< Agalatiya 1 >

1 Paulo mtumwi, osati wosankhidwa ndi anthu kapena kutumidwa ndi munthu ayi, koma Yesu Khristu, ndi Mulungu Atate amene anamuukitsa Yesuyo kwa akufa,
İnsanlarca ya da insan aracılığıyla değil, İsa Mesih ve O'nu ölümden dirilten Baba Tanrı aracılığıyla elçi atanan ben Pavlus'tan ve benimle birlikte olan bütün kardeşlerden Galatya'daki kiliselere selam!
2 pamodzi ndi abale onse amene ali nane, Kulembera mipingo ya ku Galatiya:
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale nanu.
Babamız Tanrı'dan ve Rab İsa Mesih'ten sizlere lütuf ve esenlik olsun.
4 Yesuyo anadzipereka yekha chifukwa cha machimo athu kuti atipulumutse ku njira za moyo woyipa uno, molingana ndi chifuniro cha Mulungu ndi Atate athu. (aiōn g165)
Mesih, Babamız Tanrı'nın isteğine uyarak bizi şimdiki kötü çağdan kurtarmak için günahlarımıza karşılık kendini feda etti. (aiōn g165)
5 Ulemerero ukhale kwa Mulunguyo mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
Tanrı'ya sonsuzlara dek yücelik olsun! Amin. (aiōn g165)
6 Ine ndikudabwa kuti mukusiya mwamsangamsanga chotere Mulungu amene anakuyitanani mwachisomo cha Khristu ndipo mwatembenuka ndi kutsatira uthenga wina wosiyana,
Sizi Mesih'in lütfuyla çağıranı bırakıp değişik bir müjdeye böylesine çarçabuk dönmenize şaşıyorum.
7 umene si Uthenga Wabwino konse. Pali anthu ena amene akukusokonezani komanso akufuna kupotoza Uthenga Wabwino wa Khristu.
Gerçekte başka bir müjde yoktur. Ancak aklınızı karıştırıp Mesih'in Müjdesi'ni çarpıtmak isteyenler vardır.
8 Ngakhale ife kapena mngelo wochokera kumwamba, akalalikira Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene tinakulalikirani uja, iyeyo akhale wotembereredwa!
İster biz, ister gökten bir melek size bildirdiğimize ters düşen bir müjde bildirirse, lanet olsun ona!
9 Monga tanena kale, tsopano ndikubwereza kunenanso kuti, “Ngati wina aliyense akulalikirani Uthenga Wabwino wosiyana ndi umene munawulandira, iyeyo akhale wotembereredwa.”
Daha önce söylediğimizi şimdi yine söylüyorum: Bir kimse size kabul ettiğinize ters düşen bir müjde bildirirse, ona lanet olsun!
10 Kodi tsopano ndikufuna kukopa anthu kuti andivomereze, kapena Mulungu? Kapena ndikufuna kukondweretsa anthu? Ngati ine ndikanakhala kuti ndikufunabe kukondweretsa anthu, sindikanakhala mtumiki wa Khristu.
Şimdi ben insanların onayını mı, Tanrı'nın onayını mı arıyorum? Yoksa insanları mı hoşnut etmeye çalışıyorum? Eğer hâlâ insanları hoşnut etmek isteseydim, Mesih'in kulu olmazdım.
11 Abale, ine ndikufuna kuti mudziwe, kuti Uthenga Wabwino umene ndinalalikira si ochokera kwa munthu ayi.
Kardeşlerim, yaydığım Müjde'nin insandan kaynaklanmadığını bilmenizi istiyorum.
12 Ine sindinawulandire kuchokera kwa munthu aliyense, kapena kuphunzitsidwa; koma ndinawulandira mwa vumbulutso lochokera kwa Khristu.
Çünkü ben onu insandan almadım, kimseden de öğrenmedim. Bunu bana İsa Mesih vahiy yoluyla açıkladı.
13 Pakuti inu munamva za moyo wanga wakale mʼChiyuda, mmene ndinkazunzira mpingo wa Mulungu koopsa ndi kuyesetsa kuwuwononga.
Yahudi dinine bağlı olduğum zaman nasıl bir yaşam sürdüğümü duydunuz. Tanrı'nın kilisesine alabildiğine zulmediyor, onu kırıp geçiriyordum.
14 Ine ndinkapambana Ayuda ambiri a msinkhu wanga pochita za Chiyuda, ndipo ndinali wachangu koposa pa miyambo ya makolo athu.
Yahudi dininde yaşıtım olan soydaşlarımın birçoğundan daha ilerideydim, atalarımın geleneklerini savunmakta çok daha gayretliydim.
15 Koma Mulungu, amene anandipatula ine ndisanabadwe, ndi kundiyitana mwachisomo chake, atakondweretsedwa
Ama beni daha annemin rahmindeyken seçip lütfuyla çağıran Tanrı, uluslara müjdelemem için Oğlu'nu bana göstermeye razı olunca hemen insanlara danışmadım;
16 kuvumbulutsa Mwana wake mwa ine, kuti ndikalalikire Khristuyo pakati pa anthu a mitundu ina, ine sindinapemphe nzeru kwa munthu aliyense.
17 Ine sindinapite ku Yerusalemu kukaonana ndi amene anali atumwi ine ndisanakhale mtumwi. Mʼmalo mwake nthawi yomweyo ndinapita ku Arabiya ndi kubwereranso ku Damasiko.
Yeruşalim'e, benden önce elçi olanların yanına da gitmedim; Arabistan'a gittim, sonra yine Şam'a döndüm.
18 Pambuyo pake, patatha zaka zitatu, ndinapita ku Yerusalemu kukaonana ndi Petro ndikukhala naye masiku khumi ndi asanu.
Bundan üç yıl sonra Kefas'la tanışmak üzere Yeruşalim'e gittim, on beş gün onun yanında kaldım.
19 Ine sindinaonane ndi atumwi enawo koma Yakobo yekha, mʼbale wa Ambuye.
Öbür elçilerden hiçbirini görmedim, yalnız Rab İsa'nın kardeşi Yakup'u gördüm.
20 Ine ndikutsimikizira inu pamaso pa Mulungu kuti zimene ndikukulemberani si zonama ayi.
Bakın, size yazdıklarımın yalan olmadığını Tanrı'nın önünde belirtiyorum.
21 Pambuyo pake ndinapita ku Siriya ndi ku Kilikiya.
Sonra Suriye ve Kilikya bölgelerine gittim.
22 Koma sindimadziwika ndi nkhope ku mipingo ya ku Yudeya imene ili mwa Khristu.
Yahudiye'nin Mesih'e ait kiliseleri beni şahsen tanımıyorlardı.
23 Iwo anangomva mbiri yokha yakuti, “Munthu amene poyamba anatizunza ife, tsopano akulalikira chikhulupiriro chimene iyeyo nthawi ina anafuna kuchiwononga.”
Yalnız, “Bir zamanlar bize zulmeden adam, önceleri yıkmaya çalıştığı imanı şimdi yayıyor” dendiğini duymuşlardı.
24 Ndipo iwo anayamika Mulungu chifukwa cha ine.
Böylece benden ötürü Tanrı'yı yüceltiyorlardı.

< Agalatiya 1 >