< Genesis 17 >

1 Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
Gdy Abram miał dziewięćdziesiąt dziewięć lat, PAN ukazał się Abramowi i powiedział do niego: Ja [jestem] Bogiem Wszechmogącym. Chodź przed moim obliczem i bądź doskonały.
2 Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
A zawrę moje przymierze między mną a tobą i rozmnożę cię bardzo obficie.
3 Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
Wtedy Abram upadł na twarz, a Bóg powiedział do niego:
4 “Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
Oto ja [ustanawiam] moje przymierze z tobą i będziesz ojcem wielu narodów.
5 Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
Nie będziesz już się nazywał Abram, ale twoje imię będzie Abraham, bo ustanowiłem cię ojcem wielu narodów.
6 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
Uczynię cię niezmiernie płodnym i od ciebie wywiodę narody, i od ciebie będą pochodzić królowie.
7 Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
I utwierdzę moje przymierze między mną a tobą oraz twoim potomstwem po tobie przez wszystkie pokolenia jako wieczne przymierze, abym był ci Bogiem i twemu potomstwu po tobie.
8 Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
Dam tobie i twemu potomstwu po tobie ziemię, w której teraz przebywasz, całą ziemię Kanaan, jako własność na wieki, i będę ich Bogiem.
9 Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
Potem Bóg powiedział Abrahamowi: Ty zaś zachowuj moje przymierze, ty i twoje potomstwo po tobie przez wszystkie pokolenia.
10 Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
[A] takie [jest] moje przymierze, które będziecie zachowywać, między mną a wami i między twoim potomstwem po tobie: Każdy mężczyzna wśród was ma być obrzezany.
11 Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
Obrzezacie więc ciało waszego napletka; [to] będzie znakiem przymierza między mną a wami.
12 Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
Każdy syn wśród was w ósmym dniu [życia] będzie obrzezany, każdy mężczyzna przez wszystkie pokolenia, tak narodzony w domu, [jak] i nabyty za pieniądze od jakiegokolwiek cudzoziemca, który nie pochodzi z twego potomstwa.
13 Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
Urodzony w twoim domu i nabyty za twoje pieniądze musi być obrzezany. A moje przymierze będzie na waszym ciele jako wieczne przymierze.
14 Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
A nieobrzezany mężczyzna, któremu nie obrzezano ciała jego napletka, ta dusza będzie wykluczona ze swego ludu, [bo] złamała moje przymierze.
15 Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
Potem Bóg powiedział do Abrahama: Twojej żony Saraj nie będziesz już nazywał imieniem Saraj, ale jej imię będzie Sara.
16 Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
I będę jej błogosławił, i dam ci z niej syna. Będę jej błogosławił i będzie [matką] narodów, i od niej będą pochodzić królowie narodów.
17 Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
Wtedy Abraham upadł na twarz i roześmiał się, i mówił w swoim sercu: Czy stuletniemu człowiekowi urodzi się [syn]? I czy Sara w wieku dziewięćdziesięciu lat urodzi?
18 Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
I Abraham powiedział do Boga: Oby [tylko] Izmael żył przed twoim obliczem!
19 Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
A Bóg powiedział: Naprawdę, twoja żona Sara urodzi ci syna i nadasz mu imię Izaak. I utwierdzę moje przymierze z nim jako wieczne przymierze [i] z jego potomstwem po nim.
20 Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
Co do Izmaela też cię wysłuchałem. Oto błogosławiłem mu i uczynię go płodnym, i rozmnożę go bardzo obficie. Spłodzi on dwunastu książąt i uczynię go wielkim narodem.
21 Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
Ale moje przymierze utwierdzę z Izaakiem, którego Sara urodzi ci za rok o tej porze.
22 Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
Gdy skończył z nim rozmowę, Bóg wzniósł się nad Abrahama.
23 Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
Wtedy Abraham wziął swego syna Izmaela, wszystkich urodzonych w swym domu oraz wszystkich nabytych za pieniądze, wszystkich mężczyzn wśród domowników Abrahama, i obrzezał ciała ich napletków tego samego dnia, jak Bóg mu mówił.
24 Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
Abraham miał dziewięćdziesiąt dziewięć lat, gdy obrzezano ciało jego napletka.
25 ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
A jego syn Izmael miał trzynaście lat, gdy obrzezano ciało jego napletka.
26 Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
Tego samego dnia obrzezano Abrahama i jego syna Izmaela.
27 Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.
I wszyscy mężczyźni jego domu, urodzeni w domu i nabyci za pieniądze od cudzoziemców, zostali obrzezani z nim.

< Genesis 17 >