< Genesis 20 >

1 Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
A Avram otide odande na jug, i stani se izmeðu Kadisa i Sura; i življaše kao došljak u Geraru.
2 ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
I govoraše za ženu svoju Saru: sestra mi je. A car Gerarski Avimeleh posla, te uze Saru.
3 Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
Ali doðe Bog Avimelehu noæu u snu, i reèe mu: gle, poginuæeš sa žene koju si uzeo, jer ima muža.
4 Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
A Avimeleh ne bješe se nje dotakao, i zato reèe: Gospode, eda li æeš i pravedan narod pogubiti?
5 Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
Nije li mi sam kazao: sestra mi je? a i ona sama kaza: brat mi je. Uèinio sam u èistoti srca svojega i u pravdi ruku svojih.
6 Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
Tada mu reèe Bog u snu: znam da si uèinio u èistoti srca svojega, zato te saèuvah da mi ne sagriješiš, i ne dadoh da je se dotakneš.
7 Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
A sada vrati èovjeku ženu njegovu, jer je prorok, i moliæe se za te, te æeš ostati živ. Ako li ne vratiš, znaj da æeš umrijeti ti i svi tvoji.
8 Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
I ujutru rano usta Avimeleh, i sazva sve sluge svoje, i kaza im sve ovo da èuju. I uplašiše se ljudi veoma.
9 Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
Tada Avimeleh dozva Avrama i reèe mu: šta si nam uèinio? šta li sam ti zgriješio, te navuèe na me i na carstvo moje toliko zlo? Uèinio si mi što ne valja èiniti.
10 Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
I još reèe Avimeleh Avramu: šta ti je bilo, te si to uèinio?
11 Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
A Avram odgovori: veljah: jamaèno nema straha Božijega u ovom mjestu, pa æe me ubiti radi žene moje.
12 Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
A upravo i jest mi sestra, kæi oca mojega; ali nije kæi moje matere, pa poðe za me.
13 Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
A kad me Bog izvede iz doma oca mojega, ja joj rekoh: uèini dobro, i kaži za me gdje god doðemo: brat mi je.
14 Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
Tada Avimeleh uze ovaca i goveda i sluga i sluškinja, te dade Avramu, i vrati mu Saru ženu njegovu.
15 Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
I reèe Avimeleh Avramu: evo, zemlja ti je moja otvorena, živi slobodno gdje ti je volja.
16 Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
A Sari reèe: evo dao sam tvojemu bratu tisuæu srebrnika; gle, on ti je oèima pokrivalo pred svima koji budu s tobom; i to sve da ti je za nauku.
17 Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
I Avram se pomoli Bogu, i iscijeli Bog Avimeleha i ženu njegovu i sluškinje njegove, te raðahu.
18 Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.
Jer Gospod bješe sasvijem zatvorio svaku matericu u domu Avimelehovu radi Sare žene Avramove.

< Genesis 20 >