< Genesis 31 >

1 Yakobo anamva zimene ana aamuna a Labani ankanena kuti, “Yakobo watenga chilichonse cha abambo athu ndipo wapeza chuma chonsechi pogwiritsa ntchito chuma cha abambo athu.”
A Jakov èu gdje sinovi Lavanovi govore: Jakov uze sve što bješe našega oca, i od onoga što bješe našega oca steèe sve ovo blago.
2 Choncho Yakobo anaona kuti Labani sankamuonetsanso nkhope yabwino monga kale.
I vidje Jakov gdje lice Lavanovo nije prema njemu kao prije.
3 Pamenepo Yehova anati kwa Yakobo, “Bwerera ku dziko la makolo ako ndi kwa abale ako, ndipo Ine ndidzakhala nawe.”
I Gospod reèe Jakovu: vrati se u zemlju otaca svojih i u rod svoj, i ja æu biti s tobom.
4 Choncho Yakobo anatumiza mawu kukayitana Rakele ndi Leya kuti abwere ku busa kumene ankaweta ziweto zake.
I poslav Jakov dozva Rahilju i Liju u polje k stadu svojemu.
5 Iye anawawuza kuti, “Abambo anu sakundionetsanso nkhope yabwino monga kale, koma Mulungu wa makolo anga wakhala ali nane.
I reèe im: vidim gdje lice oca vašega nije prema meni kao prije; ali je Bog oca mojega bio sa mnom.
6 Inu mukudziwa kuti ndagwirira ntchito abambo anu ndi mphamvu zanga zonse,
I vi znate da sam služio ocu vašemu kako sam god mogao;
7 chonsecho abambo anu akhala akundinyenga posintha malipiro anga kakhumi konse. Komabe Mulungu sanalole kuti andichitire choyipa
A otac me je vaš varao i mijenjao mi platu deset puta; ali mu Bog ne dade da me ošteti;
8 Pamene abambo anu anati, ‘Zamawangamawanga zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana amawangamawanga; ndipo pamene anati, ‘Zamichocholozi zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana a michocholozi.
Kad on reèe: što bude šareno neka ti je plata, onda se mladilo sve šareno; a kad reèe: s biljegom što bude neka ti je plata, onda se mladilo sve s biljegom.
9 Motero Mulungu walanda abambo anu ziweto zawo ndi kundipatsa.
Tako Bog uze stoku ocu vašemu i dade je meni;
10 “Pa nthawi imene ziweto zimatenga mawere ndinalota maloto, ndipo ndinaona kuti atonde onse amene ankakwerawo anali amichocholozi, amawangamawanga kapena amathothomathotho
Jer kad se upaljivaše stoka, podigoh oèi svoje i vidjeh u snu, a to ovnovi i jarci što skaèu na ovce i koze bijahu šareni, s biljegama prutastim i kolastim.
11 Kutulo komweko, mngelo wa Mulungu anati, ‘Yakobo.’ Ine ndinayankha, ‘Ee, Ambuye.’
A anðeo Gospodnji reèe mi u snu: Jakove! A ja odgovorih: evo me.
12 Ndipo iye anati, ‘Tayangʼana ndipo taona kuti atonde onse okwerana ndi ziweto ali amichocholozi, amawangamawanga kapena a mathothomathotho, popeza ndaona zonse zimene Labani wakhala akukuchitira.
A on reèe: podigni sad oèi svoje i gledaj, ovnovi i jarci što skaèu na ovce i koze, šareni su, s biljegama prutastim i kolastim; jer vidjeh sve što ti èini Lavan.
13 Ine ndine Mulungu amene ndinadza kwa iwe pa Beteli paja. Beteli ndi kumalo kuja kumene unayimika mwala ndi kuwudzoza mafuta, komanso kulumbira kwa Ine. Tsopano choka mʼdziko lino msanga ndi kubwerera ku dziko la kwanu.’”
Ja sam Bog od Vetilja, gdje si prelio kamen i uèinio mi zavjet; ustani sada i idi iz ove zemlje, i vrati se na postojbinu svoju.
14 Pamenepo Rakele ndi Leya anayankha, “Kodi ngati ife tilinso ndi gawo ngati cholowa pa chuma cha abambo athu?
Tada odgovori Rahilja i Lija, i rekoše mu: eda li još imamo kakav dio i našljedstvo u domu oca svojega?
15 Kodi abambo athu samationa ife ngati alendo? Iwo anatigulitsa ndi kuwononga ndalama zonse anazipeza pa ifezo.
Nije li nas držao kao tuðinke kad nas je prodao? pa je još i naše novce jednako jeo.
16 Chuma chonse chimene Mulungu walanda abambo athu, ndi chathu ndi ana athu. Tsono inu chitani zimene Mulungu wakuwuzani.”
Jer sve ovo blago što uze Gospod ocu našemu, naše je i naše djece. Zato èini sve što ti je Gospod kazao.
17 Pamenepo Yakobo anakonzeka nakweza ana ake ndi akazi ake pa ngamira,
I podiže se Jakov, i metnu djecu svoju i žene svoje na kamile;
18 anakusa ziweto zake zonse patsogolo natenga katundu wake yense amene anamupeza ku Padanaramu, ndipo ananyamuka kupita ku Kanaani, ku dziko la abambo ake, Isake.
I odvede svu stoku svoju i sve blago što bješe stekao, stoku koju bješe stekao u Padan-Aramu, i poðe k Isaku ocu svojemu u zemlju Hanansku.
19 Labani atachoka pa khomo kupita kukameta nkhosa, mʼmbuyomu Rakele anaba timafano ta milungu ta abambo ake.
A Lavan bješe otišao da striže ovce svoje; i Rahilja ukrade idole ocu svojemu.
20 Komanso nthawi iyi nʼkuti Yakobo atamunamiza Labani Mwaramu posamuwuza zoona kuti afuna kuthawa.
I Jakov otide kradom od Lavana Sirina ne javivši mu da hoæe da ide.
21 Choncho anathawa ndi zonse anali nazo. Ananyamuka nawoloka mtsinje wa Yufurate kupita cha ku Giliyadi, dziko la mapiri.
I pobježe sa svijem blagom svojim, i podiže se te prijeðe preko vode, i uputi se ka gori Galadu.
22 Patapita masiku atatu, Labani anawuzidwa kuti Yakobo wathawa.
A treæi dan javiše Lavanu da je pobjegao Jakov.
23 Pomwepo anatengana ndi abale ake namulondola Yakobo kwa masiku asanu ndi awiri ndipo anakamupezera ku Giliyadi, dziko la mapiri.
I uze sa sobom braæu svoju, i poðe za njim u potjeru, i za sedam dana stiže ga na gori Galadu.
24 Koma Mulungu anabwera kwa Labani, Mwaramu kutulo usiku nati kwa iye, “Samala kuti usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.”
Ali Bog doðe Lavanu Sirinu noæu u snu, i reèe mu: èuvaj se da ne govoriš s Jakovom ni lijepo ni ružno.
25 Pamene Labani amamupeza Yakobo, nʼkuti Yakobo atamanga matenti ake ku mapiri a dziko la Giliyadi. Nayenso Labani ndi abale ake anamanga matenti awo komweko.
I stiže Lavan Jakova; a Jakov bješe razapeo šator svoj na gori, pa i Lavan takoðer razape svoj s braæom svojom na gori Galadu.
26 Tsono Labani anati kwa Yakobo, “Kodi ndakuchita chiyani kuti iwe undinamize ndi kutenga ana anga ngati anthu ogwidwa ku nkhondo?
I Lavan reèe Jakovu: šta uèini te kradom pobježe od mene i odvede kæeri moje kao na maè otete?
27 Chifukwa chiyani unandinamiza ndi kuthawa mozemba wosandiwuza? Ukanandiwuza, bwezi titatsanzikana mwa chisangalalo ndi kuyimba nyimbo ndi zisekese ndi azeze.
Zašto tajno pobježe i kradom otide od mene? niti mi reèe da te ispratim s veseljem i s pjesmama, s bubnjima i guslama?
28 Sunandilole kuti ndingopsompsona adzukulu anga ndi ana anga aakazi motsanzikana nawo. Unachita zopusa.
Niti mi dade da izljubim sinove svoje i kæeri svoje? ludo si radio.
29 Ndili nayo mphamvu yakukuchita choyipa; koma usiku wapitawu, Mulungu wa abambo ako wandiwuza ine kuti, ‘Usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.’
Mogao bih vam dosaditi; ali Bog oca vašega noæas mi reèe govoreæi: èuvaj se da ne govoriš s Jakovom ni lijepo ni ružno.
30 Ndikudziwa kuti unachoka chifukwa unapukwa kufuna kubwerera kwanu kwa abambo ako. Koma nʼchifukwa chiyani unaba milungu yanga?”
Idi dakle kad si se tako uželio kuæe oca svojega; ali zašto ukrade bogove moje?
31 Yakobo anayankha Labani kuti, “Ine ndinkaopa chifukwa ndinkaganiza kuti mukhoza kundilanda anawa.
A Jakov odgovori i reèe: bojah se i mišljah: hoæeš silom oteti kæeri svoje od mene.
32 Koma mukapeza wina aliyense ndi milungu yanu, ameneyo sakhala ndi moyo. Anthu onse akupenya, lozani chilichonse chanu chimene chili ndi ine, ndipo ngati muchipeze tengani. Koma Yakobo sankadziwa kuti Rakele anabadi milunguyo.”
A bogove svoje u koga naðeš, onaj neka ne živi više; pred našom braæom traži što je tvoje u mene, pa uzmi. Jer Jakov nije znao da ih je ukrala Rahilja.
33 Choncho Labani analowadi mu tenti ya Yakobo, ya Leya ndi mʼmatenti a adzakazi awiri aja, koma sanapeze kalikonse. Atatuluka mu tenti ya Leya, analowa ya Rakele.
I uðe Lavan u šator Jakovljev i u šator Lijin i u šator dviju robinja, i ne naðe ih; i izašav iz šatora Lijina uðe u šator Rahiljin.
34 Koma Rakele anatengadi milungu ija ndi kuyiika mʼkati mwa chokhalira cha pa ngamira, iye nʼkukhalapo. Choncho Labani anafunafuna mu tenti monse koma wosapeza kanthu.
A Rahilja uze idole i sakri ih pod samar kamile svoje i sjede ozgo; i Lavan pipaše po cijelom šatoru, i ne naðe.
35 Rakele anati kwa abambo ake, “Pepanitu musandikwiyire mbuye wanga chifukwa choti sinditha kuyimirira pamaso panu chifukwa ndili kumwezi.” Choncho Labani anafunafuna koma sanayipeze milungu ija.
A ona reèe ocu svojemu: nemoj se srditi, gospodaru, što ti ne mogu ustati, jer mi je što u žena biva. Traživ dakle ne naðe idola svojih.
36 Yakobo anapsa mtima nafunsa Labani mwaukali kuti, “Kodi ndalakwa chiyani? Ndi tchimo lanji limene ndachita kuti muchite kundisaka chonchi?
I Jakov se rasrdi, i stade koriti Lavana, i govoreæi reèe mu: šta sam uèinio, šta sam skrivio, te si me tako žestoko tjerao?
37 Chifukwa chiyani mwafunyulula katundu wanga? Ndipo mwapeza chiyani cha inu pamenepa? Chimene mwapezapo chiyikeni poyera pamaso pa abale anu ndi anga kuti atiweruze.
Pipao si sav prtljag moj, pa šta si našao iz svoje kuæe? daj ovamo pred moju i svoju braæu, neka rasude izmeðu nas dvojice.
38 “Ndakhala nanu kwa zaka makumi awiri tsopano ndipo nkhosa ndi mbuzi zanu sizinapoloze, kapena ine kudyapo nkhosa za mʼkhola mwanu.
Evo dvadeset godina bijah kod tebe: ovce tvoje i koze tvoje ne jaloviše se, a ovnova iz stada tvojega ne jedoh.
39 Chiweto chikakhadzulidwa ndi chirombo, sindinkabwera nacho kwa inu. Ineyo ndinkalipira. Inuyo munkandilipiritsa kalikonse kobedwa masana kapena usiku.
Što bi zvijerje zaklalo nijesam ti donosio, sam sam podmirivao; od mene si iskao što bi mi bilo ukradeno danju ili noæu.
40 Moyo wanga unali wotere: Dzuwa limanditentha masana ndipo usiku ndimazunzika ndi kuzizira. Tulo sindimalipeza konse.
Danju me ubijaše vruæina a noæu mraz; i san mi ne padaše na oèi.
41 Zinthu zinali chonchi kwa zaka makumi awiri zimene ndinali mʼnyumba mwanu. Ndinakugwirirani ntchito kwa zaka khumi ndi zinayi chifukwa cha ana anu aakazi awiri ndipo zaka zina zisanu ndi chimodzi chifukwa cha ziweto zanu, ndipo munandisinthira malipiro kakhumi konse.
Tako mi je bilo dvadeset godina u tvojoj kuæi; služio sam ti èetrnaest godina za dvije kæeri tvoje i šest godina za stoku tvoju, i platu si mi mijenjao deset puta.
42 Akanapanda kukhala nane Mulungu wa abambo anga, Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu amene Isake ankamuopa, mosakayika inu mukanandichotsa chimanjamanja. Koma Mulungu waona zovuta zanga ndi kulimbikira ntchito kwanga, ndipo usiku wapitawu anakudzudzulani.”
Da nije Bog oca mojega, Bog Avramov, i strah Isakov bio sa mnom, bi me zacijelo otpustio prazna. Ali je Bog vidio nevolju moju i trud ruku mojih, pa te ukori noæas.
43 Labani anayankha Yakobo nati, “Ana aakaziwa ndi anga, ana awo ndi anganso. Ziwetozi ndi zanga. Chilichonse ukuona apa ndi changa. Koma tsopano ndingachite chiyani ndi ana anga aakaziwa kapena ndi ana awo?
A Lavan odgovori Jakovu i reèe: ove su kæeri moje kæeri, i ovi su sinovi moji sinovi, i ova stoka moja stoka, i što god vidiš sve je moje; pa šta bih uèinio danas kæerima svojim ili sinovima njihovijem koje rodiše?
44 Tsono, tiye tichite pangano pakati pa iwe ndi ine, ndipo likhale mboni pakati pathu.”
Nego hajde da uhvatimo vjeru, ja i ti, da bude svjedoèanstvo izmeðu mene i tebe.
45 Choncho Yakobo anayimiritsa mwala ngati chipilala.
I Jakov uze kamen i utvrdi ga za spomen.
46 Nati kwa abale ake, “Tutani miyala ina.” Choncho anawunjika miyalayo, ndipo anadya chakudya atakhala pa mbali pa muluwo.
I reèe Jakov braæi svojoj: nakupite kamenja. I nakupiše kamenja i složiše na gomilu, i jedoše na gomili.
47 Labani anawutcha muluwo Yegara-sahaduta, ndipo Yakobo anawutcha Galeeda.
I Lavan ga nazva Jegar-Sahadut, a Jakov ga nazva Galed.
48 Labani anati, “Mulu uwu ndi mboni pakati pa inu ndi ine lero.” Ndi chifukwa chake unatchedwa Galeeda.
I reèe Lavan: ova gomila neka bude svjedok izmeðu mene i tebe danas. Zato se prozva Galed.
49 Unatchedwanso Mizipa, chifukwa iye anati, “Yehova aonetsetsa kuti palibe mmodzi mwa ife adzaswe panganoli ngakhale titatalikirana.
A prozva se i Mispa, jer reèe Lavan: neka Gospod gleda izmeðu mene i tebe, kad ne uzmožemo vidjeti jedan drugoga.
50 Ngati ukazunza ana anga kapena kukwatira akazi enanso, ngakhale kuti palibe wina amene ali nafe pano, koma kumbukira kuti Mulungu ndiye mboni pakati pathu.”
Ako ucvijeliš kæeri moje i ako uzmeš žene preko mojih kæeri, neæe èovjek biti izmeðu nas, nego gle Bog svjedok izmeðu mene i tebe.
51 Labani anatinso kwa Yakobo, “Taona pano pali miyala ndi chipilala chimene ndayimika pakati pa iwe ndi ine.
I još reèe Lavan Jakovu: gledaj ovu gomilu i gledaj ovaj spomenik, koji podigoh izmeðu sebe i tebe.
52 Mulu wa miyala uwu ndi chipilalachi ndi mboni. Ine sindidzadutsa mulu wa miyalawu kudzalimbana ndi iwe. Iwenso usadzadutse mulu wa miyalawu kudzalimbana nane.
Svjedok je ova gomila i svjedok je ovaj spomenik: da ni ja neæu prijeæi preko ove gomile k tebi ni ti k meni da neæeš prijeæi preko ove gomile i spomenika ovoga na zlo.
53 Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori ndiye adzatiweruze.” Choncho Yakobo analumbira mʼdzina la Mulungu amene Isake, abambo ake ankamuopa.
Bog Avramov i bogovi Nahorovi, bogovi oca njihova, neka sude meðu nama. A Jakov se zakle strahom oca svojega Isaka.
54 Yakobo anapereka nsembe pa phiri paja, ndipo anayitana abale ake kuti adzadye chakudya. Atadya chakudya anagona pa phiri pomwepo.
I Jakov prinese žrtvu na gori, i sazva braæu svoju na veèeru; i jedoše pa noæiše na gori.
55 Mmamawa wake, Labani anapsompsona zidzukulu zake ndi ana ake nawadalitsa. Kenaka ananyamuka kubwerera ku mudzi.
A ujutru rano usta Lavan, i izljubi svoju unuèad i kæeri svoje, i blagoslovi ih, pa otide i vrati se u svoje mjesto.

< Genesis 31 >