< Ezara 8 >

1 Nawa mayina a atsogoleri a mabanja amene anabwera nane kuchokera ku Babuloni nthawi ya ulamuliro wa mfumu Aritasasita:
A oto naczelnicy rodów i rodowody tych, którzy wyruszyli ze mną z Babilonu za panowania króla Artakserksesa:
2 Geresomu wa fuko la Finehasi; Danieli wa fuko la Itamara; Hatusi
Z synów Pinchasa – Gerszom; z synów Itamara – Daniel; z synów Dawida – Chattusz;
3 mwana wa Sekaniya wa fuko la Davide; Zekariya wa fuko la Parosi. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwa anthu ena 150;
Z synów Szekaniasza, z synów Parosza – Zachariasz, a z nim spisanych według rodowodów było stu pięćdziesięciu mężczyzn;
4 Elihunai mwana wa Zerahiya, wa fuko la Pahati-Mowabu. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu ena 400.
Z synów Pachat-Moaba – Elioenaj, syn Zerachiasza, a z nim dwustu mężczyzn;
5 Sekaniya, mwana wa Yahazieli wa fuko la Zatu. Pamodzi ndi iyeyu panalembedwanso anthu 300.
Z synów Szekaniasza – syn Jahaziela, a z nim trzystu mężczyzn;
6 Ebedi, mwana wa Yonatani wa fuko la Adini. Pamodzi naye analembedwanso anthu ena makumi asanu.
Z synów Adina – Ebed, syn Jonatana, a z nim pięćdziesięciu mężczyzn;
7 Yesaiya, mwana wa Ataliya wa fuko la Elamu. Pamodzi naye panali anthu ena 70.
Z synów Elama – Jeszajasz, syn Ataliasza, a z nim siedemdziesięciu mężczyzn;
8 Zebadiya, mwana wa Mikayeli wa fuko la Sefatiya. Pamodzi naye panalinso anthu 80.
Z synów Szefatiasza – Zebadiasz, syn Mikaela, a z nim osiemdziesięciu mężczyzn;
9 Obadiya, mwana wa Yehieli wa fuko la Yowabu. Pamodzi naye panalinso anthu 218.
Z synów Joaba – Obadiasz, syn Jechiela, a z nim dwustu osiemnastu mężczyzn;
10 Selomiti mwana wa Yosifiya wa fuko la Bani. Pamodzi ndi iyeyu panalinso anthu 160.
Z synów Szelomita – syn Josifiasza, a z nim stu sześćdziesięciu mężczyzn;
11 Zekariya, mwana wa Bebai wa fuko la Babai. Pamodzi naye analembedwanso anthu 28.
Z synów Bebaja – Zachariasz, syn Bebaja, a z nim dwudziestu ośmiu mężczyzn;
12 Yohanani, mwana wa Hakatani wa fuko la Azigadi. Pamodzi naye panalinso anthu 110.
Z synów Azgada – Johanan, syn Hakkatana, a z nim stu dziesięciu mężczyzn;
13 Atsogoleri a fuko la Adonikamu, anthu amene anabwera pambuyo pake mayina awo anali Elifeleti, Yeiyeli ndi Semaya. Pamodzi ndi iwowa panalinso anthu 60.
Z synów Adonikama [wyruszyli] ostatni, a oto ich imiona: Elifelet, Jejel i Szemajasz, a z nimi sześćdziesięciu mężczyzn;
14 Atsogoleri a fuko la Bigivai anali Utai ndi Zakuri. Pamodzi ndi iwowa panali anthu 70.
Z synów Bigwaja – Utaj i Zabbud, a z nimi siedemdziesięciu mężczyzn.
15 Anthu onse ndinawasonkhanitsa ku mtsinje umene umapita mpaka ku Ahava, ndipo kumeneko tinagona mʼmisasa masiku atatu. Nditayangʼana pakati pa anthu ndi ansembe, ndinapeza kuti panalibe Alevi.
I zgromadziłem ich nad rzeką, która płynie do Achawy, i obozowaliśmy tam przez trzy dni. Potem dokonałem przeglądu ludu i kapłanów, a z synów Lewiego nie znalazłem tam [żadnego].
16 Choncho ndinayitana atsogoleri awa: Eliezara, Arieli, Semaiya, Elinatani, Yaribu, Elinatani, Natani, Zekariya ndi Mesulamu, pamodzi ndi aphunzitsi awiri, Yoyaribu ndi Elinatani,
Posłałem więc Eliezera, Ariela, Szemajasza, Elnatana, Jariba, Elnatana, Natana, Zachariasza i Meszullama, naczelników, a także Jojariba i Elnatana, [ludzi] rozumnych;
17 ndipo ndinawatuma kwa Ido, mtsogoleri wa malo otchedwa Kasifiya. Ine ndinawawuza zoti akanene kwa Ido ndi kwa abale ake, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ku Kasifiyako, kuti atitumizire anthu odzatumikira ku Nyumba ya Mulungu.
I dałem przez nich polecenie Iddo, przełożonemu w miejscowości Kasifia, i przekazałem im słowa, które mieli powiedzieć do niego i jego braci Netinitów w miejscowości Kasifia; poleciłem, aby nam przyprowadzili sługi dla domu naszego Boga.
18 Chifukwa cha kutikomera mtima kwa Mulungu wathu, Ido anatitumizira munthu wanzeru, Serabiya, wa fuko la Mahili, mwana wa Levi, mwana wa Israeli, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi abale ake, anthu 18.
I ponieważ łaskawa ręka naszego Boga była nad nami, przyprowadzili do nas, człowieka rozumnego spośród synów Machliego, syna Lewiego, syna Izraela, oraz Szerebiasza wraz z jego synami i braćmi – razem osiemnaście [osób];
19 Anatitumiziranso Hasabiya ndi Yesaiya wa fuko la Merari pamodzi ndi abale ake ndi adzukulu ake, anthu makumi awiri.
I Chaszabiasza, a z nim Jeszajasz spośród synów Merariego wraz z jego braćmi i ich synów – razem dwadzieścia [osób];
20 Panalinso anthu ena 220 mwa anthu ogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amene Davide ndi nduna zake anawasankha kuti azitumikira Alevi. Anthu onsewa analembedwa potsata mayina awo.
Ponadto spośród Netinitów, których Dawid i naczelnicy ustanowili do posługiwania Lewitom – dwieście dwadzieścia Netinitów. Ci wszyscy zostali imiennie wyznaczeni.
21 Ku mtsinje wa Ahava, ndinalengeza kuti anthu onse asale zakudya, adzichepetse pamaso pa Mulungu wathu ndi kupempha kuti atiyendetse bwino ife ndi ana athu, ndi kuteteza katundu wathu yense.
Wtedy tam, nad rzeką Achawa, ogłosiłem post, abyśmy ukorzyli się przed naszym Bogiem i abyśmy uprosili u niego szczęśliwą drogę dla nas, naszych dzieci i całego naszego dobytku.
22 Ine ndinali ndi manyazi kupempha mfumu kuti atipatse asilikali oyenda pansi ndi ena okwera pa akavalo kuti atiteteze kwa adani athu pa ulendo wathuwu popeza tinali titawuza kale mfumu kuti “Yehova amateteza aliyense amene amamudalira, koma amakwiyira onse amene amamukana.”
Wstydziłem się bowiem prosić króla o żołnierzy i jeźdźców, aby nas w drodze ratowali przed wrogami, ponieważ powiedzieliśmy królowi: Ręka naszego Boga [jest] nad wszystkimi, którzy go szukają, dla ich dobra, ale jego moc i gniew przeciwko wszystkim, którzy go opuszczają.
23 Choncho tinasala zakudya ndi kupemphera kwa Mulungu wathu kuti atiteteze ndipo Iye anamva pemphero lathu.
Pościliśmy więc i prosiliśmy o to naszego Boga. A on nas wysłuchał.
24 Tsono ndinasankha atsogoleri a ansembe khumi ndi awiri awa, Serebiya, Hasabiya ndi abale awo khumi
Wtedy spośród przedniejszych kapłanów wydzieliłem dwunastu: Szerebiasza, Chaszabiasza, a z nimi dziesięciu ich braci;
25 ndipo ndinawayezera siliva ndi golide, ndiponso ziwiya ndi zopereka za ku Nyumba ya Mulungu wathu zimene mfumu ndi alangizi ake, nduna zake ndi Aisraeli onse amene anali kumeneko anazipereka.
I odważyłem im srebro, złoto i naczynia, czyli ofiarę dla domu naszego Boga, którą złożyli: król, jego doradcy, jego dostojnicy oraz cały Izrael tam obecny.
26 Nditayeza zonse, ndinapereka mʼmanja mwawo, matani 22 asiliva, ziwiya zasiliva zolemera makilogalamu 70, ndiponso makilogalamu 3,400 a golide,
Odważyłem im więc do rąk sześćset pięćdziesiąt talentów srebra, sto talentów naczyń srebrnych, sto talentów złota;
27 mbale zagolide makumi awiri zolemera makilogalamu asanu ndi atatu ndi theka ndiponso ziwiya ziwiri zamkuwa wosalala, wonyezimira bwino ngati golide wamtengowapatali.
Dwadzieścia złotych pucharów, [ważących] po tysiąc darejków, i dwa naczynia z wybornego mosiądzu, tak piękne jak złoto.
28 Kenaka ndinawawuza kuti, “Inu ndi opatulika a Yehova, ndiponso mphatso zonsezi ndi zopatulika. Siliva ndi golideyu ndi zopereka zaufulu kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu.
Potem powiedziałem do nich: Wy jesteście poświęceni PANU, naczynia [także] są poświęcone, a to srebro i złoto [są] dobrowolnym darem dla PANA, Boga waszych ojców.
29 Muzisamale bwino mpaka mutaziyeza pamaso pa atsogoleri a ansembe ndi Alevi ndi akulu a mabanja a Israeli mʼzipinda za mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu.”
Pilnujcie i strzeżcie [ich], dopóki nie odważycie [ich] przed przedniejszymi kapłanami, Lewitami i naczelnikami rodów Izraela w Jerozolimie, w komnatach domu PANA.
30 Choncho ansembe ndi Alevi analandira zonse zoyezedwa zija, siliva, golide pamodzi ndi ziwiya kuti apite nazo ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu.
Wzięli więc kapłani i Lewici odważone srebro, złoto i naczynia, aby [je] zanieść do Jerozolimy, do domu naszego Boga.
31 Pa tsiku la khumi ndi chiwiri la mwezi woyamba, tinachoka ku mtsinje wa Ahava kupita ku Yerusalemu. Ndipo Mulungu wathu anali nafe, ndipo anatiteteza kwa adani athu makamaka otibisalira pa njira.
Potem wyruszyliśmy znad rzeki Achawa dwunastego [dnia] pierwszego miesiąca, aby udać się do Jerozolimy. A ręka naszego Boga była nad nami i wyrwała nas z ręki wrogów i czyhających [na nas] w drodze.
32 Tinafika ku Yerusalemu, komwe tinapumula masiku atatu.
I przybyliśmy do Jerozolimy, i zamieszkaliśmy tam przez trzy dni.
33 Pa tsiku la chinayi lake, mʼNyumba ya Mulungu wathu, tinayeza siliva ndi golide ndi ziwiya zija nʼkuzipereka mʼmanja mwa Meremoti mwana wa wansembe Uriya. Pamodzi ndi iyeyo panali Eliezara mwana wa Finehasi ndiponso Alevi awa: Yozabadi mwana wa Yesuwa ndi Nowadiya mwana wa Binuyi.
A czwartego dnia odważono srebro, złoto i naczynia w domu naszego Boga – do ręki Meremota, syna kapłana Uriasza, z którym był Eleazar, syn Pinchasa; z nimi też [byli] Jozabad, syn Jeszuy, i Noadiasz, syn Binnuja, Lewici;
34 Zonsezi anaziwerenga ndi kuziyeza ndipo analemba kulemera kwa chinthu chilichonse.
Wszystko według liczby i wagi; i zapisano wagę tego wszystkiego w tym czasie.
35 Pamenepo anthu amene anatengedwa ukapolo aja anabwerera, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israeli: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, kuperekera Aisraeli onse, nkhosa zazimuna 96, ana ankhosa 77, ndiponso mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri ngati nsembe yopepesera machimo. Zonsezi zinali nsembe yopsereza zopereka kwa Yehova.
Następnie ci, którzy zostali pojmani, a powrócili z niewoli, złożyli Bogu Izraela ofiarę całopalną: dwanaście cielców za całego Izraela, dziewięćdziesiąt sześć baranów, siedemdziesiąt siedem jagniąt i dwanaście kozłów na ofiarę za grzech, wszystko jako całopalenie PANU.
36 Iwo anaperekanso chidziwitso cha mfumu chija kwa akuluakulu a mfumu ndi kwa akazembe a mʼdera la Patsidya pa Yufurate. Pamenepo iwo anathandiza Ayuda ndiponso ntchito za pa Nyumba ya Mulungu.
I przekazano rozporządzenie króla jego satrapom i namiestnikom zarzecza, a ci wspomagali lud i dom Boży.

< Ezara 8 >