< Genesis 20 >

1 Abrahamu anachokako kumeneko napita ku Negevi ndipo anakakhala ku dziko la Gerari, limene lili pakati pa mzinda wa Kadesi ndi mzinda wa Suri. Anakhala ku Gerari kwa kanthawi,
Abraham yede forth fro thennus in to the lond of the south, and dwellide bitwixe Cades and Sur, and was a pilgrym in Geraris;
2 ndipo Abrahamu ankawawuza za Sara kuti, “Iyeyu ndi mlongo wanga.” Choncho Abimeleki, mfumu wa ku Gerari anamutenga Sara uja.
and he seide of Sare, his wijf, Sche is my sistir. Therfor Abymalec, kyng of Gerare, sente, and took hir.
3 Koma usiku, Mulungu anafika kwa Abimeleki kutulo nati, “Ufatu iwe chifukwa cha mkazi amene watengayu popeza ndi wokwatiwa.”
Sotheli God cam to Abymalec bi a sweuene in the nyyt, and seide to hym, Lo! thou schalt die, for the wooman which thou hast take, for sche hath an hosebond.
4 Nthawi imeneyi nʼkuti Abimeleki asanamukhudze mkaziyo, kotero kuti anati, “Ambuye, kodi mudzawonongadi mtundu wolungama?
Forsothe Abymalech touchide not hir; and he seide, Lord, whether thou schalt sle folc vnkunnynge and iust?
5 Kodi Abrahamu sanandiwuze kuti iyeyu ndi mlongo wake? Ndiponso mkaziyu ankanena kuti Abrahamu ndi mlongo wake. Choncho ine pochita izi, ndinkachita moona mtima ndiponso mopanda chinyengo.”
Whether he seide not to me, Sche is my sistir, and sche seide, He is my brother? In the symplenesse of myn herte, and in the clennesse of myn hondis Y dide this.
6 Tsono kumaloto komweko Mulungu anati kwa iye, “Inde ndikudziwa kuti wachita izi moona mtima, ndipo Ine sindinafune kuti undichimwire. Nʼchifukwa chake sindinakulole kuti umukhudze.
And the Lord seide to hym, And Y woot that thou didist bi symple herte, and therfor Y kepte thee, lest thou didist synne ayens me, and I suffride not that thou touchidist hir;
7 Tsopano kabwezere mkaziyo kwa mwamuna wake. Iyeyu ndi mneneri, ndipo adzakupempherera kuti ukhale ndi moyo. Koma ukapanda kukamupereka, udziwiretu kuti udzafa pamodzi ndi onse a pa banja pako.”
now therfor yelde thou the wijf to hir hosebonde, for he is a profete; and he schal preye for thee, and thou schalt lyue; sotheli if thou nylte yelde, wite thou that thou schalt die bi deeth, thou and alle thingis that ben thine.
8 Mmamawa mwake Abimeleki anayitanitsa akuluakulu ake onse, ndipo atawafotokozera zimene zinachitika, iwo aja anachita mantha kwambiri.
And anoon Abynalech roos bi nyyt, and clepide alle his seruauntis, and spak alle these wordis in the eeris of hem; and alle men dredden greetli.
9 Kenaka Abimeleki anayitana Abrahamu ndipo anati, “Kodi wachita chiyani? Ndakulakwira chiyani kuti undibweretsere ine pamodzi ndi anthu anga chilango chachikulu chotere? Wandichitira zinthu zimene sizinayenera kuchitika.”
Sotheli Abymalec clepide also Abraham, and seide to hym, What hast thou do to vs? what synneden we ayens thee, for thou hast brouyt in on me and on my rewme a greuouse synne? thou hast do to vs whiche thingis thou ouytist not do.
10 Ndipo Abrahamu anafunsa Abimeleki kuti, “Chifukwa chiyani wachita zimenezi?”
And eft Abimalech axide, and seide, What thing seiyist thou, that thou woldist do this?
11 Abrahamu anayankha nati, “Ndinkaganiza kuti kuno kulibiretu munthu woopa Mulungu. Ndiye ndimati mwina adzandipha chifukwa cha mkazi wanga.
Abraham answerde, Y thouyte with me, and seide, in hap the drede of God is not in this place; and thei schulen sle me for my wijf;
12 Komabe kunena zoona, iyeyu ndi mlongo wangadi, mwana wamkazi wa abambo anga ngakhale kuti si ife a mayi mmodzi. Tsono akhoza kukhala mkazi wanga.
in other maner forsothe and sche is my sister verili, the douyter of my fadir, and not the douyter of my moder; and Y weddide hir in to wijf;
13 Ndiye pamene Mulungu anati ndichoke ku nyumba ya abambo anga, ndinawuza mkazi wangayu kuti, ‘Kuti uwonetse kuti ndiwe mkazi wokoma mtima, uziwuza anthu kulikonse kumene tingapite kuti ndine mlongo wako.’”
sotheli aftir that God ladde me out of the hous of my fadir, Y seide to hir, Thou schalt do this mercy with me in ech place to which we schulen entre; thou schalt seie, that Y am thi brother.
14 Tsono Abimeleki anapereka nkhosa, ngʼombe ndi antchito aamuna ndi aakazi kwa Abrahamu. Ndipo anamubwezeranso Abrahamu Sara, mkazi wake.
Therfore Abymelech took scheep, and oxun, and seruauntis, and handmaydenes, and yaf to Abraham; and he yeldide to him Sare, `his wijf, and seide, The lond is bifor you;
15 Tsono Abimeleki anati kwa Abrahamu, “Dziko langa ndi limene ukulionali; ukhale paliponse pamene ufuna.”
dwelle thou, where euere it plesith thee. Forsothe Abymelech seide to Sare, Lo!
16 Ndipo kwa Sara, iye anati, “Ndikumupatsa mlongo wakoyu makilogalamu khumi ndi awiri a siliva kutsimikiza kuti iwe ndi wosalakwa pamaso pa onse amene ali ndi iwe; ulibedi mlandu.”
Y yaf a thousand platis of siluer to thi brother; this schal be to thee in to hiling of iyen to al men that ben with thee; and whider euere thou goist, haue thou mynde that thou art takun.
17 Tsono Abrahamu anapemphera kwa Mulungu ndipo Mulunguyo anachiritsa Abimeleki, mkazi wake pamodzi ndi adzakazi ake kuti athenso kubereka ana.
Sotheli for Abraham preiede, God curide Abymelech, and his wijf, and handmaydens, and thei childiden;
18 Paja Yehova nʼkuti atatseka akazi onse a mʼbanja la Abimeleki kuti asabereke ana chifukwa cha Sara, mkazi wa Abrahamu.
for God hadde closid ech wombe of the hows of Abymelech, for Sare, the wijf of Abraham.

< Genesis 20 >