< Genesis 26 >

1 Tsono kunagwa njala ina mʼdzikomo kuwonjezera pa ija ya poyamba ya nthawi ya Abrahamu ndipo Isake anapita kwa Abimeleki mfumu ya Afilisti ku Gerari.
Ali nasta glad u zemlji svrh prve gladi koja bješe za vremena Avramova; i Isak otide k Avimelehu caru Filistejskom u Gerar.
2 Yehova anadza kwa Isake nati, “Usapite ku Igupto; koma ukhale mʼdziko limene ndidzakuwuza kuti ukakhalemo.
I javi mu se Gospod i reèe: nemoj iæi u Misir, nego sjedi u zemlji koju æu ti kazati.
3 Khala mʼdziko lino ndipo ndidzakhala nawe ndi kukudalitsa. Pakuti kwa iwe ndi zidzukulu zako ndidzapereka mayiko onsewa. Choncho ndidzakwaniritsa pangano limene ndinalumbira kwa Abrahamu, abambo ako.
Sjedi u toj zemlji, i ja æu biti s tobom, i blagosloviæu te; jer æu tebi i sjemenu tvojemu dati sve ove zemlje, i potvrdiæu zakletvu, kojom sam se zakleo Avramu ocu tvojemu.
4 Zidzukulu zako ndidzazichulukitsa ngati nyenyezi za mu mlengalenga ndi kuzipatsa mayiko onsewa. Ndiponso anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako,
I umnožiæu sjeme tvoje da ga bude kao zvijezda na nebu, i daæu sjemenu tvojemu sve ove zemlje; i u sjemenu tvojem blagosloviæe se svi narodi na zemlji.
5 chifukwa Abrahamu anandimvera, nasunga malamulo anga onse.”
Zato što je Avram slušao glas moj i èuvao naredbu moju, zapovijesti moje, pravila moja i zakone moje.
6 Choncho Isake anakhala ku Gerari.
I osta Isak u Geraru.
7 Anthu akumaloko atafunsa Isake za mkazi wake, iye anati, “Ndi mlongo wanga ameneyu.” Iye anaopa kunena kuti, “Ndi mkazi wanga ameneyu,” popeza ankaganiza kuti anthu akumeneku akhoza kumupha ndi kukwatira mkazi wake popeza Rebeka anali wokongola.
A ljudi u mjestu onom pitahu za ženu njegovu, a on govoraše: sestra mi je. Jer se bojaše kazati: žena mi je; da me, veli, ne ubiju ovi ljudi radi Reveke, jer je lijepa.
8 Isake atakhalako kumeneko nthawi yayitali, Abimeleki mfumu ya Afilisti, anasuzumira pa zenera kuyangʼana kunja, ndipo anaona Isake akugwiragwira Rebeka, mkazi wake.
I kad provede mnogo vremena ondje, dogodi se, te pogleda Avimeleh car Filistejski s prozora, i vidje Isaka gdje se šali s Revekom ženom svojom.
9 Choncho Abimeleki anamuyitanitsa Isake nati, “Uyu ndi mkazi wako ndithu! Nanga bwanji umati, ‘Ndi mlongo wanga’?” Ndipo Isake anamuyankha kuti, “Ine ndimaganiza kuti ndingataye moyo wanga chifukwa cha iyeyu.”
I dozva Avimeleh Isaka i reèe: ta to ti je žena; kako si kazao: sestra mi je? A Isak mu odgovori: rekoh: da ne poginem s nje.
10 Tsono Abimeleki anati, “Nʼchiyani chimene watichitira? Mmodzi mwa anthuwa anatsala pangʼono kugona ndi mkazi wako ndipo ukanatisandutsa ife kukhala olakwa.”
A Avimeleh reèe: šta si nam uèinio? lako je mogao ko od naroda ovoga leæi s tvojom ženom, te bi nas ti uvalio u grijeh.
11 Choncho Abimeleki analamula anthu ake onse nati, “Aliyense amene avutitse munthu uyu pamodzi ndi mkazi wake adzaphedwa ndithu.”
I zapovjedi Avimeleh svemu narodu svojemu govoreæi: ko se dotakne ovoga èovjeka ili žene njegove, poginuæe.
12 Isake anadzala mbewu mʼmunda, ndipo chaka chomwecho anakolola zinthu zambiri chifukwa Yehova anamudalitsa.
I Isak stade sijati u onoj zemlji, i dobi one godine po sto, tako ga blagoslovi Gospod.
13 Isake analemera. Chuma chake chinkachulukirachulukira mpaka anasanduka munthu wolemera kwambiri.
I obogati se èovjek, i napredovaše sve veæma, te posta silan.
14 Anali ndi nkhosa, ngʼombe ndi antchito ambiri mwakuti Afilisti anamuchitira nsanje.
I imaše ovaca i goveda i mnogo sluga; a Filisteji mu zaviðahu,
15 Nthawi iyi nʼkuti Afilisti atakwirira ndi dothi zitsime zonse zimene antchito abambo ake Abrahamu anakumba mu nthawi ya abambo akewo.
Pa sve studence koje bjehu iskopale sluge oca njegova za vremena Avrama oca njegova zaroniše Filisteji, i zasuše ih zemljom.
16 Ndipo Abimeleki anati kwa Isake, “Muchoke pakati pathu chifukwa mwasanduka wamphamvu kuposa ife.”
I Avimeleh reèe Isaku: idi od nas, jer si postao silniji od nas.
17 Choncho Isake anachokako kumeneko nakakhala ku chigwa cha Gerari kumene anakhazikikako.
I Isak otide odande, i razape šatore u dolini Gerarskoj, i nastani se ondje.
18 Isake anafukulanso zitsime zija zimene zinakumbidwa mu nthawi ya abambo ake Abrahamu. Atamwalira Abrahamu, Afilisti anakwirira zitsimezi. Tsono anazitcha mayina omwewo amene abambo ake anazitcha.
I stade Isak otkopavati studence, koji bjehu iskopani za vremena Avrama oca njegova, i koje zaroniše Filisteji po smrti Avramovoj; i prozva ih imenima koja im bješe nadio otac njegov.
19 Antchito a Isake anakumba mʼchigwamo ndipo anapezamo kasupe wa madzi.
I kopajuæi sluge Isakove u onom dolu naðoše studenac žive vode.
20 Koma abusa a ku Gerari anakangana ndi abusa a Isake nati, “Madziwa ndi athu.” Motero iye anachitcha chitsimecho Mkangano chifukwa anakangana naye.
Ali se svadiše pastiri Gerarski s pastirima Isakovim govoreæi: naša je voda. I nadjede ime onom studencu Esek, jer se svadiše s njim.
21 Kenaka iwo anakumba chitsime china, koma anakangananso chifukwa cha chitsimecho. Choncho anachitcha dzina lakuti Chidani.
Poslije iskopaše drugi studenac, pa se i oko njega svadiše, zato ga nazva Sitna.
22 Anachokapo pamenepo nakakumba china. Koma apa sanakanganiranenso ndi munthu. Iye anachitcha Kutakasuka, nati, “Tsopano Yehova watipatsa ife malo otakasukirako ndipo tilemera muno.”
Tada se podiže odande, i iskopa drugi studenac, i oko njega ne bi svaðe; zato ga nazva Rehovot, govoreæi: sad nam dade Gospod prostora da rastemo u ovoj zemlji.
23 Kenaka Isake anachoka ku malo kuja kupita ku Beeriseba.
I otide odande gore u Virsaveju.
24 Usiku umenewo Yehova anadza kwa Isake nati, “Ine ndine Mulungu wa abambo ako Abrahamu. Usachite mantha popeza Ine ndili ndi iwe. Ndidzakudalitsa ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri chifukwa cha mtumiki wanga Abrahamu.”
I istu noæ javi mu se Gospod, i reèe: ja sam Bog Avrama oca tvojega. Ne boj se, jer sam ja s tobom, i blagosloviæu te i umnožiæu sjeme tvoje Avrama radi sluge svojega.
25 Isake anamanga guwa lansembe pamenepo ndipo anapembedza Yehova. Pomwepo anamanga tenti yake, ndipo antchito ake anakumba chitsime.
I naèini ondje žrtvenik, i prizva ime Gospodnje; i ondje razape šator svoj; i sluge Isakove iskopaše ondje studenac.
26 Abimeleki pamodzi ndi Ahuzati mlangizi wake ndi Fikolo mkulu wa ankhondo ake anabwera kwa Isake kuchokera ku Gerari.
I doðe k njemu Avimeleh iz Gerara s Ohozatom prijateljem svojim i s Fiholom vojvodom svojim.
27 Tsopano Isake anawafunsa kuti, “Bwanji mwabwera kwa ine, popeza munandichitira nkhanza ndi kundithamangitsa?”
A Isak im reèe: što ste došli k meni, kad mrzite na me i otjeraste me od sebe?
28 Iwo anayankha, “Tsopano tadziwa kuti Yehova anali ndi iwe; ndiye taganiza kuti inu ndi ife tichite lumbiro. Ife tichite pangano ndi inu
A oni rekoše: vidjesmo zaista da je Gospod s tobom, pa rekosmo: neka bude zakletva izmeðu nas, izmeðu nas i tebe; hajde da uhvatimo vjeru s tobom:
29 kuti inu simudzatichitira zoyipa monga ifenso sitinakuchitireni nkhondo. Ife tinakuchitirani zabwino zokhazokha, ndipo tinakulolani kuti musamuke kuchoka kwathu mu mtendere. Tsopano Yehova wakudalitsani.”
Da nam ne èiniš zla, kao što se mi tebe ne dotakosmo i kao što mi tebi samo dobro èinismo, i pustismo te da ideš na miru, i eto si blagosloven od Gospoda.
30 Tsono Isake anawakonzera phwando, ndipo anadya ndi kumwa.
Tada ih on ugosti; te jedoše i piše.
31 Mmawa wake aliyense analumbira pangano kwa mnzake. Tsono Isake anawalola kuti anyamuke ndipo anamusiya mu mtendere.
A sjutradan ustavši rano, zakleše se jedan drugome, i otpusti ih Isak i otidoše od njega s mirom.
32 Tsiku limenelo, antchito a Isake anabwera namuwuza za chitsime chimene anakumba. Iwo anati, “Tawapeza madzi!”
Isti dan došavši sluge Isakove kazaše mu za studenac koji iskopaše, i rekoše mu: naðosmo vodu.
33 Iye chitsimecho anachitcha Pangano. Nʼchifukwa chake mzindawu umatchedwa Beeriseba mpaka lero.
I nazva ga Saveja; otuda se zove grad onaj Virsaveja do današnjega dana.
34 Pamene Esau anali ndi zaka 40, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Mhiti. Anakwatiranso Basemati mwana wa mkazi wa Eloni Mhiti.
A kad bi Isavu èetrdeset godina, uze za ženu Juditu kæer Veoha Hetejina, i Vasematu kæer Elona Hetejina.
35 Akazi awiriwa anasandutsa Isake ndi Rebeka kukhala ndi moyo wa madandawulo nthawi zonse.
I one zadavahu mnogo jada Isaku i Reveci.

< Genesis 26 >