< Genesis 15 >

1 Zitatha izi, Yehova anayankhula ndi Abramu mʼmasomphenya nati: “Usaope Abramu. Ine ndili ngati chishango chokutchinjiriza. Mphotho yako idzakhala yayikulu.”
And so whanne these thingis weren don, the word of the Lord was maad to Abram bi a visioun, and seide, Abram, nyle thou drede, Y am thi defender, and thi meede is ful greet.
2 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, mukhoza kundipatsa chiyani popeza ndikanali wopanda mwana ndipo amene adzatenge chuma changa ndi Eliezara wa ku Damasiko?
And Abram seide, Lord God, what schalt thou yyue to me? Y schal go with oute fre children, and this Damask, sone of Elieser, the procuratour of myn hous, schal be myn eir.
3 Inu simunandipatse ana kotero kuti wantchito wa ku nyumba kwanga ndiye amene adzalowe mʼmalo mwanga.”
And Abram addide, Sotheli thou hast not youe seed to me, and, lo! my borun seruaunt schal be myn eir.
4 Yehova anayankhula naye nati: “Munthu uyu sadzalowa mʼmalo mwako, koma mwana wako weniweni wamwamuna, wobereka wekha ndiye adzalowe mʼmalo mwako.”
And anoon the word of the Lord was maad to hym, and seide, This schal not be thin eir, but thou schalt haue hym eir, that schal go out of thi wombe.
5 Yehova anapita naye Abramu panja nati, “Tayangʼana kumwambaku, ndipo chifukwa cha chimenechi uwerenge nyenyezi ngati ungathe kuziwerenga.” Ndipo anamuwuza kuti, “Ndi mmene adzakhalire ana ako ndi zidzukulu zako.”
And the Lord ledde out Abram, and seide to hym, Biholde thou heuene, and noumbre thou sterris, if thou maist. And the Lord seide to Abram, So thi seed schal be.
6 Abramu anakhulupirira Yehova, ndipo ichi chinamuchititsa kukhala wolungama.
Abram bileuede to God, and it was arettid to hym to riytfulnesse.
7 Ndipo anamuwuza kuti, “Ine ndine Yehova amene ndinakuchotsa iwe ku mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kuti ndikupatse dziko ili kuti likhale lako.”
And God seide to hym, Y am the Lord, that ladde thee out of Vr of Caldeis, that Y schulde yyue this lond to thee, and thou schuldist haue it in possessioun.
8 Koma Abramu anati, “Haa! Ambuye Yehova, kodi ndingadziwe bwanji kuti lidzakhaladi langa?”
And Abram seide, Lord God, wherbi may I wite that Y schal welde it?
9 Kotero Yehova anati kwa iye, “Kanditengere kamsoti kangʼombe ka zaka zitatu, kamsoti ka mbuzi ka zaka zitatu, ndi nkhosa yayimuna ya zaka zitatu pamodzi ndi nkhunda ndi kamwana ka njiwa.”
And the Lord answerde, and seide, Take thou to me a cow of thre yeer, and a geet of thre yeer, and a ram of thre yeer, a turtle also, and a culuer.
10 Abramu anabweretsadi zonsezi nadula chilichonse pakati nʼkuzindandalika, chidutswa chilichonse kuyangʼanana ndi chinzake; koma njiwa ndi nkhunda sanazidule pakati.
Which took alle these thingis, and departide tho bi the myddis, and settide euer eithir partis ech ayens other; but he departide not the briddis.
11 Pamene miphamba inabwera kuti itole nyama ija, Abramu anayipirikitsa.
And foulis camen doun on the careyns, and Abram drof hem awey.
12 Pamene dzuwa limalowa Abramu anagona tulo tofa nato ndipo mdima wandiweyani ndi wochititsa mantha unamuphimba.
And whanne the sunne was gon doun, drede felde on Abram, and a greet hidousenesse and derk asaylide him.
13 Tsono Yehova anati kwa iye, “Uyenera kudziwa mosakayika kuti zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.
And it was seid to hym, Wite thou bifore knowinge, that thi seed schal be pilgrim foure hundrid yeer in a lond not his owne, and thei schulen make hem suget to seruage, and thei schulen turment hem;
14 Koma ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo ndipo pambuyo pake iwo adzatulukamo ndi chuma chambiri.
netheles Y schal deme the folk to whom thei schulen serue; and aftir these thingis thei schulen go out with greet catel.
15 Komabe iweyo udzamwalira mu mtendere ndi kuyikidwa mʼmanda utakalamba bwino.
Forsothe thou schalt go to thi fadris in pees, and schalt be biried in good age.
16 Patapita mibado inayi, adzukulu ako adzabwereranso kuno popeza tchimo la Aamori silinafike pachimake kuti alangidwe.”
Sotheli in the fourthe generacioun thei schulen turne ayen hidir, for the wickidnesses of Amoreis ben not yit fillid, `til to present tyme.
17 Dzuwa litalowa ndipo mdima utagwa, panaoneka mʼphika wofuka nthunzi ya moto ndi sakali yoyaka ndipo zinadutsa pakati pa zidutswa za nyama zija.
Therfor whanne the sunne was gon doun, a derk myst was maad, and a furneis smokynge apperide, and a laumpe of fier, and passide thorou tho departingis.
18 Pa tsiku limenelo, Yehova anachita pangano ndi Abramu nati, “Ndikulonjeza kuti ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako, kuchokera ku mtsinje wa ku Igupto mpaka ku mtsinje waukulu wa Yufurate.
In that dai the Lord made a couenaunt of pees with Abram, and seide, Y schal yyue to thi seed this lond, fro the ryuer of Egipt til to the greet ryuer Eufrates; Cyneis,
19 Ndidzakupatsani dziko la Akeni, Akenizi, Akadimoni,
and Cyneseis, and Cethmoneis, and Etheis,
20 Ahiti, Aperezi, Arefaimu,
and Fereseis, and Raphaym, and Amorreis,
21 Aamori, Akanaani, Agirigasi ndi Ayebusi.”
and Cananeis, and Gergeseis, and Jebuseis.

< Genesis 15 >