika mʼndende kwa masiku atatu.
I zatvori ih u tamnicu na tri dana.
18 Pa tsiku lachitatu Yosefe anawawuza kuti, “Popeza ine ndimaopa Mulungu, ndipo inuyo ngati mukufuna kukhala ndi moyo muchite izi:
A treæi dan reèe im Josif: ako ste radi životu, ovo uèinite, jer se ja Boga bojim:
19 Ngati muli anthu achilungamo, mmodzi wa inu atsale mʼndende, pamene ena nonse mupite kwanu kuti muwatengere chakudya anthu akwanu kuli njalako.
Ako ste pošteni ljudi, jedan brat izmeðu vas neka ostane u tamnici, a vi idite i odnesite žita koliko treba porodicama vašim.
20 Mukabwere naye kuno mngʼono wanu wotsirizayo kuti titsimikizire zimene munanena kuti musafe.” Ndipo anachita zomwezo.
Pa onda dovedite k meni najmlaðega brata svojega da se posvjedoèe rijeèi vaše i da ne izginete. I oni uèiniše tako.
21 Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Ndithu ife tinalakwira mʼbale wathu uja popeza kuti ngakhale tinaona kuvutika kwake ndi kumva kulira kwake pamene ankatidandaulira kuti timuchitire chifundo, koma ife sitinamvere. Nʼchifukwa chake masautso awa atigwera.”
I rekoše jedan drugom: doista se ogriješismo o brata svojega, jer vidjesmo muku duše njegove kad nam se moljaše, pa ga se oglušismo; zato doðe na nas ova muka.
22 Rubeni anayankha, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musamuchite kanthu mnyamata uja? Koma inu simunamvere! Tsopano tikulandira malipiro a magazi ake.”
A Ruvim odgovori im govoreæi: nijesam li vam govorio: nemojte se griješiti o dijete? ali me ne poslušaste; i zato se evo traži od nas krv njegova.
23 Koma sanadziwe kuti Yosefe ankawamva popeza kuti ankagwiritsa ntchito wotanthauzira poyankhula naye.
A oni ne znadijahu da ih Josif razumije, jer se s njim razgovarahu preko tumaèa.
24 Yosefe anapita pambali payekha kukalira. Kenaka anabweranso nadzayankhula nawo. Iye anatenga Simeoni namumanga iwo akuona.
A Josif okrete se od njih, i zaplaka se. Potom se opet okrete k njima, i progovori s njima, i uzev izmeðu njih Simeuna veza ga pred njima.
25 Yosefe analamula kuti awadzazire matumba awo ndi tirigu, awayikiremo ndalama zawo momwemo ndiponso awapatse chakudya cha panjira. Izi anawachitiradi.
I zapovjedi Josif da im naspu vreæe žita, pa i novce što je koji dao da metnu svakome u vreæu, i da im dadu brašnjenice na put. I tako bi uèinjeno.
26 Abale a Yosefe aja anasenzetsa abulu awo tirigu amene anagula uja ndipo ananyamuka ulendo wawo.
I natovarivši žito svoje na magarce svoje otidoše.
27 Atafika pamalo pena poti agone, mmodzi mwa iwo anatsekula thumba lake kuti atapemo chakudya cha bulu wake. Atangomasula anaona kuti ndalama zake zili pakamwa pa thumba.
A jedan od njih otvoriv svoju vreæu da nahrani magarca svojega u jednoj gostionici, vidje novce svoje ozgo u vreæi.
28 Iye anati kwa abale akewo, “Ndalama zanga andibwezera, izi zili mʼthumba mwangamu.” Mitima yawo inachita ngati yachokamo ndipo anali ndi mantha ambiri, nati, “Ndi chiyani chimene Mulungu watichitira?”
I reèe braæi svojoj: ja dobih natrag novce svoje, evo ih u mojoj vreæi. I zadrhta srce u njima i uplašiše se govoreæi jedan drugome: što nam to uèini Bog?
29 Atafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani anafotokoza zonse zimene zinawachitikira nati,
I došavši k Jakovu ocu svojemu u zemlju Hanansku, pripovjediše mu sve što im se dogodi, govoreæi:
30 “Nduna yayikulu ya mʼdzikomo inatiyankhula mwa ukali kwambiri ndipo inkatiyesa kuti ndife akazitape.
Oštro govoraše s nama èovjek, koji zapovijeda u onoj zemlji, i doèeka nas kao uhode.
31 Koma tinamuwuza kuti, ‘Ndife anthu woona mtima osati akazitape.
A kad mu rekosmo: mi smo pošteni ljudi, nigda nijesmo bili uhode;
32 Ife tonse tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri, abambo mmodzi. Mmodzi anamwalira, ndipo wamngʼono ali ndi abambo athu ku Kanaani.’”
Bilo nas je dvanaest braæe, sinova oca našega; jednoga veæ nema, a najmlaði je danas kod oca našega u zemlji Hananskoj;
33 Ndipo nduna ija inati kwa ife, “Kuti ndidziwedi kuti ndinu anthu owona mtima muchite izi: Mmodzi mwa inu atsale ndi ine kuno, ndipo enanu mutenge chakudya ndi kubwerera kwanu kumene kuli njalako.
Reèe nam èovjek, koji zapovijeda u onoj zemlji: ovako æu doznati jeste li pošteni ljudi: brata jednoga izmeðu sebe ostavite kod mene, a što vam treba za porodice vaše gladi radi, uzmite i idite.
34 Koma mundibweretsere wotsirizayo kuti ndidziwedi kuti sindinu akazitape koma anthu achilungamo. Kenaka ndidzakubwezerani mʼbale wanuyu ndipo mukhoza kuchita malonda mʼdzikoli.”
Poslije dovedite k meni brata svojega najmlaðega, da se uvjerim da nijeste uhode nego pošteni ljudi; brata æu vam vratiti, i moæi æete trgovati po ovoj zemlji.
35 Pamene amakhuthula matumba awo a tirigu aliyense anapeza kuti kathumba kake ka ndalama kali momwemo. Ataona zimenezi, iwo pamodzi ndi abambo awo anachita mantha kwambiri.
A kad izruèivahu vreæe svoje, gle, svakome u vreæi bjehu u zavežljaju novci njegovi; i vidjevši zavežljaje novaca svojih uplašiše se i oni i otac im.
36 Abambo awo Yakobo anawawuza kuti, “Mwandilanda ana anga ine. Yosefe anamwalira ndipo Simeoni palibenso, ndiye tsopano mukufuna mutengenso Benjamini. Zonsezi zandigwera ine!”
I reèe im Jakov otac njihov: potrste mi djecu; Josifa nema, Simeuna nema, pa hoæete i Venijamina da uzmete; sve se skupilo na me.
37 Koma Rubeni anati kwa abambo ake, “Ngati sindidzabwera naye kwa inu, mudzaphe ana anga aamuna awiri. Muperekeni mʼmanja mwangamu ndipo ndidzamusamala ndi kubwera naye kwa inu.”
A Ruvim progovori i reèe ocu svojemu: dva sina moja ubij, ako ti ga ne dovedem natrag; daj ga u moje ruke, i ja æu ti ga opet dovesti.
38 Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.” (Sheol h7585)
A on reèe: neæe iæi sin moj s vama, jer je brat njegov umro i on osta sam, pa ako bi ga zadesilo kako zlo na putu na koji æete iæi, svalili biste me stara s tugom u grob. (Sheol h7585)

< Genesis 42 >