< Ezara 4 >

1 Adani a Yuda ndi Benjamini anamva kuti anthu obwera ku ukapolo aja akumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli.
A gdy wrogowie Judy i Beniamina usłyszeli, że lud, [który powrócił] z niewoli, budował świątynię PANU, Bogu Izraela;
2 Tsono anapita kwa Zerubabeli ndi kwa atsogoleri a mabanja awo ndi kunena kuti, “Mutilole kuti tikuthandizeni kumangaku chifukwa ife timapembedza Mulungu wanu monga momwe mumachitira inu, ndipo takhala tikupereka nsembe kwa Iye kuyambira nthawi ya Esrahadoni, mfumu ya ku Asiriya, amene anabwera nafe kuno.”
Wówczas przybyli do Zorobabela i naczelników rodów i powiedzieli im: Będziemy budować z wami, gdyż szukamy waszego Boga tak jak wy i składamy mu ofiary od czasów Asarchaddona, króla Asyrii, który nas tu przyprowadził.
3 Koma Zerubabeli, Yesuwa ndi atsogoleri ena otsala a mabanja a Aisraeli anayankha kuti, “Inu simungatithandize kumangira Nyumba Yehova, Mulungu wathu. Tokha tidzamumangira Nyumba Yehova, Mulungu wa Aisraeli, monga mfumu Koresi, mfumu ya Perisiya inatilamulira.”
Ale Zorobabel, Jeszua i pozostali naczelnicy rodów z Izraela odpowiedzieli im: Nie wolno wam razem z nami budować domu naszemu Bogu, ale my sami będziemy budować PANU, Bogu Izraela, jak nam rozkazał Cyrus, król Persji.
4 Tsono anthu a mʼdzikomo anayamba kuchititsa ulesi anthu a ku Yuda, ndi kuwachititsa mantha kuti aleke ntchito yomangayo.
Wtedy lud tej ziemi zaczął zniechęcać lud Judy i przeszkadzał im w budowie.
5 Analemba alangizi ena kuti alepheretse cholinga chawo pa ntchitoyo pa nthawi yonse ya Koresi, mfumu ya ku Perisiya, ndiponso mpaka pamene Dariyo mfumu ya ku Perisiya ankalamulira dzikolo.
Ponadto przekupywał przeciwko nim radców, aby udaremnić ich zamiar po wszystkie dni Cyrusa, króla Persji, aż do panowania Dariusza, króla Persji.
6 Mfumu Ahasiwero atangoyamba kulamulira dzikolo, adani aja analemba kalata yoneneza anthu a Yuda ndi Yerusalemu.
Za panowania Aswerusa, na początku jego panowania, napisali skargę przeciwko obywatelom Judy i Jerozolimy;
7 Ndiponso mʼnthawi ya Aritasasita mfumu ya Perisiya, Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli ndi anzawo ena analemba kalata inanso kwa Aritasasita. Kalatayo inalembedwa mʼChiaramu ndipo ankatanthauzira poyiwerenga.
A za czasów Artakserksesa Biszlam, Mitredat, Tabeel wraz z pozostałymi towarzyszami napisali do Artakserksesa, króla Persji. List [był] sporządzony pismem syryjskim i przetłumaczony na język syryjski.
8 Rehumu mkulu wankhondo ndi Simisai mlembi, nawonso analemba kalata yawo yoneneza anthu a ku Yerusalemu kwa mfumu Aritasasita. Anayilemba motere:
Kanclerz Rechum i pisarz Szimszaj napisali do króla Artakserksesa list przeciwko Jerozolimie następującej treści:
9 Kalata yochokera kwa Rehumu, mkulu wa gulu lankhondo, mlembi Simisai ndi anzawo awa: oweruza, nduna, akuluakulu ena, anthu a ku Peresiya, Ereki, Babuloni, Susa mʼdziko la Elamu,
Kanclerz Rechum, pisarz Szimszaj i pozostali ich towarzysze: Dynajczycy, Afarsadchajczycy, Tarpelajczycy, Afarsajczycy, Arkewijczycy, Babilończycy, Susanchici, Dehawici [i] Elamici;
10 ndi mitundu ina imene mkulu wolemekezeka, Osanipara anayisamutsa ndi kuyikhazika mʼmizinda ya Samariya ndi mʼmadera ena apatsidya la Yufurate.
I reszta narodów, które wielki i sławny Asnappar przyprowadził i osiedlił w miastach Samarii, oraz pozostali, którzy są za rzeką – otóż;
11 Mawu a mʼkalata ya kwa Aritasasita anali awa: Kwa mfumu Aritasasita: Kuchokera kwa atumiki anu, anthu a kutsidya kwa Yufurate:
To [jest] odpis listu, który posłali do króla Artakserksesa – Twoi słudzy, ludzie mieszkający za rzeką – otóż:
12 Amfumu tati mudziwe kuti Ayuda amene anabwera kuno kuchokera kwanuko apita ku Yerusalemu ndipo akumanganso mzinda wa anthu owukira ndi oyipa uja. Akumaliza makoma ake ndipo akukonzanso maziko.
Niech królowi będzie wiadomo, że Żydzi, którzy wyszli od ciebie, przybyli do nas, do Jerozolimy, i odbudowują to buntownicze i niegodziwe miasto, już wznosili mury i położyli fundamenty.
13 Kuwonjeza apo amfumu mudziwe kuti ngati amalize kumanganso mzindawu ndi kukonzanso makoma ake, adzaleka kukhoma msonkho, kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko kapena msonkho wina uliwonse, ndipo chuma cha thumba la ufumu chidzachepa.
Niech więc będzie królowi wiadomo, że jeśli to miasto zostanie odbudowane i [jego] mury będą wzniesione, wtedy podatku, danin ani cła oni nie będą płacić, a to przyniesie szkodę dochodom króla.
14 Popeza tsono ife timadya nawo kwa mfumu sitiyenera tizingoonerera zinthu zochititsa mfumu manyazi. Nʼchifukwa chake tikutumiza uthenga kwa inu a mfumu kuti mudziwe zonse.
Teraz więc, ponieważ jesteśmy na utrzymaniu [twego] pałacu i nie przystoi nam patrzeć na zniewagę króla, posyłamy królowi tę wiadomość;
15 Choncho pachitike kafukufuku mʼbuku la mbiri yakale ya makolo anu. Mʼbuku la mbiri zakale mudzapezamo ndi kuwerenga kuti mzinda umenewu ndi waupandu, wosautsa mafumu ndi nduna zamʼmadera zomwe. Kuyambira kale wakhala ukuwukira ulamuliro uliwonse. Nʼchifukwa chake mzinda umenewu anawuwononga.
Aby poszukano w księdze kronik twoich ojców, a znajdziesz w niej i dowiesz się, że to miasto jest miastem buntowniczym i przynosi szkodę królom i prowincjom i że od dawien dawna wzniecano w nim bunty. Z tego powodu to miasto zostało zburzone.
16 Tsono tikukudziwitsani amfumu kuti ngati mzinda umenewu umangidwanso ndi makoma ake nʼkutsirizidwanso ndiye kuti inu simudzalamuliranso chigawo cha patsidya pa Yufurate.
Zawiadamiamy króla, że jeśli to miasto zostanie odbudowane i jego mury będą wzniesione, wtedy już nie będziesz miał udziału za rzeką.
17 Mfumu inatumiza yankho ili: Mkulu wa gulu lankhondo Rehumu, mlembi Simisai ndi anzanu onse amene akukhala ku Samariya ndi mʼzigawo zina zonse za Patsidya pa Yufurate. Landirani moni.
[Wtedy] król wysłał taką odpowiedź: Kanclerzowi Rechumowi, pisarzowi Szimszajowi i pozostałym ich towarzyszom, którzy mieszkają w Samarii, a także i pozostałym za rzeką: Pokój! Otóż:
18 Kalata imene munatumiza ija yawerengedwa bwino lomwe pamaso panga.
List, który do nas przysłaliście, został przede mną dokładnie odczytany.
19 Ine nditalamula kuti afufuze nkhaniyi kwapezekadi kuti mzinda umenewu uli ndi mbiri yowukira mafumu ndi kuti zaupandu ndi zowukira zinkachitikadi mʼmenemo.
Dlatego rozkazałem, aby poszukano. I znaleziono, że to miasto od dawna powstawało przeciwko królom, a bunt i rozruchy były w nim wzniecane;
20 Mafumu amphamvu akhala akulamulira Yerusalemu ndi chigawo chonse cha Patsidya pa Yufurate. Iwo ankalandira msonkho ndi kulipira ndalama zakatundu olowa mʼdziko pa kanthu kena kalikonse.
Ponadto potężni królowie panowali nad Jerozolimą i rządzili nad wszystkimi za rzeką, i płacono im podatek, daninę i cło.
21 Tsopano inu khazikitsani lamulo kuti anthu amenewo asiye ntchitoyo, asamangenso mzindawo mpaka ine nditalamula
Wydajcie więc wyrok, aby powstrzymać tych mężczyzn, żeby to miasto nie zostało odbudowane, dopóki [inny] rozkaz nie będzie przeze mnie wydany.
22 Musachedwe kuchita zimenezi. Kodi ine ndingalole bwanji kuti zowononga zotere zikule ndi kupweteka ine mfumu?
Pilnujcie, abyście nie zaniedbali tego. Dlaczego miałoby to wzrastać na szkodę królów?
23 Kalata ya mfumu Aritasasitayi itangowerengedwa pamaso pa Rehumu ndi Simisai mlembi uja, ndi anzawo onse, iwo anapita msangamsanga ku Yerusalemu kukawaletsa Ayuda aja mwamphamvu kuti asapitirire ntchito yawo.
Gdy więc odpis listu króla Artakserksesa został odczytany przed Rechumem, pisarzem Szimszajem i ich towarzyszami, udali się spiesznie do Żydów w Jerozolimie i siłą i mocą wstrzymali budowę.
24 Motero ntchito yomanga Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu inayimitsidwa mpaka chaka cha chiwiri cha ulamuliro wa Dariyo mfumu ya ku Perisiya.
W ten sposób ustała praca przy domu Bożym, który był w Jerozolimie. I została wstrzymana aż do drugiego roku panowania Dariusza, króla Persji.

< Ezara 4 >