< Genesis 24 >

1 Tsopano Abrahamu anali atakalamba kwambiri, ndipo Yehova anamudalitsa mu zonse anachita.
Et Abraham était vieux, avancé en âge, et l'Éternel avait béni Abraham en toute chose.
2 Tsiku lina Abrahamu anawuza wantchito wake wamkulu amene ankayangʼanira zonse anali nazo, kuti “Ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga.
Alors Abraham dit à son serviteur, le plus ancien de sa maison, qui avait le gouvernement de tout ce qui lui appartenait: Pose ta main sous ma hanche,
3 Ndikufuna kuti ulumbire pamaso pa Yehova, Mulungu wakumwamba ndi dziko lapansi, kuti sudzamupezera mwana wanga mkazi pakati pa atsikana Achikanaani a kuno kumene ndikukhala,
afin que je t'adjure au nom de l'Éternel, Dieu des cieux et Dieu de la terre, de ne choisir pour la femme de mon fils aucune des filles des Cananéens au milieu desquels je demeure,
4 koma kuti udzapita ku dziko la kwathu ndi kukamupezera mkazi mwana wanga Isake pakati pa abale anga.”
mais d'aller dans mon pays et dans ma patrie choisir une femme pour mon fils Isaac.
5 Wantchito uja anafunsa kuti, “Nanga atakhala kuti mkaziyo sakufuna kubwera nane kuno? Kodi ine ndingadzatenge mwana wanu ndi kubwerera naye ku dziko kumene munachokera?”
Alors le serviteur lui dit: Peut-être la femme ne voudra-t-elle pas me suivre dans ce pays-ci: dois-je pour lors reconduire ton fils dans le pays d'où tu es sorti?
6 Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.
Et Abraham lui dit: Garde-toi d'y reconduire mon fils!
7 Yehova Mulungu wakumwamba amene ananditenga kwa makolo anga nanditulutsa mʼdziko lobadwira, ameneyo anayankhula nane molumbira kuti, ‘Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko ili.’ Iyeyu adzatumiza mngelo wake kuti akutsogolere kumeneko kukapezera mwana wanga mkazi.
L'Éternel, Dieu du ciel, qui m'a tiré de la maison de mon père, et de ma patrie et qui m'a fait cette promesse et ce serment: Je donnerai ce pays-ci à ta postérité, Lui-même enverra son ange pour te précéder, afin que tu ramènes de là une femme pour mon fils.
8 Ngati mkaziyo adzakana kubwerera nawe ndiye kuti udzakhala womasuka ku lumbiro langa. Koma usadzamutenge mwana wanga ndi kubwerera naye kumeneko.”
Que si la femme ne voulait pas te suivre, alors tu seras libéré de ce serment que je t'impose; seulement ne dois-tu pas reconduire mon fils là.
9 Choncho wantchitoyo anayika dzanja lake pansi pa ntchafu ya mbuye wake Abrahamu nalumbira kwa iye kuti adzachitadi monga mwa mawu a Abrahamu.
Le serviteur posa donc la main sous la hanche d'Abraham, son seigneur, et lui prêta le serment dans ce sens.
10 Tsono wantchito uja anatengapo ngamira khumi mwa ngamira za mbuye wake pamodzi ndi zinthu zabwino za mitundumitundu. Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda wa Nahori, mʼdziko la Mesopotamiya.
Alors le serviteur prit dix chameaux parmi les chameaux de son maître, et il partit chargé de toutes sortes de beaux dons de son seigneur, et il se mit en route et gagna la Mésopotamie, la ville de Nachor.
11 Atafika, anagwaditsa pansi ngamira zija pafupi ndi chitsime chimene chinali kunja kwa mzinda uja. Awa anali madzulo ndithu, nthawi imene amayi amapita kukatunga madzi.
Et il agenouilla les chameaux en dehors de la ville près d'une fontaine au temps de la soirée, au temps où sortent celles qui puisent l'eau.
12 Ndipo wantchito uja anapemphera nati, “Haa, Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, mulole kuti zinthu zindiyendere ine lero, ndipo muonetseni mbuye wanga Abrahamu kukoma mtima kwanu kosasinthika.
Et il dit: Éternel, Dieu de mon seigneur Abraham, daigne me faire rencontrer aujourd'hui, et use de bienveillance envers mon seigneur Abraham!
13 Taonani ndayima pambali pa chitsimechi, ndipo atsikana a mu mzindawu akubwera kudzatunga madzi.
Voici je reste posté près de la fontaine, et les filles des hommes de la ville sortent pour puiser de l'eau.
14 Ine ndipempha mtsikana wina kuti, ‘Chonde tula mtsuko wako kuti ndimweko madzi.’ Tsono iye akayankha kuti ‘Imwani,’ ndipo ndidzapatsanso ngamira zanu madziwo, ameneyo akhale mkazi amene mwasankhira mtumiki wanu Isake.” Zimenezi zikachitika, ndidzadziwa kuti mwaonetsadi kukoma mtima kwanu kosasinthika kwa mbuye wanga.
Or, qu'il se fasse que la jeune fille à qui je dirai: Penche donc ta cruche, afin que je boive, et qui dira: Bois! et j'abreuverai aussi tes chameaux, se trouve être celle que tu as destinée à ton serviteur Isaac; et à cela je reconnaîtrai que tu uses de bienveillance envers mon seigneur.
15 Asanatsirize kupemphera, anangoona Rebeka watulukira atasenza mtsuko wake pa phewa. Iyeyu anali mwana wa Betueli mwana wa Milika, mkazi wa Nahori mʼbale wake wa Abrahamu.
Et il n'avait pas encore achevé de parler que voici venir Rebecca, qui était née à Béthuel, fils de Milca, femme de Nachor, frère d'Abraham, sa cruche sur son épaule.
16 Mtsikanayo anali wokongola kwambiri, namwali amene sanadziwe mwamuna. Iye anatsikira ku chitsime nadzaza mtsuko nakweranso ku mtunda.
Or la jeune fille était très belle de figure, encore vierge, et nul homme ne l'avait connue. Et elle descendit à la fontaine, et emplit sa cruche et remonta.
17 Wantchito uja anathamanga kukakumana naye nati, “Chonde patseko madzi pangʼono a mu mtsuko wakowo kuti ndimwe.”
Alors le serviteur courut au-devant d'elle, et dit: Laisse-moi donc boire un peu d'eau de ta cruche!
18 Mtsikanayo anati, “Imwani mbuye wanga.” Ndipo mofulumira anatsitsa mtsuko uja nawuyika mʼmanja ndi kumupatsa kuti amwe.
Et elle répondit: Bois, mon seigneur! et vite elle abaissa sa cruche sur sa main et lui donna à boire.
19 Atatha kupereka madzi akumwa kwa mlendo uja, mtsikanayo anati, “Ndikatungiranso ngamira madzi kuti zimwe mpaka zitakwana.”
Et après l'avoir entièrement désaltéré, elle dit: Je puiserai aussi pour tes chameaux jusqu'à ce qu'ils soient entièrement abreuvés.
20 Choncho anafulumira kukhuthula madzi a mu mtsuko aja momwera ziweto, nathamanga kubwerera ku chitsime kukatunga madzi ena, ndipo anatunga okwanira ngamira zake zonse.
Et vite elle vida sa cruche dans l'auge, et courut encore à la fontaine pour puiser, et elle puisa pour tous ses chameaux.
21 Modekha, munthu uja anayangʼanitsitsa kwambiri mtsikana uja kuti adziwedi ngati Yehova anamutsogolera pa ulendo wake uja kapena ayi.
Et l'homme la contemplait en silence pour voir si l'Éternel donnerait ou non du succès à son voyage.
22 Ngamira zija zitatha kumwa, mlendo uja anatulutsa chipini chagolide cholemera theka la sekeli ndi zibangiri zagolide ziwiri zolemera masekeli 100.
Et lorsque les chameaux eurent fini de s'abreuver, l'homme prit un anneau d'or, pesant un demi-sicle, et deux bracelets pour ses poignets, du poids de dix sicles d'or,
23 Kenaka anafunsa namwaliyo kuti, “Chonde tandiwuza, kodi ndiwe mwana wa yani? Ndipo kodi malo alipo kwanu woti ife nʼkugona?”
et dit: De qui es-tu fille? Indique-le moi donc! Y a-t-il pour nous dans la maison de ton père une place où passer la nuit?
24 Anamuyankha kuti, “Ine ndine mwana wa Betueli, mwana amene Milika anaberekera Nahori.”
Et elle lui répondit: Je suis fille de Béthuel, fils de Milca, que celle-ci a enfanté à Nachor.
25 Ndipo anapitiriza kunena kuti, “Chakudya chodyetsa nyamazi chilipo kwathu ndipo malo woti mugone aliponso.”
Et elle lui dit: Et paille et fourrage sont en abondance chez nous, et il y a gîte aussi pour passer la nuit.
26 Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,
Alors l'homme s'inclina et se prosterna devant l'Éternel,
27 nati, “Alemekezeke Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene waonetsa kukoma mtima kwake kosasintha ndi kukhulupirika kwake kwa mbuye wanga. Yehova wanditsogolera pa ulendo wanga mpaka ndafika ku nyumba kwa abale ake a mbuye wanga.”
et dit: Béni soit l'Éternel, Dieu de mon seigneur Abraham, qui ne s'est pas départi de son amour et de sa fidélité envers mon seigneur! Pour moi, l'Éternel m'a guidé sur la route de la maison des frères de mon seigneur.
28 Mtsikana uja anathamanga nakafotokozera zimenezi anthu a kwa amayi ake.
Et la jeune fille courut informer de ces choses la maison de sa mère.
29 Tsono Rebeka anali ndi mlongo wake dzina lake Labani.
Or Rebecca avait un frère, dont le nom était Laban. Et Laban accourut vers l'homme dehors à la fontaine.
30 Iyeyu atangoona chipini pa mphuno ndi zibangiri pa mikono ya mlongo wake komanso kumva zimene mlendo uja ananena kwa Rebekayo, anathamangira kwa mlendo uja, ndipo anamupeza atangoyima ndi ngamira zake pafupi ndi chitsime.
Et ayant vu l'anneau et les bracelets aux mains de sa sœur, et entendu les discours de Rebecca, sa sœur, qui disait: Ainsi m'a parlé cet homme, il vint auprès de l'homme; et voici, il se tenait près de ses chameaux à la fontaine.
31 Iye anati, “Tiyeni kwathu, ndinu munthu amene Yehova wamudalitsa. Bwanji mwangoyimirira panja pano? Ine ndakukonzerani malo ogona inu ndi ngamira zanu.”
Et il dit: Entre, béni de l'Éternel! pourquoi te tiens-tu dehors? J'ai disposé la maison, et il y a place pour les chameaux.
32 Choncho munthu uja analowa mʼnyumba. Labani anatsitsa katundu anali pa ngamira uja. Kenaka anazipatsa ngamira zija chakudya, ndiponso anapereka madzi wosamba mapazi kwa mlendo uja ndi anthu ena onse.
Et l'homme entra dans la maison; et [Laban] débâta les chameaux, et donna de la paille et du fourrage pour les chameaux, et de l'eau pour laver ses pieds et les pieds des gens de sa suite.
33 Chakudya chitabwera mlendo uja anati, “Sindidya mpaka nditakuwuzani zimene ndadzera kuno.” Labani anati, “Yankhulani.”
Et on lui servit à manger. Mais il dit: Je ne mangerai point que je n'aie dit ce que j'ai à dire.
34 Motero iye anati, “Ine ndine wantchito wa Abrahamu.
Et [Laban] répondit: Parle! Et il dit: Je suis serviteur d'Abraham.
35 Yehova wadalitsa mbuye wanga kwambiri, ndiponso walemera. Wamupatsa nkhosa ndi ngʼombe, siliva ndi golide, antchito aamuna ndi antchito aakazi, komanso ngamira ndi abulu.
Et l'Éternel a grandement béni mon seigneur qui a est un homme considérable, et auquel Il a donné des brebis et des bœufs et de l'argent et de l'or et des serviteurs et des servantes, et des chameaux et des ânes.
36 Sara, mkazi wa mbuye wanga anamubalira iye mwana wamwamuna ngakhale kuti Sarayo anali wokalamba. Tsono mbuye wanga wamupatsa mwanayo chuma chonse.
Et Sarah, femme d'Abraham, mon seigneur, a dans sa vieillesse enfanté un fils à mon seigneur, et il lui a donné tout ce qu'il possède.
37 Tsono mbuye wanga anandilumbiritsa kuti ndisunge mawu ake akuti, ‘Usadzamupezere mwana wanga mkazi kuchokera mwa atsikana a dziko lino la Kanaani,
Et mon seigneur m'a adjuré en ces termes: Tu ne choisiras pour femme de mon fils aucune des filles des Cananéens dont j'habite le pays;
38 koma upite ku banja la abambo anga ndi kwa abale anga kuti ukamupezere mkazi mwana wanga.’”
mais tu te rendras dans la maison de mon père et dans ma famille, et tu y choisiras une femme pour mon fils.
39 “Ndipo ine ndinati kwa mbuye wanga, ‘Nanga mkaziyo akakapanda kubwera nane pamodzi?’
Et je dis à mon seigneur: Peut-être la femme ne voudra-t-elle pas me suivre!
40 “Iye anayankha, ‘Yehova amene ndakhala ndikumumvera nthawi zonse, adzatumiza mngelo wake kuti akuperekeze ndipo adzakuthandiza mpaka ukamupezere mwana wanga mkazi kuchokera ku mtundu wanga, wa fuko langa.
Et il me dit: L'Éternel en la présence de qui j'ai marché, enverra son ange avec toi, et fera réussir ton voyage, et tu prendras une femme pour mon fils dans ma famille et dans la maison de mon père.
41 Ukadzachita zimenezi udzakhala mfulu wosamangidwa ndi lumbiro langali. Koma tsono ukadzafika kwa fuko langa, ndipo ngati sadzalola kukupatsa mbeta ya mwana wanga, aponso udzamasuka ku lumbiro langali.’”
Alors tu seras libéré du serment que tu me fais, si tu vas t'adresser à ma famille; et si on ne te l'accorde pas, tu seras libéré du serment que tu me fais.
42 “Tsono lero lino pamene ndafika pa chitsime, ndinapempha kuti, ‘Yehova, Mulungu wa mbuye wanga, Abrahamu, ngati Inu mwandidalitsadi pa ulendowu,
Et en arrivant aujourd'hui à la fontaine, j'ai dit: Éternel, Dieu de mon seigneur Abraham, si tu daignes faire réussir mon voyage que je fais:
43 taonani ndayima pambali pa chitsime ichi; ndipo ndidzati kwa namwali amene atabwere kudzatunga kuti, chonde nditamwako madzi a mu mtsuko wakowu,’
voici, je me tiendrai près de la fontaine; et qu'il se fasse que la jeune fille sortant pour puiser de l'eau, à qui je dirai: Laisse-moi donc boire un peu d'eau de ta cruche,
44 ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”
et qui me répondra: Bois toi-même, et je puiserai aussi pour tes chameaux, se trouve être la femme que l'Éternel a destinée au fils de mon seigneur.
45 “Ndisanatsirize kupemphera, ndinangoona Rebeka akutulukira mtsuko wake uli pa phewa. Anatsetserekera ku chitsime kukatunga madzi ndipo ndinati kwa iye, ‘Chonde patseko madzi akumwa.’
Je n'avais pas encore fini de parler en mon cœur que voilà que Rebecca sort, la cruche sur l'épaule, et descend à la fontaine et puise; et je lui dis: Donne-moi donc à boire!
46 “Mofulumira, anatsitsa mtsuko wake pa phewa pake nati, ‘Imwani ndiponso ndizimwetsa madzi ngamira zanuzi.’ Kotero ine ndinamwa ndipo anamwetsanso ngamirazo.
Et vite elle abaissa sa cruche de dessus son épaule et dit: Bois, et j'abreuverai aussi tes chameaux, et je bus et elle abreuva aussi les chameaux.
47 “Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,
Puis je lui fis cette question: De qui es-tu fille? Et elle répondit: De Béthuel, fils de Nachor à qui Milca l'a enfanté. Et je mis l'anneau à sa narine, et les bracelets à ses poignets.
48 kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
Et je m'inclinai et me prosternai devant l'Éternel, et je bénis l'Éternel, Dieu de mon seigneur Abraham, qui m'a guidé dans la vraie voie pour marier la fille du frère de mon seigneur à son fils.
49 Tsono ngati mukufuna kuonetsa kukoma mtima kwanu kwa mbuye wanga, ndikuonetsa kukhulupirika kwanu, ndiwuzeni; ndipo ngati si choncho ndiwuzeninso kuti ndidziwe chochita.”
Et maintenant, si votre intention est de témoigner à mon seigneur bienveillance et fidélité, déclarez-le-moi; dans le cas contraire, déclarez-le-moi, afin que je me tourne à droite ou à gauche.
50 Labani ndi Betueli anayankha nati, “Izi ndi zochokera kwa Yehova, ndipo ife sitinganenepo kanthu.
Alors Laban et Béthuel répondirent et dirent: Ceci procède de l'Éternel; nous ne pouvons rien te dire ni en mal, ni en bien.
51 Nayu Rebeka, mutengeni muzipita naye kuti akakhale mkazi wa mwana wa mbuye wanu, monga Yehova wanenera.”
Voilà Rebecca devant toi; prends-la et t'en va, et qu'elle devienne la femme du fils de ton seigneur, ainsi qu'a prononcé l'Éternel.
52 Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.
Et lorsque le serviteur d'Abraham entendit leur discours, il se prosterna contre terre devant l'Éternel.
53 Kenaka wantchitoyo anatulutsa ziwiya zagolide ndi zasiliva ndi zovala nazipereka kwa Rebeka. Anaperekanso mphatso zina za mtengowapatali kwa mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka.
Et le serviteur sortit des joyaux d'argent et des joyaux d'or, et des habillements, et les donna à Rebecca, et il donna des objets de prix à son frère et à sa mère.
54 Tsono wantchito uja ndi anthu amene anali naye anadya, kumwa nagona komweko. Kutacha mmawa wake, wantchito uja anati, “Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
Alors ils mangèrent et burent, lui et les gens de sa suite, et passèrent la nuit. Et le matin ils se levèrent, et il dit: Laissez-moi retourner vers mon seigneur.
55 Koma mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka anayankha kuti, “Muloleni mtsikanayu abakhala nafe masiku khumi kapena kupyolerapo, kenaka mukhoza kupita.”
Et le frère et la mère de Rebecca dirent: Que la jeune fille reste avec nous quelques jours, soit dix jours; ensuite tu partiras.
56 Koma iye anawawuza kuti, “Chonde musandichedwetse. Yehova wandithandiza kale pa ulendo wanga. Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
Mais il leur dit: Ne me retardez pas! L'Éternel a fait réussir mon voyage, laissez-moi partir, afin que je retourne chez mon seigneur.
57 Koma iwo anati, “Bwanji timuyitane mtsikanayo ndipo timufunse ngati afuna kupita nanu panopa.”
Et ils dirent: Nous appellerons la jeune fille et nous lui demanderons de se prononcer.
58 Choncho iwo anamuyitana Rebeka uja namufunsa kuti, “Kodi ukufuna kupita ndi munthuyu panopa?” Iye anayankha kuti, “Ndipita.”
Et ils appelèrent Rebecca et lui dirent: Vas-tu avec cet homme? Et elle répondit: Je vais.
59 Kotero anamulola Rebeka pamodzi ndi mlezi wake kuti apite ndi wantchito wa Abrahamu pamodzi ndi anthu amene anali naye.
Sur quoi ils laissèrent partir Rebecca, leur sœur, et sa nourrice et le serviteur d'Abraham et son monde.
60 Ndipo iwo anadalitsa Rebeka ndi kumuwuza kuti, “Iwe ndiwe mlongo wathu, Mulungu akudalitse iwe, ukhale mayi wa anthu miyandamiyanda; ndi kuti zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo.”
Et ils bénirent Rebecca et lui dirent: O toi, notre sœur! deviens des milliers de myriades, Et que ta race occupe la porte de tes ennemis!
61 Kenaka Rebeka ndi antchito ake ananyamuka kukakwera ngamira zawo ndipo anapita naye pamodzi munthu uja. Choncho wantchito uja anatenga Rebeka nʼkumapita.
Alors Rebecca et ses femmes se levèrent, et se placèrent sur les chameaux, et suivirent l'homme; et le serviteur ayant pris Rebecca se mit en route.
62 Pa nthawiyi nʼkuti Isake atafika kuchokera ku chitsime cha Wamoyo Wondipenya (Beeri-lahai-roi), popeza tsopano ankakhala ku Negevi.
Cependant Isaac était revenu de la fontaine du Vivant-qui-voit, car il habitait le Midi du pays.
63 Tsiku lina chakumadzulo, Isake anatuluka kukayendayenda ku munda, ndipo atakweza maso anaona ngamira zikubwera.
Et Isaac était sorti pour se livrer à ses pensées dans les champs à l'approche du soir; et il leva les yeux et regarda, et voilà que des chameaux arrivaient.
64 Rebeka nayenso anatukula maso naona Isake. Ndipo anatsika pa ngamira yake
Et Rebecca levant les yeux aperçut Isaac, et elle descendit de son chameau.
65 nafunsa wantchito uja kuti, “Kodi munthu uyo ndi ndani akuyenda mʼmundamo kubwera kudzakumana nafe?” Wantchitoyo anayankha, “Ndiye mbuye wanga.” Choncho Rebeka anatenga nsalu ndi kufunda kumaso.
Et elle dit au serviteur: Qui est cet homme qui s'avance par les champs à notre rencontre? Et le serviteur dit: C'est mon seigneur. Alors elle prit son voile et s'en couvrit.
66 Tsono wantchito uja anawuza Isake zonse zimene anazichita.
Et le serviteur raconta à Isaac toutes les choses qu'il avait faites.
67 Isake analowa naye Rebeka mu tenti ya amayi ake Sara, ndipo anakhala mkazi wake. Isake anamukonda kwambiri Rebeka mkazi wake motero kuti zimenezi zinamutonthoza imfa ya amayi ake.
Et Isaac introduisit Rebecca dans la tente de Sarah, sa mère, et il prit Rebecca, et elle devint sa femme et il l'aima; et Isaac se consola après le deuil de sa mère.

< Genesis 24 >