< Ezara 1 >

1 Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
In the firste yeer of Cirus, kyng of Persis, that the word of the Lord bi the mouth of Jeremye schulde be fillid, the Lord reiside the spirit of Cyrus, kyng of Persis; and he pupplischide a vois in al his rewme, ye, bi the scripture, and seide, Cirus,
2 Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
the kyng of Persis, seith these thingis, The Lord God of heuene yaf to me alle the rewmes of erthe, and he comaundide to me, that Y schulde bilde to hym an hows in Jerusalem, which is in Judee.
3 Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
Who is among you of al his puple? his God be with hym; stie he in to Jerusalem, which is in Judee, and bilde he the hows of the Lord God of Israel; he is God, which is in Jerusalem.
4 Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
And alle othere men, `that dwellen where euere in alle places, helpe hym; the men of her place helpe in siluer, and gold, and catel, and scheep, outakun that that thei offren wilfulli to the temple of God, which is in Jerusalem.
5 Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
And the princis of fadris of Juda and of Beniamyn risiden, and the preestis, and dekenes, and ech man whos spirit God reiside, for to stie to bilde the temple of the Lord, that was in Jerusalem.
6 Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
And alle men that weren `in cumpas helpiden the hondis of hem, in vesselis of siluer, and of gold, `in catel, in purtenaunce of houshold, and in alle werk beestis, outakun these thingis which thei offriden bi fre wille.
7 Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
Forsothe kyng Cyrus brouyte forth the vessels of the temple of the Lord, whiche Nabugodonosor hadde take fro Jerusalem, and hadde set tho in the temple of his god.
8 Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
Sotheli Cyrus, the kyng of Persis, brouyte forth tho bi the hond of Mytridatis, sone of Gazabar; and noumbride tho to Sasabazar, the prince of Juda.
9 Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
And this is the noumbre of tho vessels; goldun violis, thritti; siluerne viols, a thousynde; `grete knyues, nyne and twenti; goldun cuppis, thritti; siluerne cuppis,
10 timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
two thousynde foure hundrid and ten; othere vessels, a thousynde;
11 Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.
alle the vessels of gold and siluere weren fyue thousynde foure hundrid. Sasabazar took alle vessels, with hem that stieden fro the transmygracioun of Babiloyne, in to Jerusalem.

< Ezara 1 >