< Genesis 19 >

1 Angelo awiri aja anafika ku Sodomu madzulo ndipo Loti anali atakhala pansi pa chipata cha mzindawo. Loti atawaona, anayimirira ndi kukakumana nawo ndipo anaweramitsa mutu wake pansi mwaulemu.
A uveèe doðoše dva anðela u Sodom; a Lot sjeðaše na vratima Sodomskim; i kad ih ugleda, ustade te ih srete, i pokloni se licem do zemlje,
2 Iye anati, “Ambuye wanga, chonde patukirani ku nyumba kwa mtumiki wanu. Mukhoza kusambitsa mapazi anu ndi kugona usiku uno kenaka nʼkumapitirira ndi ulendo wanu mmamawa.” Iwo anati, “Ayi, tigona panja.”
I reèe: hodite, gospodo, u kuæu sluge svojega, i prenoæite i operite noge svoje; pa sjutra rano kad ustanete poðite svojim putem. A oni rekoše: ne, nego æemo prenoæiti na ulici.
3 Koma iye anawawumiriza kwambiri kotero kuti anapita naye pamodzi ku nyumba kwake. Anawakonzera chakudya buledi wopanda yisiti ndipo anadya.
Ali on navali na njih, te se uvratiše k njemu i uðoše u kuæu njegovu, i on ih ugosti, i ispeèe hljebova prijesnijeh, i jedoše.
4 Alendo aja asanapite kogona, amuna onse achinyamata ndi achikulire ochokera mbali zonse za mzinda wa Sodomu anazinga nyumba ya Loti.
I još ne bjehu legli, a graðani Sodomljani slegoše se oko kuæe, staro i mlado, sav narod sa svijeh krajeva,
5 Iwo anayitana Loti namufunsa kuti, “Ali kuti amuna aja amene afika kuno usiku womwe uno? Atulutse, utipatse kuti tigone nawo malo amodzi.”
I vikahu Lota i govorahu mu: gdje su ljudi što doðoše sinoæ k tebi? izvedi ih k nama da ih poznamo.
6 Loti anatuluka panja kukakumana nawo natseka chitseko
A Lot izide k njima pred vrata zatvoriv vrata za sobom,
7 ndipo anati, “Ayi anzanga, musachite zinthu zoyipa zotere.
I reèe im: nemojte, braæo, èiniti zla.
8 Taonani, ine ndili ndi ana anga akazi awiri amene sanagonepo ndi mwamuna. Mundilole ndikutulutsireni amenewo ndipo muchite nawo zimene mungafune. Koma musachite chilichonse ndi anthuwa, pakuti iwowa ndi alendo anga ndipo ndiyenera kuwatchinjiriza.”
Evo imam dvije kæeri, koje još ne poznaše èovjeka; njih æu vam izvesti, pa èinite s njima što vam je volja; samo ne dirajte u one ljude, jer su zato ušli pod moj krov.
9 Iwo anayankha kuti, “Tachoka apa tidutse.” Ndipo anati, “Munthu uyu anabwera kuno ngati mlendo chabe, tsono lero akufuna kuti akhale wotiweruza! Tikukhawulitsa kuposa iwowa.” Anapitiriza kumuwumiriza Loti uja nʼkumasunthira kutsogolo kuti athyole chitseko.
A oni mu rekoše: hodi amo. Pa onda rekoše: ovaj je sam došao amo da živi kao došljak, pa još hoæe da nam sudi; sad æemo tebi uèiniti gore nego njima. Pa navališe jako na èovjeka, na Lota, i stadoše istavljati vrata.
10 Koma anthu aja anali mʼkatiwa anasuzumira namukokera Loti uja mʼkati mwa nyumba nʼkutseka chitseko.
A ona dva èovjeka digoše ruke, i uvukoše Lota k sebi u kuæu, i zatvoriše vrata.
11 Kenaka anawachititsa khungu anthu amene anali panja pa nyumba aja, aangʼono ndi aakulu omwe, kuti asaone pa khomo.
A ljudi što bijahu pred vratima kuænim ujedanput oslijepiše od najmanjega do najveæega, te ne mogahu naæi vrata.
12 Anthu awiri aja anati kwa Loti, “Kodi uli ndi wina aliyense pano, kaya ndi akamwini ako, kaya ndi ana ako aamuna kapena aakazi, kapena aliyense mu mzindamu amene ndi anzako? Atulutse onse muno,
Tada ona dva èovjeka rekoše Lotu: ako imaš ovdje još koga svoga, ili zeta ili sina ili kæer, ili koga god svoga u ovom gradu, gledaj nek idu odavde;
13 chifukwa tiwononga malo ano. Yehova waona kuti kuyipa kwa anthu a mu mzindawu kwakulitsa. Choncho watituma kuti tiwuwononge.”
Jer hoæemo da zatremo mjesto ovo, jer je vika njihova velika pred Gospodom, pa nas posla Gospod da ga zatremo.
14 Choncho Loti anatuluka nayankhula ndi akamwini ake amene anali kuyembekezera kukwatira ana ake akazi nati, “Fulumirani, tiyeni tichoke pa malo ano chifukwa Yehova watsala pangʼono kuwononga mzindawu.” Koma akamwini akewo ankayesa kuti akungoselewula.
I izide Lot, i kaza zetovima svojim, za koje šæaše dati kæeri svoje, i reèe im: ustajte, idite iz mjesta ovoga, jer æe sada zatrti Gospod grad ovaj. Ali se zetovima njegovijem uèini da se šali.
15 Mmene kumacha, angelo aja anamufulumizitsa Loti nati, “Nyamuka, tenga mkazi wako ndi ana ako aakazi awiriwo, ndipo mutuluke mu mzindawo kuopa kuti mungaphedwe pamodzi nawo.”
A kad zora zabijelje, navališe anðeli na Lota govoreæi: ustani, uzmi ženu svoju i dvije kæeri svoje koje su tu, da ne pogineš u bezakonju grada toga.
16 Koma Loti ankakayikabe. Koma Yehova anawachitira chifundo motero kuti anthu aja anagwira mkazi wake ndi ana ake aakazi aja nawatsogolera bwinobwino kuwatulutsa mu mzindawo.
A on se stade šèinjati, te ljudi uzeše za ruku njega i ženu njegovu i dvije kæeri njegove, jer ga bješe žao Gospodu, i izvedoše ga i pustiše iza grada.
17 Atangowatulutsa, mmodzi wa angelowo anati, “Thawani kuti mudzipulumutse, musachewuke, musayime pena paliponse mʼchigwamo! Thawirani ku mapiri kuopa kuti mungawonongeke!”
I kad ih izvedoše napolje, reèe jedan: izbavi dušu svoju i ne obziri se natrag, i u cijeloj ovoj ravni da nijesi stao; bježi na ono brdo, da ne pogineš.
18 Koma Loti anawawuza kuti, “Ayi, ambuye anga chonde musatero!
A Lot im reèe: nemoj, Gospode!
19 Taonani, Inu mwachitira mtumiki wanu chifundo, ndipo mwaonetsa kukoma mtima kwanu pondipulumutsa. Sindingathawire ku mapiri chifukwa chiwonongekochi chikhoza kundipeza ndisanafike ku mapiriko ndipo ndingafe.
Gle, sluga tvoj naðe milosti pred tobom, i milost je tvoja prevelika koju mi uèini saèuvavši mi život; ali ne mogu uteæi na brdo da me ne stigne zlo i ne poginem.
20 Koma, chapafupi pomwepa pali mudzi woti ndikhoza kuthamanga nʼkukafikako. Mundilole ndithawireko, ndi waungʼono kwambiri, si choncho? Mukatero, moyo wanga upulumuka.”
Eno grad blizu; onamo se može uteæi, a mali je; da bježim onamo; ta mali je, te æu ostati živ.
21 Mngeloyo anati kwa iye, “Chabwino, ndavomeranso pempho lako, sindiwononga mudzi ukunenawo.
A on mu reèe: eto poslušaæu te i zato, i neæu zatrti grada, za koji reèe.
22 Koma uthawireko mofulumira chifukwa sindichita kena kalikonse mpaka utafikako.” (Nʼchifukwa chake mudziwo unatchedwa Zowari).
Brže bježi onamo; jer ne mogu èiniti ništa dokle ne stigneš onamo. Zato se prozva onaj grad Sigor.
23 Pamene Loti amafika ku Zowari, nʼkuti dzuwa litatuluka.
I kad sunce ogranu po zemlji, Lot doðe u Sigor.
24 Ndiye Yehova anathira sulufule wamoto wochokera kumwamba kwa Yehova pa Sodomu ndi Gomora.
Tada pusti Gospod na Sodom i na Gomor od Gospoda s neba dažd od sumpora i ognja,
25 Kotero, anawononga mizindayo, chigwa chonse pamodzi ndi onse okhala mʼmizindayo. Anawononganso zomera zonse za mʼdzikolo.
I zatr one gradove i svu onu ravan, i sve ljude u gradovima i rod zemaljski.
26 Koma mkazi wa Loti anachewuka ndipo anasanduka mwala wa mchere.
Ali žena Lotova bješe se obazrela iduæi za njim, i posta slan kamen.
27 Mmawa mwake, Abrahamu ananyamuka nabwerera kumalo kumene anakumana ndi Yehova kuja.
A sjutradan rano ustavši Avram, otide na mjesto gdje je stajao pred Gospodom;
28 Anayangʼana kumunsi ku Sodomu, Gomora ndi ku dziko lonse la ku chigwa, ndipo anaona chiwutsi chikufuka mʼdzikolo ngati chikuchokera mʼngʼanjo.
I pogleda na Sodom i Gomor i svu okolinu po onoj ravni, i ugleda, a to se dizaše dim od zemlje kao dim iz peæi.
29 Choncho Mulungu anawononga mizinda ya ku chigwa, koma anakumbukira pemphero la Abrahamu natulutsa Loti ku sulufule ndi moto zimene zinawononga mizinda ya kumene Loti amakhalako.
Ali kad Bog zatiraše gradove u onoj ravni, opomenu se Bog Avrama, i izvede Lota iz propasti kad zatr gradove gdje življaše Lot.
30 Loti ndi ana ake awiri aakazi anachoka ku Zowari nakakhala ku mapiri, chifukwa amachita mantha kukhala ku Zowari. Iye ndi ana ake awiri ankakhala mʼphanga.
A Lot otide iz Sigora, i stani se na onom brdu s dvije kæeri svoje, jer se bojaše ostati u Sigoru; i življaše u peæini s dvije kæeri svoje.
31 Tsiku lina mwana wake wamkazi wamkulu anawuza mngʼono wake kuti, “Abambo athu ndi wokalamba ndipo palibe mwamuna aliyense pano woti atikwatire ndi kubereka ana monga mwa chikhalidwe cha pa dziko lonse lapansi.
A starija reèe mlaðoj: naš je otac star, a nema nikoga na zemlji da doðe k nama kao što je obièaj po svoj zemlji.
32 Tiye tiwamwetse vinyo ndipo tigone nawo. Tikatero mtundu wathu udzakhalapobe.”
Hajde da damo ocu vina neka se opije, pa da legnemo s njim, eda bismo saèuvale sjeme ocu svojemu.
33 Usiku umenewo analedzeretsa vinyo abambo awo, ndipo wamkuluyo analowa nagona naye. Abambo awo samadziwa kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
I dadoše ocu vina onu noæ; i došavši starija leže s ocem svojim, i on ne osjeti ni kad ona leže ni kad ustade.
34 Tsiku linali mwana wamkazi wamkulu uja anati kwa mngʼono wake, “Usiku wathawu ine ndinagona ndi abambo anga. Tiye tiwaledzeretsenso vinyo usiku uno ndipo iwe upite ndi kugona nawo ndipo mtundu wathu udzakhalapobe.”
A sjutradan reèe starija mlaðoj: gle, noæas spavah s ocem svojim. Da mu damo vina i doveèe, pa idi ti i lezi s njim, eda bismo saèuvale sjeme ocu svojemu.
35 Choncho analedzeranso vinyo abambo awo usiku umenewonso, ndipo mwana wamkazi wamngʼono anapita nagona nawo. Abambo awo sanadziwenso kanthu pamene mwanayo anagona naye kapena pamene anadzuka.
Pa i to veèe dadoše ocu vina i ustavši mlaða leže s njim, i on ne osjeti ni kad ona leže ni kad ustade.
36 Choncho ana onse awiri a Loti aja anatenga pathupi pa abambo awo.
I obje kæeri Lotove zatrudnješe od oca svojega.
37 Mwana wamkazi wamkulu uja anabereka mwana wa mwamuna ndipo anamutcha Mowabu. Iyeyo ndiye kholo la Amowabu onse.
I starija rodi sina, i nadjede mu ime Moav; od njega su Moavci do današnjega dana.
38 Mwana wamkazi wamngʼono naye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha iye Beni-Ammi. Iyeyu ndiye kholo la Aamoni onse.
Pa i mlaða rodi sina, i nadjede mu ime Ven-Amije; od njega su Amonci do današnjega dana.

< Genesis 19 >