< Genesis 10 >

1 Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
Now these [are] the generations of the sons of Noe, Sem, Cham, Japheth; and sons were born to them after the flood.
2 Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
The sons of Japheth, Gamer, and Magog, and Madoi, and Jovan, and Elisa, and Thobel, and Mosoch, and Thiras.
3 Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
And the sons of Gamer, Aschanaz, and Riphath, and Thorgama.
4 Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
And the sons of Jovan, Elisa, and Tharseis, Cetians, Rhodians.
5 (Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
From these were the islands of the Gentiles divided in their land, each according to his tongue, in their tribes and in their nations.
6 Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
And the sons of Cham, Chus, and Mesrain, Phud, and Chanaan.
7 Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
And the sons of Chus, Saba, and Evila, and Sabatha, and Rhegma, and Sabathaca. And the sons of Rhegma, Saba, and Dadan.
8 Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
And Chus begot Nebrod: he began to be a giant upon the earth.
9 Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
He was a giant hunter before the Lord God; therefore they say, As Nebrod the giant hunter before the Lord.
10 Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
And the beginning of his kingdom was Babylon, and Orech, and Archad, and Chalanne, in the land of Senaar.
11 Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
Out of that land came Assur, and built Ninevi, and the city Rhooboth, and Chalach,
12 ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
and Dase between Ninevi and Chalach: this is the great city.
13 Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
And Mesrain begot the Ludiim, and the Nephthalim, and the Enemetiim, and the Labiim,
14 Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
and the Patrosoniim, and the Chasmoniim (whence came forth Phylistiim) and the Gaphthoriim.
15 Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
And Chanaan begot Sidon his firstborn, and the Chettite,
16 Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
and the Jebusite, and the Amorite, and the Girgashite,
17 Ahivi, Aariki, Asini,
and the Evite, and the Arukite, and the Asennite,
18 Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
and the Aradian, and the Samarean, and the Amathite; and after this the tribes of the Chananites were dispersed.
19 mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
And the boundaries of the Chananites were from Sidon till one comes to Gerara and Gaza, till one comes to Sodom and Gomorrha, Adama and Seboim, as far as Dasa.
20 Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
There [were] the sons of Cham in their tribes according to their tongues, in their countries, and in their nations.
21 Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
And to Sem himself also were children born, the father of all the sons of Heber, the brother of Japheth the elder.
22 Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
Sons of Sem, Elam, and Assur, and Arphaxad, and Lud, and Aram, and Cainan.
23 Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
And sons of Aram, Uz, and Ul, and Gater, and Mosoch.
24 Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
And Arphaxad begot Cainan, and Cainan begot Sala. And Sala begot Heber.
25 A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
And to Heber were born two sons, the name of the one, Phaleg, because in his days the earth was divided, and the name of his brother Jektan.
26 Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
And Jektan begot Elmodad, and Saleth, and Sarmoth, and Jarach,
27 Hadoramu, Uzali, Dikila,
and Odorrha, and Aibel, and Decla,
28 Obali, Abimaeli, Seba,
Eval, and Abimael, and Saba,
29 Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
and Uphir, and Evila, and Jobab, all these were the sons of Jektan.
30 Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
And their dwelling was from Masse, till one comes to Saphera, a mountain of the east.
31 Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
These were the sons of Sem in their tribes, according to their tongues, in their countries, and in their nations.
32 Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.
These are the tribes of the sons of Noe, according to their generations, according to their nations: of them were the islands of the Gentiles scattered over the earth after the flood.

< Genesis 10 >