< Ezara 8 >

1 Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:
A ovo su glavari domova otaèkih i pleme onijeh što poðoše sa mnom iz Vavilona za vlade cara Artakserksa:
2 Geresomu wa fuko la Finehasi; Danieli wa fuko la Itamara; Hatusi
Od sinova Finesovijeh Girsom; od sinova Itamarovijeh Danilo; od sinova Davidovijeh Hatus;
3 mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide; Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;
Od sinova Sehanije, koji bješe od sinova Farosovijeh, Zaharija i s njim na broj muškinja sto i pedeset;
4 Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.
Od sinova Fat-Moavovijeh Elioinaj sin Zerajin i s njim muškinja dvjesta;
5 Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.
Od sinova Sehanijinih sin Jasilov i s njim muškinja tri stotine;
6 Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.
I od sinova Adinovijeh Eved sin Jonatanov i s njim muškinja pedeset;
7 Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.
I od sinova Elamovijeh Isaija sin Atalijin i s njim muškinja sedamdeset;
8 Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.
I od sinova Sefatijinih Zevadija sin Mihailov i s njim muškinja osamdeset;
9 Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.
Od sinova Joavovijeh Ovadija sin Jehilov i s njim muškinja dvjesta i osamdeset;
10 Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.
I od sinova Selomitovijeh sin Josifijin i s njim muškinja sto i šezdeset;
11 Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.
I od sinova Vivajevih Zaharija sin Vivajev i s njim muškinja dvadeset i osam;
12 Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.
I od sinova Azgadovijeh Joanan sin Akatanov i s njim muškinja sto i deset;
13 Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.
I od sinova Adonikamovijeh pošljednjih po imenu Elifelet, Jeilo i Semaja i s njima muškinja šezdeset;
14 Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.
I od sinova Vigvajevijeh Gutaj i Zavud, i s njima muškinja sedamdeset.
15 Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi.
I sabrah ih kod rijeke koja teèe u Avu, i ondje stajasmo u okolu tri dana; poslije pregledah narod i sveštenike, ali ne naðoh ondje nijednoga od sinova Levijevih.
16 Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani,
Zato poslah Elijezera, Arila, Semaju i Elnatana i Jariva i Elnatana i Natana i Zahariju i Mesulama glavare, i Jojariva i Elnatana uèitelje,
17 ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu.
I opravih ih k Idu poglavaru u mjestu Kasifiji, i nauèih ih šta æe govoriti Idu i braæi njegovoj Netinejima u mjestu Kasifiji da bi nam doveli sluge za dom Boga našega.
18 Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18.
I dovedoše nam, jer dobra ruka Božija bješe nad nama, èovjeka razumna izmeðu sinova Malija sina Levija sina Izrailjeva, Sereviju sa sinovima njegovijem i braæom njegovom, njih osamnaest;
19 Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri.
I Asaviju i s njim Isaiju od sinova Merarijevih, s braæom njegovom i njihovijem sinovima, njih dvadeset,
20 Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.
I od Netineja, koje odredi David i knezovi da služe Levitima, dvjesta i dvadeset Netineja, koji svi biše imenovani poimence.
21 Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
Tada oglasih ondje na rijeci Avi post, da bismo se ponizili pred Bogom svojim i izmolili u njega sreæan put sebi i djeci svojoj i svemu blagu svojemu.
22 Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.”
Jer me bijaše stid iskati od cara vojske i konjika da nas brane od neprijatelja putem, jer bijasmo rekli caru govoreæi: ruka je Boga našega na dobro nad svima koji ga traže, i jaèina je njegova i gnjev na sve koji ga ostavljaju.
23 Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.
Tako postismo i molismo Boga svojega za to, i umolismo ga.
24 Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi
Tada odvojih izmeðu glavara sveštenièkih dvanaest, Sereviju, Asaviju i s njima desetoricu braæe njihove.
25 ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka.
I izmjerih im srebro i zlato i sudove, priloge domu Boga našega što priloži car i savjetnici njegovi i knezovi njegovi i sav narod Izrailjev koji se naðe;
26 Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide,
Izmjerih im u ruke šest stotina i pedeset talanata srebra, i sudova srebrnijeh sto talanata, i sto talanata zlata,
27 mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.
I dvadeset èaša zlatnijeh od tisuæu drama, i dva suda od mjedi dobre i skupocjene kao zlato.
28 Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu.
I rekoh im: vi ste sveti Gospodu i ovi su sudovi sveti, i ovo srebro i zlato dragovoljan je prilog Gospodu Bogu otaca vaših.
29 Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.”
Pazite i èuvajte dokle ne izmjerite pred glavarima sveštenièkim i Levitima i glavarima otaèkih domova Izrailjevijeh u Jerusalimu u klijetima doma Gospodnjega.
30 Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.
I tako primiše sveštenici i Leviti izmjereno srebro i zlato i sudove da odnesu u Jerusalim u dom Boga našega.
31 Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira.
I poðosmo od rijeke Ave dvanaestoga dana prvoga mjeseca da idemo u Jerusalim, i ruka Boga našega bijaše nad nama i izbavi nas iz ruku neprijateljskih i zasjedaèkih na putu.
32 Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.
I doðosmo u Jerusalim i stajasmo ondje tri dana.
33 Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi.
A èetvrti dan izmjeri se srebro i zlato i sudovi u domu Boga našega u ruke Merimotu sinu Urijinu svešteniku, s kojim bijaše Eleazar sin Finesov, i s njima Jozavad sin Isusov i Noadija sin Venujev, Leviti.
34 Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.
Sve na broj i na mjeru, i mjera bi zapisana od svega u isto vrijeme.
35 Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova.
I koji biše u ropstvu pa se vratiše iz ropstva prinesoše na žrtvu paljenicu Bogu Izrailjevu dvanaest junaca za svega Izrailja, devedeset i šest ovnova, sedamdeset i sedam jaganjaca, dvanaest jaraca za grijeh, sve to na žrtvu paljenicu Gospodu.
36 Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.
I predaše zapovijesti careve namjesnicima carevijem i knezovima s ove strane rijeke, i oni potpomogoše narod i dom Božji.

< Ezara 8 >