< Genesis 2 >

1 Motero kumwamba, dziko lapansi ndi zonse za mʼmenemo zinatha kulengedwa monga mwa kuchuluka kwawo.
Tako se dovrši nebo i zemlja i sva vojska njihova.
2 Pofika tsiku lachisanu ndi chiwiri Mulungu anamaliza ntchito zonse zimene ankagwira ndipo pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anapumula ku ntchito zake zonse.
I svrši Bog do sedmoga dana djela svoja, koja uèini; i poèinu u sedmi dan od svijeh djela svojih, koja uèini;
3 Ndipo Mulungu anadalitsa tsiku lachisanu ndi chiwiri nalipatula, chifukwa pa tsiku limeneli Iye anapumula ku ntchito yonse yolenga imene anayigwira.
I blagoslovi Bog sedmi dan, i posveti ga, jer u taj dan poèinu od svijeh djela svojih, koja uèini;
4 Mbiri ya momwe kumwamba ndi dziko lapansi zinalengedwera pa tsiku lija Yehova Mulungu ankazilenga ndi iyi: Yehova Mulungu atapanga dziko lapansi ndi kumwamba,
To je postanje neba i zemlje, kad postaše, kad Gospod Bog stvori zemlju i nebo,
5 zitsamba zinali zisanamere ndipo chomera chilichonse chinali chisanamerenso popeza Yehova Mulungu anali asanagwetse mvula pa dziko lapansi. Panalibe munthu wolima nthaka,
I svaku biljku poljsku, dokle je još ne bješe na zemlji, i svaku travku poljsku, dokle još ne nicaše; jer Gospod Bog još ne pusti dažda na zemlju, niti bješe èovjeka da radi zemlju,
6 koma kasupe ankatuluka mʼnthaka ndi kuthirira pa dziko lonse.
Ali se podizaše para sa zemlje da natapa svu zemlju.
7 Tsono Yehova Mulungu anawumba munthu kuchokera ku dothi nawuziramo mpweya wamoyo mʼmphuno mwake ndipo munthuyo anakhala wamoyo.
A stvori Gospod Bog èovjeka od praha zemaljskoga, i dunu mu u nos duh životni; i posta èovjek duša živa.
8 Kenaka Yehova Mulungu anatsekula munda wa Edeni chakummawa; kumeneko anayikako munthu amene anamupanga uja.
I nasadi Gospod Bog vrt u Edemu na istoku; i ondje namjesti èovjeka, kojega stvori.
9 Ndipo Yehova Mulungu anameretsa mʼmundamo mitengo ya mitundu yonse. Inali mitengo yokongola ndi ya zipatso zokoma. Pakati pa munda uja panali mtengo wopatsa moyo ndi mtengo wopatsa nzeru zodziwitsa chabwino ndi choyipa.
I uèini Gospod Bog, te nikoše iz zemlje svakojaka drveta lijepa za gledanje i dobra za jelo, i drvo od života usred vrta i drvo od znanja dobra i zla.
10 Mtsinje wothirira mundawo unkatuluka mu Edeni; kuchokera apo unkagawikana kukhala mitsinje inayi.
A voda tecijaše iz Edema natapajuæi vrt, i odande se dijeljaše u èetiri rijeke.
11 Dzina la mtsinje woyamba ndi Pisoni; uwu umazungulira dziko lonse la Havila, kumene kuli golide.
Jednoj je ime Fison, ona teèe oko cijele zemlje Evilske, a ondje ima zlata,
12 (Golide wa ku dziko ili ndi wabwino. Kulinso miyala yokongola ya bedola ndi onikisi).
I zlato je one zemlje vrlo dobro; ondje ima i bdela i dragoga kamena oniha.
13 Dzina la mtsinje wachiwiri ndi Gihoni; uwu umazungulira dziko lonse la Kusi.
A drugoj je rijeci ime Geon, ona teèe oko cijele zemlje Huske.
14 Dzina la mtsinje wachitatu ndi Tigirisi; umayenda chakummawa kwa Asiriya. Ndipo mtsinje wachinayi ndi Yufurate.
A treæoj je rijeci ime Hidekel, ona teèe k Asirskoj. A èetvrta je rijeka Efrat.
15 Yehova Mulungu anatenga munthu uja ndi kumuyika mʼmunda wa Edeni kuti awulime ndi kuwusamalira.
I uzevši Gospod Bog èovjeka namjesti ga u vrtu Edemskom, da ga radi i da ga èuva.
16 Ndipo Yehova Mulungu analamula munthu uja kuti, “Uzidya zipatso za mu mtengo wina uliwonse mʼmundamu;
I zaprijeti Gospod Bog èovjeku govoreæi: jedi slobodno sa svakoga drveta u vrtu;
17 koma usadye zipatso za mu mtengo wodziwitsa chabwino ndi choyipa, popeza ukadzadya za mu mtengowu udzafa ndithu.”
Ali s drveta od znanja dobra i zla, s njega ne jedi; jer u koji dan okusiš s njega, umrijeæeš.
18 Ndipo Yehova Mulungu anati, “Sibwino kuti munthu akhale yekha. Ndidzamupangira mnzake womuthandiza.”
I reèe Gospod Bog: nije dobro da je èovjek sam; da mu naèinim druga prema njemu.
19 Kenaka Yehova Mulungu anawumba ndi dothi nyama zonse zakuthengo ndi mbalame zonse zamlengalenga. Ndipo Iye anapita nazo kwa munthu uja kuti akazipatse mayina; ndipo dzina lililonse limene Adamu anapereka ku chamoyo chilichonse, lomwelo linakhala dzina lake.
Jer Gospod Bog stvori od zemlje sve zvijeri poljske i sve ptice nebeske, i dovede k Adamu da vidi kako æe koju nazvati, pa kako Adam nazove koju životinju onako da joj bude ime;
20 Choncho Adamu anazitcha mayina ziweto zonse, mbalame zamlengalenga ndi nyama zakuthengo zonse. Komabe munthu uja analibe mnzake womuthandiza.
I Adam nadjede ime svakom živinèetu i svakoj ptici nebeskoj i svakoj zvijeri poljskoj; ali se ne naðe Adamu drug prema njemu.
21 Tsono Yehova Mulungu anamugonetsa munthu uja tulo tofa nato; ali mtulo chomwecho, Mulungu anachotsa imodzi mwa nthiti zake ndi kutseka pamalopo ndi mnofu.
I Gospod Bog pusti tvrd san na Adama, te zaspa; pa mu uze jedno rebro, i mjesto popuni mesom;
22 Motero Yehova Mulungu anapanga mkazi ndi nthiti ija imene anatenga kwa munthu uja nabwera naye kwa iye.
I Gospod Bog stvori ženu od rebra, koje uze Adamu, i dovede je k Adamu.
23 Munthu uja anati, “Uyu ndiye fupa lochokera ku mafupa anga ndi mnofu wochokera ku mnofu wanga; adzatchedwa ‘mkazi,’ popeza wachokera mwa mwamuna.”
A Adam reèe: sada eto kost od mojih kosti, i tijelo od mojega tijela. Neka joj bude ime èovjeèica, jer je uzeta od èovjeka.
24 Nʼchifukwa chake, mwamuna amasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake ndipo awiriwo amakhala thupi limodzi.
Zato æe ostaviti èovjek oca svojega i mater svoju, i prilijepiæe se k ženi svojoj, i biæe dvoje jedno tijelo.
25 Munthu uja ndi mkazi wakeyo, onse awiri anali maliseche ndipo analibe manyazi.
A bjehu oboje goli, Adam i žena mu, i ne bješe ih sramota.

< Genesis 2 >