< Genesis 39 >

1 Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
A Josifa odvedoše u Misir; i Petefrije dvoranin Faraonov, zapovjednik stražarski, èovjek Misirac, kupi ga od Ismailjaca, koji ga odvedoše onamo.
2 Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
I Gospod bješe s Josifom, te bi sreæan, i življaše u kuæi gospodara svojega Misirca.
3 Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
I gospodar njegov vidje da je Gospod s njim i da sve što radi Gospod vodi u napredak u ruci njegovoj.
4 Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
I Josif steèe milost u njega, i dvoraše ga; a najposlije postavi ga nad cijelijem domom svojim, i što god imaše njemu dade u ruke.
5 Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
A kad ga postavi nad domom svojim i nad svijem što imaše, od tada Gospod blagoslovi dom toga Misirca radi Josifa; i blagoslov Gospodnji bješe na svemu što imaše u kuæi i u polju.
6 Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
I ostavi u Josifovijem rukama sve što imaše, i ne razbiraše ni za što osim jela koje jeðaše. A Josif bijaše lijepa stasa i lijepa lica.
7 Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
I dogodi se poslije, te se žena gospodara njegova zagleda u Josifa, i reèe: lezi sa mnom.
8 Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
A on ne htje, nego reèe ženi gospodara svojega: eto gospodar moj ne razbira ni za što što je u kuæi, nego što god ima dade meni u ruke.
9 Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
Ni sam nije veæi od mene u ovoj kuæi, i ništa ne krije od mene osim tebe, jer si mu žena; pa kako bih uèinio tako grdno zlo i Bogu zgriješio?
10 Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
I ona govoraše take rijeèi Josifu svaki dan, ali je ne posluša da legne s njom ni da se bavi kod nje.
11 Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
A jedan dan kad doðe Josif u kuæu da radi svoj posao, a ne bješe nikoga od domašnjih u kuæi,
12 Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
Ona ga uhvati za haljinu govoreæi: lezi sa mnom. Ali on ostaviv joj u rukama haljinu svoju pobježe i otide.
13 Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
A kad ona vidje gdje joj ostavi u rukama haljinu svoju i pobježe,
14 iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
Viknu èeljad svoju, i reèe im govoreæi: gledajte, doveo nam je èovjeka Jevrejina da nas sramoti; doðe k meni da legne sa mnom, a ja povikah iza glasa;
15 Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
A on kad èu gdje vièem, ostavi haljinu svoju kod mene i pobježe i otide.
16 Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
I ona ostavi haljinu njegovu kod sebe dok mu gospodar doðe kuæi.
17 Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
A tada mu reèe ovako govoreæi: sluga Jevrejin, kojega si nam doveo, doðe k meni da me osramoti;
18 Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
A ja povikah iza glasa, te on ostaviv haljinu svoju kod mene pobježe.
19 Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
A kad gospodar njegov èu rijeèi žene svoje gdje mu reèe: to mi je uèinio sluga tvoj, razgnjevi se vrlo.
20 Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
I gospodar Josifov uhvati ga, i baci ga u tamnicu, gdje ležahu sužnji carski; i bi ondje u tamnici.
21 koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
Ali Gospod bješe s Josifom i raširi milost svoju nad njim i uèini te omilje tamnièaru.
22 Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
I povjeri tamnièar Josifu sve sužnje u tamnici, i što je god trebalo ondje èiniti on ureðivaše.
23 Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.
I tamnièar ne nadgledaše ništa što bješe u Josifovoj ruci, jer Gospod bješe s njim; i što god èinjaše, Gospod voðaše u napredak.

< Genesis 39 >